< Song of Solomon 1 >
1 The Song of Songs, which is Solomon's.
Nyimbo ya Solomoni, nyimbo yoposa nyimbo zonse.
2 Oh, that he would kiss me with the kisses of his mouth, The woman speaking to the man for your love is better than wine.
Undipsompsone ndi milomo yako chifukwa chikondi chako nʼchokoma kuposa vinyo.
3 Your anointing oils have a delightful fragrance; your name is like flowing perfume, so the young women love you.
Mafuta ako odzola ndi onunkhira bwino; dzina lako lili ngati mafuta onunkhira otsanulidwa. Nʼchifukwa chake atsikana amakukonda!
4 Take me with you, and we will run. The woman speaking to herself The king has brought me into his rooms. The woman speaking to the man We are glad; We rejoice about you; let us celebrate your love; it is better than wine. It is natural for the other women to adore you.
Nditenge ndipo ndizikutsata, tiye tifulumire! Mfumu indilowetse mʼchipinda chake. Abwenzi Ife timasangalala ndi kukondwera nawe, tidzatamanda chikondi chako kupambana vinyo. Mkazi Amachita bwinotu potamanda iwe!
5 I am dark but lovely, you daughters of Jerusalem— dark like the tents of Kedar, lovely like the curtains of Solomon.
Ndine wakuda, komatu ndine wokongola, inu akazi a ku Yerusalemu, ine ndine wakuda ngati tenti ya ku Kedara, ngati makatani a tenti ya Solomoni.
6 Do not stare at me because I am dark, because the sun has scorched me. My mother's sons were angry with me; they made me keeper of the vineyards, but my own vineyard I have not kept.
Musandiyangʼane monyoza chifukwa ndine wakuda, ndine wakuda chifukwa cha dzuwa. Alongo anga anandikwiyira ndipo anandigwiritsa ntchito mʼminda ya mpesa; munda wangawanga sindinawusamalire.
7 Tell me, you whom my soul loves, where do you feed your flock? Where do you rest your flock at noontime? Why should I be like someone who wanders beside the flocks of your companions?
Ndiwuze iwe, amene ndimakukonda, kumene umadyetsa ziweto zako ndi kumene umagoneka nkhosa zako nthawi yamasana. Ndikhalirenji ngati mkazi wachiwerewere pambali pa ziweto za abwenzi ako?
8 If you do not know, most beautiful among women, follow the tracks of my flock, and pasture your young goats near the shepherds' tents.
Ngati sukudziwa iwe wokongola kwambiri kuposa akazi ena, ngati sukudziwa, tsatira makwalala a nkhosa ndipo udyetse ana ambuzi pambali pa matenti a abusa.
9 I compare you, my love, to a mare among Pharaoh's chariot horses.
Iwe bwenzi langa, uli ngati kavalo wamkazi ku magaleta a Farao.
10 Your cheeks are beautiful with ornaments, your neck with strings of jewels.
Masaya ako ndi okongola ndi ndolo zamʼmakutuzo, khosi lako likukongola ndi mikanda yamiyala yamtengowapatali.
11 We will make for you gold ornaments with silver studs.
Tidzakupangira ndolo zagolide zokongoletsedwa ndi mikanda yasiliva.
12 While the king lay on his couch, my nard emitted its fragrance.
Pamene mfumu inali pa malo ake odyera, mafuta anga onunkhira anamveka fungo lake.
13 My beloved is to me like a bag of myrrh that spends the night lying between my breasts.
Wokondedwa wanga ali ngati kathumba ka mure kwa ine, kamene kamakhala pakati pa mawere angawa.
14 My beloved is to me like a cluster of henna flowers in the vineyards of En Gedi.
Wokondedwa wanga ali ngati mpukutu wa maluwa ofiira, ochokera ku minda ya mpesa ya ku Eni-Gedi.
15 Listen, you are beautiful, my love; listen, you are beautiful; your eyes are doves.
Iwe wokondedwa wanga, ndiwe wokongoladi! Ndithu, ndiwe chiphadzuwa, maso ako ali ngati nkhunda.
16 Listen, you are handsome, my beloved, how handsome. The lush plants are our bed.
Iwe bwenzi langa, ndiwe wokongoladi! Ndithu, ndiwe wokongoladi kwambiri! Ndipo malo athu ogonapo ndi msipu wobiriwira.
17 The beams of our house are cedars; our rafters are firs.
Mitanda ya nyumba yathu ndi ya mkungudza, phaso lake ndi la mtengo wa payini.