< Song of Solomon 7 >
1 How beautiful your feet appear in your sandals, prince's daughter! The curves of your thighs are like jewels, the work of the hands of a master craftsman.
Iwe namwali waufumu, mapazi ako ngokongola mu nsapato wavalazo! Ntchafu zako nʼzowumbika bwino ngati miyala yamtengowapatali, ntchito ya manja ya mmisiri waluso.
2 Your navel is like a round bowl; may it never lack mixed wine. Your belly is like a mound of wheat encircled with lilies.
Mchombo wako uli ngati chikho chowumbika bwino chimene nthawi zonse ndi chodzaza ndi vinyo. Chiwuno chako ndi choningʼa ngati mtolo wa tirigu utazunguliridwa ndi maluwa okongola.
3 Your two breasts are like two fawns, twins of a gazelle.
Mawere ako akuoneka ngati ana awiri a mbawala, ngati mphoyo zamapasa.
4 Your neck is like a tower of ivory; your eyes are the pools in Heshbon by the gate of Bath Rabbim. Your nose is like the tower in Lebanon that looks toward Damascus.
Khosi lako lili see! ngati nsanja ya mnyanga wa njovu. Maso ako ali ngati mayiwe a ku Hesiboni, amene ali pafupi ndi chipata cha Bati Rabimu. Mphuno yako ili ngati nsanja ya ku Lebanoni, yoyangʼana ku Damasiko.
5 Your head is on you like Carmel; the hair on your head is dark purple. The king is held captive by its tresses.
Mutu wako uli bwinobwino nengʼaa ngati phiri la Karimeli. Tsitsi lako lili ngati nsalu yakuda yaufumu; mfumu yakopeka ndi maonekedwe ake okongola.
6 How beautiful and how lovely you are, my love, with delights!
Ndiwe wokongola kwambiri ndiponso wosangalatsa, iwe wokondedwa, namwali wokondweretsawe!
7 Your height is like that of a date palm tree, and your breasts like clusters of fruit.
Msinkhu wako uli ngati mtengo wa mgwalangwa, ndipo mawere ako ali ngati phava la zipatso.
8 I said, “I want to climb that palm tree; I will take hold of its branches.” May your breasts be like clusters of grapes, and may the fragrance of your nose be like apricots.
Ndinati, “Ndikwera mtengo wa mgwalangwa; ndidzathyola zipatso zake.” Mawere ako ali ngati maphava a mphesa, fungo la mpweya wako lili ngati ma apulosi,
9 May your palate be like the best wine, flowing smoothly for my beloved, gliding over the lips of those who sleep.
ndipo pakamwa pako pali ngati vinyo wokoma kwambiri. Mkazi Tsono vinyo ameneyu amuthirire wachikondi wanga, ayenderere bwino pa milomo yake ndi mano ake.
10 I am my beloved's, and he desires me.
Wokondedwayo ine ndine wake, ndipo chilakolako chake chili pa ine.
11 Come, my beloved, let us go out into the countryside; let us spend the night in the villages.
Bwera wachikondi wanga, tiye tipite ku madera a ku midzi, tikagone ku midzi.
12 Let us rise early to go to the vineyards; let us see whether the vines have budded, whether their blossoms have opened, and whether the pomegranates are in flower. There I will give you my love.
Tiye tilawirire mmamawa kupita ku minda ya mpesa, tikaone ngati mitengo ya mpesa yayamba kuphukira, ngati maluwa ake ayamba kuoneka, komanso ngati makangadza ayamba kuonetsa maluwa. Kumeneko ndidzakuonetsa chikondi changa.
13 The mandrakes give off their fragrance; at the door where we are staying are all sorts of choice fruits, new and old, that I have stored up for you, my beloved.
Mitengo ya mankhwala a chisulo ikupereka fungo lake labwino, ndipo pa khomo pathu pali zipatso zonse zokoma, zatsopano ndi zakale zomwe, zimene ndakusungira wokondedwa wanga.