< Song of Solomon 5 >

1 I have come into my garden, my sister, my bride; I have gathered my myrrh with my spice. I have eaten my honeycomb with my honey; I have drunk my wine with my milk. The friends speaking to the man and the woman Eat, friends; drink and be drunk with love.
Ndalowa mʼmunda mwanga, iwe mlongo wanga, iwe mkwatibwi wanga; ndasonkhanitsa mure wanga ndi zokometsera zakudya zanga. Ndadya uchi wanga pamodzi ndi zisa zake zomwe; ndamwa vinyo wanga ndi mkaka wanga. Abwenzi Idyani abwenzi anga, imwani; Inu okondana, imwani kwambiri.
2 I was asleep, but my heart was awake. There is the sound of my beloved knocking and saying, “Open to me, my sister, my love, my dove, my undefiled one, for my head is wet with dew, my hair with the night's dampness.”
Ndinagona tulo koma mtima wanga unali maso. Tamverani, bwenzi langa akugogoda: “Nditsekulire, mlongo wanga, bwenzi langa, nkhunda yanga, wangwiro wanga. Mutu wanga wanyowa ndi mame, tsitsi langa lanyowa chifukwa cha nkhungu ya usiku.”
3 “I have taken off my robe; must I put it on again? I have washed my feet; must I get them dirty?”
Ndavula kale zovala zanga, kodi ndizivalenso? Ndasamba kale mapazi anga kodi ndiwadetsenso?
4 My beloved put in his hand through the opening of the door latch, and my heart was stirred up for him.
Bwenzi langa anapisa dzanja lake pa chibowo cha pa chitseko; mtima wanga unagunda chifukwa cha iye.
5 I got up to open the door for my beloved; my hands were dripping with myrrh, my fingers with moist myrrh, on the door handle.
Ndinanyamuka kukamutsekulira wachikondi wangayo, ndipo manja anga anali noninoni ndi mure, zala zanga zinali mure chuchuchu, pa zogwirira za chotsekera.
6 I opened the door for my beloved, but my beloved had turned and gone. My heart sank when he spoke. I looked for him, but I did not find him; I called him, but he did not answer me.
Ndinamutsekulira wachikondi wanga, koma nʼkuti wachikondi wangayo atachoka; iye anali atapita. Mtima wanga unafumuka chifukwa cha kuchoka kwake. Ndinamuyangʼanayangʼana koma sindinamupeze. Ndinamuyitana koma sanandiyankhe.
7 The watchmen found me as they were making their rounds in the city. They struck me and wounded me; the guards on the walls took away my cloak from me.
Alonda anandipeza pamene ankayendera mzindawo. Anandimenya ndipo anandipweteka; iwo anandilanda mwinjiro wanga, alonda a pa khoma aja!
8 I want you to swear, daughters of Jerusalem, that if you find my beloved— What will you make known to him?— that I am sick from love.
Inu akazi a ku Yerusalemu ndithu ndikukupemphani, mukapeza wokondedwa wangayo, kodi mudzamuwuza chiyani? Muwuzeni kuti ine ndadwala nacho chikondi.
9 How is your beloved better than another beloved man, most beautiful among women? Why is your beloved better than another beloved, that you ask us to take an oath like this?
Iwe wokongola kuposa akazi onsewa, kodi wokondedwa wakoyo ndi wopambana wina aliyense bwanji? Kodi wokondedwa wakoyo ndi wopambana ena onse chotani kuti uzichita kutipempha motere?
10 My beloved is radiant and ruddy, outstanding among ten thousand.
Wokondedwa wangayo ndi wowala kwambiri ndi wathanzi pakati pa anthu 1,000.
11 His head is the purest gold; his hair is curly and as black as a raven.
Mutu wake ndi golide woyengeka bwino; tsitsi lake ndi lopotanapotana, ndiponso lakuda bwino ngati khwangwala.
12 His eyes are like doves beside streams of water, bathed in milk, mounted like jewels.
Maso ake ali ngati nkhunda mʼmbali mwa mitsinje ya madzi, ngati nkhunda zitasamba mu mkaka, zitayima ngati miyala yamtengowapatali.
13 His cheeks are like beds of spices, yielding aromatic scents. His lips are lilies, dripping liquid myrrh.
Masaya ake ali ngati timinda ta mbewu zokometsera zakudya zopatsa fungo lokoma. Milomo yake ili ngati maluwa okongola amene akuchucha mure.
14 His arms are rounded gold set with jewels; his abdomen is ivory covered with sapphires.
Manja ake ali ngati ndodo zagolide zokongoletsedwa ndi miyala yamtengowapatali. Thupi lake ndi losalala ngati mnyanga wanjovu woyikamo miyala ya safiro.
15 His legs are pillars of marble, set on bases of pure gold; his appearance is like Lebanon, choice as the cedars.
Miyendo yake ili ngati mizati yamwala, yokhazikika pa maziko a golide. Maonekedwe ake ali ngati Lebanoni, abwino kwambiri ngati mkungudza.
16 His mouth is most sweet; he is completely lovely. This is my beloved, and this is my friend, daughters of Jerusalem.
Milomo yake ndi yosangalatsa kwambiri; munthuyo ndi wokongola kwambiri! Uyu ndiye wachikondi wanga ndi bwenzi langa, inu akazi a ku Yerusalemu.

< Song of Solomon 5 >