< Psalms 92 >
1 A psalm, a song for the Sabbath day. It is a good thing to give thanks to Yahweh and to sing praises to your name, Most High,
Salimo. Nyimbo ya pa tsiku la Sabata. Nʼkwabwino kutamanda Yehova ndi kuyimbira nyimbo dzina lanu, Inu Wammwambamwamba,
2 to proclaim your covenant faithfulness in the morning and your truthfulness every night,
Kulengeza chikondi chanu mmawa, ndi kukhulupirika kwanu nthawi ya usiku,
3 with a harp of ten strings and with the melody of the lyre.
kuyimbira nyimbo choyimbira cha zingwe khumi ndi mayimbidwe abwino a zeze.
4 For you, Yahweh, have made me glad through your deeds. I will sing for joy because of the deeds of your hands.
Pakuti Inu mumandisangalatsa ndi ntchito zanu, Inu Yehova; Ine ndikuyimba mwachimwemwe pa ntchito ya manja anu.
5 How great are your deeds, Yahweh! Your thoughts are very deep.
Ndi yayikuludi ntchito yanu Yehova, maganizo anu ndi ozamadi!
6 A brutish person does not know, nor does a fool understand this:
Munthu wopanda nzeru sadziwa, zitsiru sizizindikira,
7 When the wicked sprout like the grass, and even when all the evildoers thrive, still they are doomed to eternal destruction.
kuti ngakhale anthu oyipa aphuka ngati udzu ndipo anthu onse ochita zoyipa apindula, adzawonongedwa kwamuyaya.
8 But you, Yahweh, will reign forever.
Koma Inu Yehova, ndinu wokwezedwa kwamuyaya.
9 Indeed, look at your enemies, Yahweh! Indeed, look at your enemies. They will perish! All those who do evil will be scattered.
Zoonadi adani anu Yehova, zoonadi adani anu adzawonongeka; onse ochita zoyipa adzabalalitsidwa.
10 You have lifted up my horn like the horn of the wild ox; I am anointed with fresh oil.
Inu mwakweza nyanga yanga ngati nyanga ya njati; mafuta abwino akhuthulidwa pamutu wanga.
11 My eyes have seen the downfall of my enemies; my ears have heard of the doom of my evil foes.
Maso anga aona kugonjetsedwa kwa olimbana nane, makutu anga amva za kugwa kwa amaliwongo anga oyipa.
12 The righteous will flourish like the palm tree; they will grow like a cedar in Lebanon.
Anthu olungama adzaphuka ngati mtengo wa mgwalangwa, adzakula ngati mkungudza wa ku Lebanoni;
13 They are planted in the house of Yahweh; they flourish in the courts of our God.
odzalidwa mʼnyumba ya Yehova, adzakula bwino mʼmabwalo a Mulungu wathu.
14 They bear fruit even when they are old; they stay fresh and green,
Iwo adzaberekabe zipatso mu ukalamba wawo, adzakhala anthete ndi obiriwira,
15 to proclaim that Yahweh is just. He is my rock, and there is no unrighteousness in him.
kulengeza kuti, “Yehova ndi wolungama; Iye ndiye Thanthwe langa, ndipo mwa Iye mulibe choyipa.”