< Psalms 88 >

1 A song, a psalm of the sons of Korah; for the chief musician; set to the Mahalath Leannoth style. A maschil of Heman the Ezrahite. Yahweh, God of my salvation, I cry out day and night before you.
Salimo la ana a Kora. Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a nyimbo yoti: “Pa Matenda ndi pa Mazunzo.” Ndakatulo ya Hemani, wa banja la Ezara. Inu Yehova, Mulungu amene mumandipulumutsa, usana ndi usiku ndimalira pamaso panu.
2 Listen to my prayer; pay attention to my cry.
Pemphero langa lifike pamaso panu; tcherani khutu lanu kuti mumve kulira kwanga.
3 For I am filled with troubles, and my life has reached Sheol. (Sheol h7585)
Pakuti ndili ndi mavuto ambiri ndipo moyo wanga ukuyandikira ku manda. (Sheol h7585)
4 People treat me like those who go down into the pit; I am a man with no strength.
Ndikuwerengedwa pamodzi ndi iwo amene akutsikira ku dzenje; ndine munthu wopanda mphamvu.
5 I am abandoned among the dead; I am like the dead who lie in the grave, about whom you care no more because they are cut off from your power.
Ndayikidwa pambali pamodzi ndi anthu akufa, monga ophedwa amene agona mʼmanda, amene Inu simuwakumbukiranso, amene achotsedwa pa chisamaliro chanu.
6 You place me in the lowest part of the pit, in the dark and deep places.
Mwandiyika pansi pa dzenje penipeni, mʼmalo akuya a mdima waukulu.
7 Your wrath lies heavy on me, and all your waves crash over me. (Selah)
Ukali wanu ukundipsinja kwambiri, mwandiopseza kwambiri ndi mafunde anu onse. (Sela)
8 Because of you, my acquaintances avoid me. You have made me a shocking sight to them. I am hemmed in and I cannot escape.
Mwandichotsa pakati pa abwenzi anga enieni ndipo mwachititsa kuti ndikhale chonyansa kwa iwo. Ndatsekerezedwa ndipo sindingathe kuthawa;
9 My eyes grow weary from trouble; All day long I call out to you, Yahweh; I spread out my hands to you.
maso anga ada ndi chisoni. Ndimayitana Inu Yehova tsiku lililonse; ndimakweza manja anga kwa Inu.
10 Will you do wonders for the dead? Will those who have died rise and praise you? (Selah)
Kodi mumaonetsa zozizwitsa zanu kwa anthu akufa? Kodi iwo amene afa amaukanso ndi kutamanda Inu? (Sela)
11 Will your covenant faithfulness be proclaimed in the grave, your loyalty in the place of the dead?
Kodi chikondi chanu chimalalikidwa mʼmanda, za kukhulupirika kwanu ku malo a chiwonongeko?
12 Will your wonderful deeds be known in the darkness, or your righteousness in the place of forgetfulness?
Kodi zozizwitsa zanu zimadziwika ku malo a mdima, kapena ntchito zanu zolungama ku dziko la anthu oyiwalika?
13 But I cry to you, Yahweh; in the morning my prayer comes before you.
Inu Yehova, Ine ndimalirira thandizo; mmawa mapemphero anga amafika pamaso panu.
14 Yahweh, why do you reject me? Why do you hide your face from me?
Inu Yehova nʼchifukwa chiyani mukundikana ndi kundibisira nkhope yanu?
15 I have always been afflicted and on the verge of death since my youth. I have suffered from your terrors; I am in despair.
Kuyambira ubwana wanga ndakhala ndikuzunzika pafupi kufa; ndakhala ndikuchita mantha ndipo ndine wothedwa nzeru.
16 Your angry actions have passed over me, and your terrifying deeds have annihilated me.
Ukali wanu wandimiza; zoopsa zanu zandiwononga.
17 They surround me like water all the day long; they have all encircled me.
Tsiku lonse zimandizungulira ngati chigumula; zandimiza kwathunthu.
18 You have removed every friend and acquaintance from me. My only acquaintance is the darkness.
Inu mwatenga anzanga ndi okondedwa anga kuwachotsa pamaso panga; mdima ndiye bwenzi langa lenileni.

< Psalms 88 >