< Psalms 85 >

1 For the chief musician. A psalm of the sons of Korah. Yahweh, you have showed favor to your land; you have restored the well-being of Jacob.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la ana a Kora. Yehova munakomera mtima dziko lanu; munabwezeretsa ulemerero wa Yakobo.
2 You have forgiven the sin of your people; you have covered all their sin. (Selah)
Munakhululukira mphulupulu za anthu anu ndi kuphimba machimo awo onse. (Sela)
3 You have withdrawn all your wrath; you have turned back from your hot anger.
Munayika pambali ukali wanu wonse ndi kutembenuka kuchoka ku mkwiyo wanu woopsa.
4 Restore us, God of our salvation, and let go of your displeasure with us.
Tibwezeretseninso mwakale Inu Mulungu Mpulumutsi wathu, ndipo mutichotsere mkwiyo wanu.
5 Will you be angry with us forever? Will you remain angry throughout future generations?
Kodi mudzatikwiyira mpaka liti? Kodi mudzapitiriza kukwiya pa mibado yathu yonse?
6 Will you not revive us again? Then your people will rejoice in you.
Kodi simudzatitsitsimutsanso, kuti anthu anu asangalale mwa Inu?
7 Show us your covenant faithfulness, Yahweh, grant us your salvation.
Tionetseni chikondi chanu chosatha, Inu Yehova, ndipo tipatseni chipulumutso chanu.
8 I will listen to what Yahweh God says, for he will make peace with his people, his faithful followers. Yet they must not turn again to foolish ways.
Ndidzamvetsera zimene Yehova Mulungu adzanena; Iye amalonjeza mtendere kwa anthu ake, oyera mtima ake, koma musawalole kuti abwerere ku zopusa.
9 Surely his salvation is near to those who fear him; then glory will remain in our land.
Ndithu chipulumutso chake chili pafupi ndi iwo amene amaopa Iye, kuti ulemerero wake ukhale mʼdziko lathu.
10 Covenant faithfulness and trustworthiness have met together; righteousness and peace have kissed each other.
Chikondi ndi kukhulupirika zimakumana pamodzi; chilungamo ndi mtendere zimapsompsonana.
11 Trustworthiness springs up from the ground, and righteousness looks down from the sky.
Kukhulupirika kumatumphuka kuchokera ku dziko lapansi, ndipo chilungamo chimayangʼana pansi kuchokera kumwamba.
12 Yes, Yahweh will give his good blessings, and our land will yield its crops.
Ndithu Yehova adzapereka chimene chili chabwino, ndipo dziko lathu lidzapereka zokolola zake.
13 Righteousness will go before him and make a way for his footsteps.
Wolungama amapita patsogolo pake ndi kukonza njira za mapazi ake.

< Psalms 85 >