< Psalms 82 >

1 A psalm of Asaph. God stands in the divine assembly; in the midst of the gods he renders judgment.
Salimo la Asafu. Mulungu akutsogolera msonkhano waukulu; Iye akuweruza pakati pa “milungu.”
2 How long will you judge unjustly and show favoritism to the wicked? (Selah)
“Mudzateteza osalungama mpaka liti, ndi kukondera anthu oyipa?
3 Defend the poor and fatherless; maintain the rights of the afflicted and destitute.
Tetezani anthu ofowoka ndi amasiye; mukhazikitse ufulu wa anthu osauka ndi ozunzika.
4 Rescue the poor and needy; take them out of the hand of the wicked.
Landitsani anthu ofowoka ndi osowa; apulumutseni mʼdzanja la anthu oyipa.
5 They neither know nor understand; they wander around in the darkness; all the foundations of the earth crumble.
“Iwo sadziwa kanthu, sazindikira kalikonse. Amayendayenda mu mdima; maziko onse a dziko lapansi agwedezeka.
6 I said, “You are gods, and all of you sons of the Most High.
“Ndinati, ‘Inu ndinu Mulungu, nonsenu ndinu ana a Wammwambamwamba.’
7 Nevertheless you will die like men and fall like one of the princes.”
Koma mudzafa ngati anthu wamba; mudzagwa ngati wolamula wina aliyense.”
8 Arise, God, judge the earth, for you have an inheritance in all the nations.
Dzukani Inu Mulungu, weruzani dziko lapansi, pakuti mayiko onse ndi cholowa chanu.

< Psalms 82 >