< Psalms 80 >
1 For the chief musician, set to the Shoshannim Eduth style. A psalm of Asaph. Pay attention, Shepherd of Israel, you who lead Joseph like a flock; you who sit above the cherubim, shine on us!
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Kakombo wa Pangano.” Salimo la Asafu. Tcherani khutu Inu mʼbusa wa Israeli, Inu amene mumatsogolera Yosefe monga nkhosa; Inu amene mumakhala pa mpando waufumu pakati pa akerubi, walani
2 In the sight of Ephraim and Benjamin and Manasseh, stir up your power; come and save us.
kwa Efereimu, Benjamini ndi Manase. Utsani mphamvu yanu; bwerani ndi kutipulumutsa.
3 God, restore us; make your face shine on us, and we will be saved.
Tibwezereni mwakale Inu Mulungu; nkhope yanu itiwalire kuti tipulumutsidwe.
4 Yahweh God of hosts, how long will you be angry at your people when they pray?
Inu Mulungu Wamphamvuzonse, mpaka liti mkwiyo wanu udzanyeka kutsutsana ndi mapemphero a anthu anu?
5 You have fed them with the bread of tears and given them tears to drink in great quantities.
Mwawadyetsa buledi wa misozi; mwachitisa iwo kumwa misozi yodzaza mbale.
6 You make us something for our neighbors to argue over, and our enemies laugh about us among themselves.
Mwachititsa kuti tikhale gwero la mikangano pakati pa anansi athu, ndipo adani athu akutinyoza.
7 God of hosts, restore us; make your face shine on us, and we will be saved.
Tibwezereni mwakale Inu Mulungu Wamphamvuzonse, nkhope yanu itiwalire kuti tipulumutsidwe.
8 You brought a vine out of Egypt; you drove out nations and transplanted it.
Munatulutsa mpesa kuchoka ku Igupto; munathamangitsa anthu a mitundu ina ndi kuwudzala mpesawo.
9 You cleared the land for it; it took root and filled the land.
Munawulimira munda wamphesawo, ndipo unamera ndi kudzaza dziko.
10 The mountains were covered with its shade, the cedars of God by its branches.
Mapiri anaphimbidwa ndi mthunzi wake, mikungudza yamphamvu ndi nthambi zake.
11 It sent out its branches as far as the sea and its shoots to the Euphrates River.
Unatambalitsa nthambi zake mpaka ku nyanja, mphukira zake mpaka ku mtsinje.
12 Why have you broken down its walls so that all who pass by along the road pluck its fruit?
Chifukwa chiyani mwagwetsa makoma ake kuti onse amene akudutsa athyole mphesa zake?
13 The boars out of the forest ruin it, and the beasts of the field feed on it.
Nguluwe zochokera mʼnkhalango zikuwononga ndipo zirombo za mthengo zimawudya.
14 Turn back, God of hosts; look down from heaven and take notice and take care of this vine.
Bweraninso kwa ife Inu Mulungu Wamphamvuzonse! Yangʼanani pansi muli kumwambako ndipo muone! Uyangʼanireni mpesa umenewu,
15 This is the root that your right hand planted, the shoot that you made to grow.
muzu umene dzanja lanu lamanja ladzala, mwana amene inu munamukuza nokha.
16 It has been burned and cut down; they perish because of your rebuke.
Mpesa wanu wadulidwa ndi kutenthedwa ndi moto; pakudzudzula kwanu anthu anu awonongeka.
17 May your hand be on the man of your right hand, on the son of man whom you made strong for yourself.
Dzanja lanu likhale pa munthu amene ali ku dzanja lanu lamanja, mwana wa munthu amene mwalera nokha.
18 Then we will not turn away from you; revive us, and we will call on your name.
Ndipo ife sitidzatembenukira kumbali kuchoka kwa Inu; titsitsimutseni ndipo tidzayitana pa dzina lanu.
19 Yahweh God of hosts, restore us; make your face shine on us, and we will be saved.
Tibwezereni mwakale Inu Yehova Mulungu Wamphamvuzonse nkhope yanu itiwalire kuti tipulumutsidwe.