< Psalms 8 >

1 For the chief musician; set to the gittith style. A psalm of David. Yahweh our Lord, how magnificent is your name in all the earth, you who reveal your glory in the heavens above.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa gititi. Salimo la Davide. Inu Yehova Ambuye athu, dzina lanu ndi la lamphamvudi pa dziko lonse lapansi! Inu mwakhazikitsa ulemerero wanu mʼmayiko onse akumwamba.
2 Out of the mouth of babies and infants you have established praise because of your enemies, so that you might silence both the enemy and the avenger.
Kuchokera mʼkamwa mwa ana ndi makanda, Inu mwakhazikitsa mphamvu chifukwa cha adani anu, kukhazikitsa bata adani ndi anthu obwezera zoyipa.
3 When I look up at your heavens, which your fingers have made, the moon and the stars, which you have set in place,
Pamene ndilingalira za mayiko anu akumwamba, ntchito ya zala zanu, mwezi ndi nyenyezi, zimene mwaziyika pa malo ake,
4 Of what importance is the human race that you notice them, or mankind that you pay attention to them?
munthu ndani kuti Inu mumamukumbukira, ndi mwana wa munthu kuti inu mumacheza naye?
5 Yet you have made them only a little lower than the heavenly beings and have crowned them with glory and honor.
Inu munamupanga kukhala wocheperapo kusiyana ndi zolengedwa zakumwamba ndipo mwamuveka ulemerero ndi ulemu.
6 You make him to rule over the works of your hands; you have put all things under his feet:
Inu munamuyika wolamulira ntchito ya manja anu; munayika zinthu zonse pansi pa mapazi ake;
7 all sheep and oxen, and even the animals of the field,
nkhosa, mbuzi ndi ngʼombe pamodzi ndi nyama zakuthengo,
8 the birds of the heavens, and the fish of the sea, everything that passes through the currents of the seas.
mbalame zamlengalenga ndi nsomba zamʼnyanja zonse zimene zimayenda pansi pa nyanja.
9 Yahweh our Lord, how magnificent is your name in all the earth!
Inu Yehova, Ambuye athu, dzina lanu ndi lamphamvudi pa dziko lonse lapansi!

< Psalms 8 >