< Psalms 44 >
1 For the chief musician. A psalm of the sons of Korah. A maschil. We have heard with our ears, God, our fathers have told us what work you did in their days, in the days of old.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Ndakatulo ya ana a Kora. Ife tamva ndi makutu athu, Inu Mulungu; makolo athu atiwuza zimene munachita mʼmasiku awo, masiku akalekalewo.
2 You drove out the nations with your hand, but you planted our people; you afflicted the peoples, but you spread our people out in the land.
Ndi dzanja lanu munathamangitsa mitundu ya anthu ena ndi kudzala makolo athu; Inu munakantha mitundu ya anthu, koma makolo athuwo Inu munawapatsa ufulu.
3 For they did not obtain the land for their possession by their own sword, neither did their own arm save them; but your right hand, your arm, and the light of your face, because you were favorable to them.
Sanalande dziko ndi lupanga lawo, si mkono wawo umene unawabweretsera chigonjetso, koma ndi dzanja lanu lamanja, mkono wanu ndi kuwala kwa nkhope yanu, pakuti munawakonda.
4 God, You are my King; command victory for Jacob.
Inu ndinu Mfumu yanga ndi Mulungu wanga amene mumalamulira chigonjetso cha Yakobo.
5 Through you we will push down our adversaries; through your name we will tread them under, those who rise up against us.
Kudzera kwa inu ife timabweza adani athu; kudzera mʼdzina lanu timapondereza otiwukirawo.
6 For I will not trust in my bow, neither will my sword save me.
Sindidalira uta wanga, lupanga langa silindibweretsera chigonjetso;
7 But you have saved us from our adversaries, and have put to shame those who hate us.
koma Inu mumatigonjetsera adani athu, mumachititsa manyazi amene amadana nafe.
8 In God we have made our boast all the day long, and we will give thanks to your name forever. (Selah)
Timanyadira mwa Mulungu wathu tsiku lonse, ndipo tidzatamanda dzina lanu kwamuyaya.
9 But now you have thrown us off and brought us dishonor, and you do not go out with our armies.
Koma tsopano mwatikana ndi kutichepetsa; Inu simupitanso ndi ankhondo athu.
10 You make us turn back from the adversary; and those who hate us take spoil for themselves.
Munachititsa ife kubwerera mʼmbuyo pamaso pa mdani ndipo amene amadana nafe atilanda katundu.
11 You have made us like sheep to be slaughtered and have scattered us among the nations.
Inu munatipereka kuti tiwonongedwe monga nkhosa ndipo mwatibalalitsa pakati pa anthu a mitundu ina.
12 You sell your people for nothing; you have not increased your wealth by doing so.
Inu munagulitsa anthu anu pa mtengo wotsika, osapindulapo kanthu pa malondawo.
13 You make us a rebuke to our neighbors, scoffed and mocked by those around us.
Mwachititsa kuti tikhale chochititsa manyazi kwa anthu a mitundu ina, chonyozeka ndi chothetsa nzeru kwa iwo amene atizungulira.
14 You make us an insult among the nations, a shaking of the head among the peoples.
Mwachititsa kuti tikhale onyozeka pakati pa anthu a mitundu ina; anthu amapukusa mitu yawo akationa.
15 All the day long my dishonor is before me, and the shame of my face has covered me
Manyazi anga ali pamaso panga tsiku lonse ndipo nkhope yanga yaphimbidwa ndi manyazi
16 because of the voice of him who rebukes and insults, because of the enemy and the avenger.
chifukwa cha mawu otonza a iwo amene amandinyoza ndi kundichita chipongwe, chifukwa cha mdani amene watsimikiza kubwezera.
17 All this has come on us; yet we have not forgotten you or dealt falsely with your covenant.
Zonsezi zinatichitikira ngakhale kuti ifeyo sitinayiwale Inu kapena kuonetsa kusakhulupirika pa pangano lanu.
18 Our heart has not turned back; our steps have not gone from your way.
Mitima yathu sinabwerere mʼmbuyo; mapazi athu sanatayike pa njira yanu.
19 Yet you have severely broken us in the place of jackals and covered us with the shadow of death.
Koma Inu mwatiphwanya ndi kuchititsa kuti tikhale ozunzidwa ndi ankhandwe ndipo mwatiphimba ndi mdima waukulu.
20 If we have forgotten the name of our God or spread out our hands to a strange god,
Tikanayiwala dzina la Mulungu wathu kapena kutambasulira manja athu kwa mulungu wachilendo,
21 would not God search this out? For he knows the secrets of the heart.
kodi Mulungu wathu sakanazidziwa zimenezi, pakuti Iye amadziwa zinsinsi zamumtima?
22 Indeed, for your sake we are being killed all day long; we are considered to be sheep for the slaughter.
Komabe chifukwa cha Inu timakumana ndi imfa tsiku lonse, tili ngati nkhosa zoyenera kuti ziphedwe.
23 Awake, why do you sleep, Lord? Arise, do not throw us off permanently.
Dzukani Ambuye! Nʼchifukwa chiyani mukugona! Dziwutseni nokha! Musatikane kwamuyaya.
24 Why do you hide your face and forget our affliction and our oppression?
Nʼchifukwa chiyani mukubisa nkhope yanu, ndi kuyiwala mavuto athu ndi kuponderezedwa kwathu?
25 For we have melted away into the dust; our bodies cling to the earth.
Tatsitsidwa pansi mpaka pa fumbi; matupi athu amatirira pa dothi.
26 Rise up for our help and redeem us for the sake of your covenant faithfulness.
Imirirani ndi kutithandiza, tiwomboleni chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika.