< Psalms 143 >

1 A psalm of David. Hear my prayer, Yahweh; listen to my pleas. Because of your faithfulness and righteousness, answer me!
Salimo la Davide. Yehova imvani pemphero langa, mvetserani kulira kwanga kopempha chifundo; mwa kukhulupirika kwanu ndi chilungamo chanu bwerani kudzandithandiza.
2 Do not enter into judgment with your servant, for in your sight no one is righteous.
Musazenge mlandu mtumiki wanu, pakuti palibe munthu wamoyo amene ndi wolungama pamaso panu.
3 The enemy has pursued my soul; he has crushed me to the ground; he has made me to live in darkness like those who have been dead a long time.
Mdani akundithamangitsa, iye wandipondereza pansi; wachititsa kuti ndikhale mu mdima ngati munthu amene anafa kale.
4 My spirit is overwhelmed within me; my heart despairs.
Choncho mzimu wanga ukufowoka mʼkati mwanga; mʼkati mwanga, mtima wanga uli ndi nkhawa.
5 I call to mind the old days; I meditate on all your deeds; I reflect on your accomplishments.
Ndimakumbukira masiku amakedzana; ndimalingalira za ntchito yanu yonse, ndimaganizira zimene manja anu anachita.
6 I spread my hands out to you; my soul thirsts for you in a parched land. (Selah)
Ndatambalitsa manja anga kwa Inu; moyo wanga uli ndi ludzu lofuna Inu monga nthaka yowuma. (Sela)
7 Answer me quickly, Yahweh, because my spirit faints. Do not hide your face from me, or I will become like those who go down into the pit.
Yehova ndiyankheni msanga; mzimu wanga ukufowoka. Musandibisire nkhope yanu, mwina ndidzakhala ngati iwo amene atsikira ku dzenje.
8 Let me hear your covenant faithfulness in the morning, for I trust in you. Show me the way where I should walk, for I lift up my soul to you.
Lolani kuti mmawa ubweretse mawu achikondi chanu chosasinthika, pakuti ine ndimadalira Inu. Mundisonyeze njira yoti ndiyendemo, pakuti kwa Inu nditukulira moyo wanga.
9 Rescue me from my enemies, Yahweh; I flee to you to hide.
Pulumutseni kwa adani anga, Inu Yehova, pakuti ndimabisala mwa Inu.
10 Teach me to do your will, for you are my God. May your good Spirit lead me in the land of uprightness.
Phunzitseni kuchita chifuniro chanu, popeza ndinu Mulungu wanga; Mzimu wanu wabwino unditsogolere pa njira yanu yosalala.
11 Yahweh, for your name's sake, keep me alive; in your righteousness bring my soul out of trouble.
Sungani moyo wanga Inu Yehova chifukwa cha dzina lanu; mwa chilungamo chanu tulutseni mʼmasautso anga.
12 In your covenant faithfulness cut off my enemies and destroy all the enemies of my life, for I am your servant.
Mwa chikondi chanu chosasinthika khalitsani chete adani anga; wonongani adani anga, pakuti ndine mtumiki wanu.

< Psalms 143 >