< Psalms 135 >

1 Praise Yahweh. Praise the name of Yahweh. Praise him, you servants of Yahweh,
Tamandani Yehova. Tamandani dzina la Yehova; mutamandeni, inu atumiki a Yehova,
2 you who stand in Yahweh's house, in the courtyards of the house of our God.
amene mumatumikira mʼnyumba ya Yehova, mʼmabwalo a nyumba ya Mulungu wathu.
3 Praise Yahweh, for he is good; sing praises to his name, for it is pleasant to do so.
Tamandani Yehova, pakuti Yehova ndi wabwino; imbani nyimbo zotamanda dzina lake, pakuti nʼkokoma kutero,
4 For Yahweh has chosen Jacob for himself, Israel as his possession.
Pakuti Yehova wasankha Yakobo kuti akhale wake, Israeli kuti akhale chuma chake chapamtima.
5 I know that Yahweh is great, that our Lord is above all gods.
Ndikudziwa kuti Yehova ndi wamkulu, kuti Ambuye athu ndi wamkulu kuposa milungu yonse.
6 Whatever Yahweh desires, he does in heaven, on earth, in the seas and all the ocean depths.
Yehova amachita chilichonse chimene chimamukomera, kumwamba ndi dziko lapansi, ku nyanja zazikulu ndi ku malo ake onse akuya.
7 He brings the clouds from far away, making lightning bolts accompany the rain and bringing the wind out of his storehouse.
Iye amatulutsa mitambo kuchokera ku malekezero a dziko lapansi, amatumiza zingʼaningʼani pamodzi ndi mvula ndipo amatulutsa mphepo ku malo ake osungiramo.
8 He killed the firstborn of Egypt, both of man and animals.
Anakantha ana oyamba kubadwa a Igupto, ana oyamba kubadwa a anthu ndi nyama.
9 He sent signs and wonders into your midst, Egypt, against Pharaoh and all his servants.
Iye anatumiza zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa pakati pako, iwe Igupto, kutsutsana ndi Farao pamodzi ndi atumiki ake onse.
10 He attacked many nations and killed mighty kings,
Iye anakantha mitundu yambiri ya anthu ndi kupha mafumu amphamvu:
11 Sihon king of the Amorites and Og king of Bashan and all the kingdoms of Canaan.
Sihoni mfumu ya Aamori, Ogi mfumu ya Basani, ndi maufumu onse a ku Kanaani;
12 He gave us their land as an inheritance, an inheritance to Israel his people.
ndipo anapereka dziko lawo ngati cholowa, cholowa cha anthu ake Aisraeli.
13 Your name, Yahweh, endures forever; your renown, Yahweh, endures throughout all generations.
Dzina lanu, Inu Yehova, ndi losatha mpaka muyaya, mbiri yanu, Inu Yehova, idziwika mibado yonse.
14 For Yahweh defends his people and has compassion on his servants.
Pakuti Yehova adzaonetsa kuti anthu ake ngosalakwa, ndipo adzachitira chifundo atumiki ake.
15 The nations' idols are silver and gold, the work of men's hands.
Mafano a mitundu ya anthu ndi siliva ndi golide, opangidwa ndi manja a anthu.
16 Those idols have mouths, but they do not speak; they have eyes, but they do not see;
Pakamwa ali napo koma sayankhula maso ali nawo, koma sapenya;
17 they have ears, but they do not hear, nor is there breath in their mouths.
makutu ali nawo, koma sakumva ndipo mʼkamwa mwawo mulibe mpweya uliwonse.
18 Those who make them are like them, as is everyone who trusts in them.
Iwo amene amapanga mafanowo adzakhala ngati mafanowo, chimodzimodzinso iwo amene amadalira mafanowo.
19 Descendants of Israel, bless Yahweh; descendants of Aaron, bless Yahweh.
Inu nyumba ya Israeli, tamandani Yehova; inu nyumba ya Aaroni, tamandani Yehova;
20 Descendants of Levi, bless Yahweh; you who honor Yahweh, bless Yahweh.
Inu nyumba ya Levi, tamandani Yehova; Inu amene mumaopa Iye, tamandani Yehova.
21 Blessed be Yahweh in Zion, he who lives in Jerusalem. Praise Yahweh.
Wodalitsika ndi Yehova kuchokera mʼZiyoni, amene amakhala mu Yerusalemu. Tamandani Yehova.

< Psalms 135 >