< Psalms 127 >

1 A song of ascents, of Solomon. Unless Yahweh builds the house, they work uselessly, those who build it. Unless Yahweh guards the city, the watchman stands guard uselessly.
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Salimo la Solomoni. Yehova akapanda kumanga nyumba, omanga nyumbayo agwira ntchito pachabe. Yehova akapanda kulondera mzinda, mlonda akanangolondera pachabe.
2 It is useless for you to rise up early, to come home late, or to eat the bread of hard work, for Yahweh provides for his beloved as they sleep.
Mumangodzivuta nʼkulawirira mmamawa ndi kusagona msanga madzulo, kuvutikira chakudya choti mudye, pakuti Iye amapereka tulo kwa amene amawakonda.
3 See, children are a heritage from Yahweh, and the fruit of the womb is a reward from him.
Ana ndiye cholowa chochokera kwa Yehova, ana ndi mphotho yochokera kwa Iye.
4 Like arrows in the hand of a warrior, so are the children of one's youth.
Ana a pa unyamata ali ngati mivi mʼmanja mwa munthu wankhondo.
5 How blessed is the man that has his quiver full of them. He will not be put to shame when he confronts his enemies in the gate.
Wodala munthu amene motengera mivi mwake mwadzaza. Iwo sadzachititsidwa manyazi pamene alimbana ndi adani awo pa zipata.

< Psalms 127 >