< Psalms 116 >

1 I love Yahweh because he hears my voice and my pleas for mercy.
Ndimakonda Yehova pakuti Iyeyo amamva mawu anga; Iye amamva kulira kwanga kopempha chifundo.
2 Because he listened to me, I will call on him as long as I live.
Pakuti ananditchera khutu, ndidzayitana Iye masiku onse a moyo wanga.
3 The cords of death surrounded me, and the snares of Sheol confronted me; I felt anguish and sorrow. (Sheol h7585)
Zingwe za imfa zinandizinga, zoopsa za ku dziko la anthu akufa zinandigwera; ndinapeza mavuto ndi chisoni. (Sheol h7585)
4 Then I called on the name of Yahweh: “Please Yahweh, rescue my life.”
Pamenepo ndinayitana dzina la Yehova: “Inu Yehova, pulumutseni!”
5 Yahweh is merciful and fair; our God is compassionate.
Yehova ndi wokoma mtima ndi wolungama Mulungu wathu ndi wodzaza ndi chifundo.
6 Yahweh protects the naive; I was brought low, and he saved me.
Yehova amateteza munthu wodzichepetsa mtima; pamene ndinali ndi chosowa chachikulu, Iye anandipulumutsa.
7 My soul can return to its resting place, for Yahweh has been good to me.
Pumula iwe moyo wanga, pakuti Yehova wakuchitira zokoma.
8 For you rescued my life from death, my eyes from tears, and my feet from stumbling.
Pakuti Inu Yehova mwapulumutsa moyo wanga ku imfa, maso anga ku misozi, mapazi anga kuti angapunthwe,
9 I will serve Yahweh in the land of the living.
kuti ine ndiyende pamaso pa Yehova mʼdziko la anthu amoyo.
10 I believed in him, even when I said, “I am greatly afflicted.”
Ine ndinakhulupirira; choncho ndinati, “Ndasautsidwa kwambiri.”
11 In my confusion I said, “All men are liars.”
Ndipo ndili mʼnkhawa yanga ndinati, “Anthu onse ndi abodza.”
12 How can I repay Yahweh for all his kindnesses to me?
Ndingamubwezere chiyani Yehova, chifukwa cha zokoma zake zonse zimene wandichitira?
13 I will raise the cup of salvation, and call on the name of Yahweh.
Ndidzakweza chikho cha chipulumutso ndipo ndidzayitana dzina la Yehova.
14 I will fulfill my vows to Yahweh in the presence of all his people.
Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova pamaso pa anthu ake onse.
15 Precious in the sight of Yahweh is the death of his saints.
Imfa ya anthu oyera mtima ndi yamtengowapatali pamaso pa Yehova.
16 Yahweh, indeed, I am your servant; I am your servant, the son of your servant woman; you have taken away my bonds.
Inu Yehova, zoonadi ndine mtumiki wanu: ndine mtumiki wanu, mwana wa mdzakazi wanu; Inu mwamasula maunyolo anga.
17 I will offer to you the sacrifice of thanksgiving and will call on the name of Yahweh.
Ndidzapereka nsembe yachiyamiko kwa Inu ndipo ndidzayitanira pa dzina la Yehova.
18 I will fulfill my vows to Yahweh in the presence of all his people,
Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova pamaso pa anthu ake onse,
19 in the courts of Yahweh's house, in your midst, Jerusalem. Praise Yahweh.
mʼmabwalo a nyumba ya Yehova, mʼkati mwako iwe Yerusalemu. Tamandani Yehova.

< Psalms 116 >