< Psalms 115 >

1 Not to us, Yahweh, not to us, but to your name bring honor, for your covenant faithfulness and for your trustworthiness.
Kwa ife ayi Yehova, kwa ife ayi koma ulemerero ukhale pa dzina lanu, chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika ndiponso chifukwa cha kukhulupirika kwanu.
2 Why should the nations say, “Where is their God?”
Chifukwa chiyani anthu a mitundu ina akunena kuti, “Mulungu wawo ali kuti?”
3 Our God is in heaven; he does whatever he pleases.
Mulungu wathu ali kumwamba; Iye amachita chilichonse chimene chimamukondweretsa.
4 The nations' idols are silver and gold, the work of men's hands.
Koma mafano awo ndi siliva ndi golide, opangidwa ndi manja a anthu.
5 Those idols have mouths, but they do not speak; they have eyes, but they do not see;
Pakamwa ali napo koma sayankhula, maso ali nawo koma sapenya;
6 they have ears, but they do not hear; they have noses, but they do not smell.
makutu ali nawo koma samva, mphuno ali nazo koma sanunkhiza;
7 Those idols have hands, but do not feel; they have feet, but they cannot walk; nor do they speak from their mouths.
manja ali nawo koma akakhudza samva kanthu; mapazi ali nawo koma sayenda; kapena pakhosi pawo kutulutsa mawu.
8 Those who make them are like them, as is everyone who trusts in them.
Anthu amene amapanga mafanowo adzafanana nawo, chimodzimodzinso onse amene amadalira mafanowo.
9 Israel, trust in Yahweh; he is your help and shield.
Inu Aisraeli, dalirani Yehova; Iye ndiye thandizo lanu ndi chishango chanu.
10 House of Aaron, trust in Yahweh; he is your help and shield.
Iwe nyumba ya Aaroni, dalira Yehova; Iye ndiye thandizo lako ndi chishango chako.
11 You who honor Yahweh, trust in him; he is your help and shield.
Inu amene mumaopa Iye, dalirani Yehova; Iye ndiye thandizo lanu ndi chishango chanu.
12 Yahweh takes notice of us and will bless us; he will bless the family of Israel; he will bless the family of Aaron.
Yehova watikumbukira ndipo adzatidalitsa: adzadalitsa nyumba ya Israeli, adzadalitsa nyumba ya Aaroni,
13 He will bless those who honor him, both young and old.
adzadalitsa iwo amene amaopa Yehova; aangʼono ndi aakulu omwe.
14 May Yahweh increase your numbers more and more, yours and your descendants'.
Yehova akuwonjezereni madalitso; inuyo pamodzi ndi ana anu.
15 May you be blessed by Yahweh, who made heaven and earth.
Mudalitsidwe ndi Yehova, Wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.
16 The heavens belong to Yahweh; but the earth he has given to mankind.
Kumwamba ndi kwa Yehova, koma dziko lapansi Iye walipereka kwa anthu.
17 The dead do not praise Yahweh, nor do any who go down into silence;
Si anthu akufa amene amatamanda Yehova, amene amatsikira kuli chete;
18 But we will bless Yahweh now and forevermore. Praise Yahweh.
ndi ife amene timatamanda Yehova, kuyambira tsopano mpaka muyaya. Tamandani Yehova.

< Psalms 115 >