< Psalms 111 >
1 Praise Yahweh. I will give thanks to Yahweh with my whole heart in the assembly of the upright, in their gathering.
Tamandani Yehova. Ndidzathokoza Yehova ndi mtima wanga wonse mʼbwalo la anthu olungama mtima ndi pa msonkhano.
2 The works of Yahweh are great, eagerly awaited by all those who desire them.
Ntchito za Yehova nʼzazikulu; onse amene amakondwera nazo amazilingalira.
3 His work is majestic and glorious, and his righteousness endures forever.
Zochita zake ndi za ulemerero ndi zaufumu, ndipo chilungamo chake ndi chosatha.
4 He does wonderful things that will be remembered; Yahweh is gracious and merciful.
Iye wachititsa kuti zodabwitsa zake zikumbukirike; Yehova ndi wokoma mtima ndi wachifundo.
5 He gives food to his faithful followers. He will always call to mind his covenant.
Amapereka chakudya kwa amene amamuopa Iye; amakumbukira pangano lake kwamuyaya.
6 He showed his powerful works to his people in giving them the inheritance of the nations.
Waonetsa anthu ake mphamvu ya ntchito zake, kuwapatsa mayiko a anthu a mitundu ina.
7 The works of his hands are trustworthy and just; all his instructions are reliable.
Ntchito za manja ake ndi zokhulupirika ndi zolungama; malangizo ake onse ndi odalirika.
8 They are established forever, to be observed faithfully and properly.
Malamulo ndi okhazikika ku nthawi za nthawi, ochitidwa mokhulupirika ndi molungama.
9 He gave victory to his people; he ordained his covenant forever; holy and awesome is his name.
Iyeyo amawombola anthu ake; anakhazikitsa pangano lake kwamuyaya dzina lake ndi loyera ndi loopsa.
10 To honor Yahweh is the beginning of wisdom; those who carry out his instructions have good understanding. His praise endures forever.
Kuopa Yehova ndicho chiyambi cha nzeru; onse amene amatsatira malangizo ake amamvetsa bwino zinthu. Iye ndi wotamandika mpaka muyaya.