< Psalms 104 >

1 I give praise to Yahweh with all my life, Yahweh my God, you are very magnificent; you are clothed with splendor and majesty.
Tamanda Yehova, iwe moyo wanga. Inu Yehova Mulungu wanga, ndinu wamkulu kwambiri; mwavala ulemerero ndi ufumu.
2 You cover yourself with light as with a garment; you spread out the heavens like a tent curtain.
Iye wadzifunditsa kuwala ngati chovala; watambasula miyamba ngati tenti
3 You lay the beams of your chambers on the clouds; you make the clouds your chariot; you walk on the wings of the wind.
ndipo wayika pa madzi mitanda ya chipinda chake. Iye amasandutsa mitambo kukhala galeta lake, ndi kuwuluka pa mapiko a mphepo.
4 He makes the winds his messengers, flames of fire his servants.
Amapanga mphepo kukhala amithenga ake, malawi amoto kukhala atumiki ake.
5 He laid the foundations of the earth, and it will never be moved.
Anakhazikitsa dziko lapansi pa maziko ake; silingasunthike.
6 You covered the earth with water like a garment; the water covered the mountains.
Munaliphimba ndi nyanja yozama ngati chovala; madzi anayimirira pamwamba pa mapiri.
7 Your rebuke made the waters recede; at the sound of your thunderous voice they fled.
Koma pakudzudzula kwanu madzi anathawa, pa mkokomo wa bingu lanu iwo anamwazika;
8 The mountains rose, and the valleys spread out into the places that you had appointed for them.
Inu munamiza mapiri, iwo anatsikira ku zigwa kumalo kumene munawakonzera.
9 You have set a boundary for them that they will not cross; they will not cover the earth again.
Inu munayika malire ndipo sangathe kudutsa, iwo sadzamizanso dziko lapansi.
10 He made springs flow into the valleys; the streams flow between the mountains.
Iye achititsa akasupe kutulutsa madzi kupita ku zigwa; madziwo amayenda pakati pa mapiri.
11 They supply water for all the animals of the field; the wild donkeys quench their thirst.
Iwo amapereka madzi kwa zirombo zonse zakuthengo; abulu akuthengo amapha ludzu lawo.
12 By the riverbanks the birds build their nests; they sing among the branches.
Mbalame zamlengalenga zimayika zisa mʼmbali mwa madzi; zimayimba pakati pa thambo.
13 He waters the mountains from his water chambers in the sky. The earth is filled with the fruit of his labor.
Iye amathirira mapiri kuchokera ku zipinda zake zapamwamba; dziko lapansi limakhutitsidwa ndi chipatso cha ntchito yake.
14 He makes the grass grow for the cattle and plants for man to cultivate so that man may produce food from the earth.
Amameretsa udzu kuti ngʼombe zidye, ndi zomera, kuti munthu azilima kubweretsa chakudya kuchokera mʼdziko lapansi:
15 He makes wine to make man happy, oil to make his face shine, and food to sustain his life.
vinyo amene amasangalatsa mtima wa munthu, mafuta amene amachititsa nkhope yake kuwala, ndi buledi amene amapereka mphamvu.
16 The trees of Yahweh get plenty of rain; the cedars of Lebanon which he planted.
Mitengo ya Yehova ndi yothiriridwa bwino, mikungudza ya ku Lebanoni imene Iye anadzala.
17 There the birds make their nests. The stork makes the cypress tree her home.
Mbalame zimamanga zisa zawo; kakowa ali ndi malo ake mʼmikungudzamo.
18 The wild goats live on the high mountains; the mountain heights are a refuge for the hyraxes.
Mapiri ataliatali ndi a mbalale; mʼmingʼalu ya miyala ndi mobisalamo mbira.
19 He appointed the moon to mark the seasons; the sun knows its time for setting.
Mwezi umasiyanitsa nyengo ndipo dzuwa limadziwa nthawi yake yolowera.
20 You make the darkness of the night when all the beasts of the forest come out.
Inu mumabweretsa mdima nukhala usiku, ndipo zirombo zonse za ku nkhalango zimatuluka.
21 The young lions roar for their prey and seek their food from God.
Mikango imabangula kufuna nyama, ndi kufunafuna chakudya chawo kuchokera kwa Mulungu.
22 When the sun rises, they retreat and sleep in their dens.
Dzuwa limatuluka ndipo iyo imapita kukabisala; imabwerera kukagona pansi mʼmapanga awo.
23 Meanwhile, people go out to their work and labor away until the evening.
Pamenepo munthu amapita ku ntchito yake, kukagwira ntchito yake mpaka madzulo.
24 Yahweh, how many and varied are your works! With wisdom you made them all; the earth overflows with your works.
Ntchito zanu ndi zochulukadi Inu Yehova! Munazipanga zonse mwanzeru, dziko lapansi ladzaza ndi zolengedwa zanu.
25 Over there is the sea, deep and wide, teeming with innumerable creatures, both small and great.
Kuli nyanja yayikulu ndi yotambalala, yodzaza ndi zolengedwa zosawerengeka, zamoyo zanu zazikulu ndi zazingʼono zomwe.
26 The ships travel there, and Leviathan is also there, which you formed to play in the sea.
Kumeneko sitima zapamadzi zimayenda uku ndi uku, ndiponso Leviyatani amene munamulenga kuti asewere kumeneko.
27 All these look to you to give them their food on time.
Zonsezi zimayangʼana kwa Inu kuti muzipatse chakudya chawo pa nthawi yake yoyenera.
28 When you give to them, they gather; when you open your hand, they are satisfied.
Mukazipatsa, zimachisonkhanitsa pamodzi; mukatsekula dzanja lanu, izo zimakhutitsidwa ndi zinthu zabwino.
29 When you hide your face, they are troubled; if you take away their breath, they die and return to dust.
Mukabisa nkhope yanu, izo zimachita mantha aakulu; mukachotsa mpweya wawo, zimafa ndi kubwerera ku fumbi.
30 When you send out your Spirit, they are created, and you renew the countryside.
Mukatumiza mzimu wanu, izo zimalengedwa ndipo mumakozanso maonekedwe a dziko lapansi.
31 May the glory of Yahweh last forever; may Yahweh enjoy his creation.
Ulemerero wa Yehova ukhalebe mpaka muyaya; Yehova akondwere ndi ntchito ya manja ake;
32 He looks down on the earth, and it shakes; he touches the mountains, and they smoke.
Iye amene amayangʼana dziko lapansi ndipo limanjenjemera, amene amakhudza mapiri ndipo amatuluka utsi.
33 I will sing to Yahweh all my life; I will sing praise to my God as long as I live.
Ine ndidzayimbira Yehova moyo wanga wonse; ndidzayimbira matamando Mulungu wanga nthawi yonse imene ndili ndi moyo.
34 May my thoughts be sweet to him; I will rejoice in Yahweh.
Zolingalira zanga zikhale zomukomera Iye, pamene ndikusangalala mwa Yehova.
35 May sinners vanish from the earth, and let the wicked be no more. I give praise to Yahweh with all my life. Praise Yahweh.
Koma anthu ochimwa awonongeke pa dziko lapansi ndipo anthu oyipa asapezekenso. Tamanda Yehova, Iwe moyo wanga. Tamandani Yehova.

< Psalms 104 >