< Psalms 103 >

1 A psalm of David. I give praise to Yahweh with all my life, and with all that is within me, I give praise to his holy name.
Salimo la Davide. Tamanda Yehova, iwe moyo wanga; ndi zonse zamʼkati mwanga zitamande dzina lake loyera.
2 I give praise to Yahweh with all my life, and I remember all of his good deeds.
Tamanda Yehova, iwe moyo wanga, ndipo usayiwale zabwino zake zonse.
3 He forgives all your sins; he heals all your diseases.
Amene amakhululuka machimo ako onse ndi kuchiritsa nthenda zako zonse,
4 He redeems your life from destruction; he crowns you with covenant faithfulness and acts of tender mercy.
amene awombola moyo wako ku dzenje ndi kukuveka chikondi ndi chifundo chake ngati chipewa chaufumu,
5 He satisfies your life with good things so that your youth is renewed like the eagle.
amene akwaniritsa zokhumba zako ndi zinthu zabwino, kotero kuti umakhala wamphamvu zatsopano ngati mphungu.
6 Yahweh does what is fair and does acts of justice for all who are oppressed.
Yehova amachita chilungamo ndipo amaweruza molungama onse opsinjika.
7 He made known his ways to Moses, his deeds to the descendants of Israel.
Iye anadziwitsa Mose njira zake, ntchito zake kwa Aisraeli.
8 Yahweh is merciful and gracious; he is patient; he has great covenant loyalty.
Yehova ndi wachifundo ndi wokoma mtima, wosakwiya msanga ndi wachikondi chochuluka.
9 He will not always discipline; he is not always angry.
Iye sadzatsutsa nthawi zonse, kapena kusunga mkwiyo wake kwamuyaya;
10 He does not deal with us as our sins deserve or repay us for what our sins demand.
satichitira molingana ndi machimo athu, kapena kutibwezera molingana ndi mphulupulu zathu.
11 For as the skies are high above the earth, so great is his covenant faithfulness toward those who honor him.
Pakuti monga kumwamba kuli kutali ndi dziko lapansi, koteronso chikondi chake nʼchachikulu kwa iwo amene amamuopa;
12 As far as the east is from the west, this is how far he has removed the guilt of our sins from us.
monga kummawa kutalikirana ndi kumadzulo, koteronso Iye watichotsera mphulupulu zathu kuti zikhale kutali nafe.
13 As a father has compassion on his children, so Yahweh has compassion on those who honor him.
Monga bambo amachitira chifundo ana ake, choncho Yehova ali ndi chifundo ndi iwo amene amamuopa;
14 For he knows how we are formed; he knows that we are dust.
pakuti Iye amadziwa momwe tinawumbidwira, amakumbukira kuti ndife fumbi.
15 As for man, his days are like grass; he flourishes like a flower in a field.
Kunena za munthu, masiku ake ali ngati udzu, amaphuka ngati duwa la mʼmunda;
16 The wind blows over it, and it disappears, and no one can even tell where it once grew.
koma mphepo imawombapo ndipo silionekanso ndipo malo ake sakumbukirikanso.
17 But the covenant faithfulness of Yahweh is from everlasting to everlasting on those who honor him. His righteousness extends to their descendants.
Koma kuchokera muyaya mpaka muyaya chikondi cha Yehova chili ndi iwo amene amamuopa, ndi chilungamo chake chili ndi ana a ana awo;
18 They keep his covenant and remember to obey his instructions.
iwo amene amasunga pangano lake ndi kukumbukira kumvera malangizo ake.
19 Yahweh has established his throne in the heavens, and his kingdom rules over everyone.
Yehova wakhazikitsa mpando wake waufumu mmwamba ndipo ufumu wake umalamulira onse.
20 Give praise to Yahweh, you his angels, you mighty ones who are strong and do his word, and obey the sound of his word.
Tamandani Yehova, inu angelo ake, amphamvu inu amene mumachita zimene amalamula, amene mumamvera mawu ake.
21 Give praise to Yahweh, all his hosts, you are his servants who carry out his will.
Tamandani Yehova, zolengedwa zonse zakumwamba, inu atumiki ake amene mumachita chifuniro chake.
22 Give praise to Yahweh, all his creatures, in all the places where he reigns. I will give praise to Yahweh with all my life.
Tamandani Yehova, ntchito yake yonse kulikonse mu ulamuliro wake. Tamanda Yehova, iwe moyo wanga.

< Psalms 103 >