< Proverbs 29 >
1 A person who has received many rebukes but who stiffens his neck will be broken in a moment beyond healing.
Munthu amene amawumitsabe khosi lake atadzudzulidwa kwambiri, adzawonongeka mwadzidzidzi popanda chomuchiritsa.
2 When righteous people increase, the people rejoice, but when a wicked person is the ruler, the people sigh.
Anthu olungama akamalamulira mʼdziko anthu amakondwa, koma ngati dziko lilamulidwa ndi anthu oyipa mtima anthu amadandaula.
3 Whoever loves wisdom makes his father rejoice, but he who keeps company with prostitutes destroys his wealth.
Munthu amene amakonda nzeru amasangalatsa abambo ake, koma woyenda ndi akazi achiwerewere amasakaza chuma chake.
4 The king establishes the land by justice, but the one who demands bribes tears it down.
Mfumu imalimbitsa dziko poweruza mwachilungamo, koma mfumu imene imawumiriza anthu kuti ayipatse mphatso imawononga dziko.
5 A man who flatters his neighbor is spreading a net for his feet.
Munthu woshashalika mnzake, akudziyalira ukonde mapazi ake.
6 In the sin of an evil person is a trap, but the righteous person sings and rejoices.
Munthu woyipa amakodwa ndi machimo ake, koma wochita chilungamo amayimba lokoma.
7 The righteous person knows the rights of the poor; the wicked person does not understand such knowledge.
Munthu wolungama amasamalira anthu osauka, koma woyipa salabadira zimenezi.
8 Mockers set a city on fire, but those who are wise turn away wrath.
Anthu onyoza atha kuwutsa ziwawa mu mzinda, koma anthu anzeru amaletsa ukali.
9 When a wise person has an argument with a fool, he rages and laughs, and there will be no rest.
Ngati munthu wanzeru atsutsana ndi chitsiru, chitsirucho chimachita phokoso ndi kumangoseka ndipo sipakhala mtendere.
10 The bloodthirsty hate the one who is blameless and seek the life of the upright.
Anthu okhetsa magazi amadana ndi munthu wangwiro koma anthu olungama amasamalira moyo wake.
11 A fool reveals all his anger, but a wise man holds it back and calms himself down.
Munthu wopusa amaonetsa mkwiyo wake, koma munthu wanzeru amadzigwira.
12 If a ruler pays attention to lies, all his officials will be wicked.
Ngati wolamulira amvera zabodza, akuluakulu ake onse adzakhala oyipa.
13 The poor person and the oppressor are similar, for Yahweh gives light to the eyes of them both.
Munthu wosauka ndi munthu wopondereza anzake amafanana pa kuti: Yehova ndiye anawapatsa maso onsewa.
14 If a king judges the poor by the truth, his throne will be established forever.
Ngati mfumu iweruza osauka moyenera, mpando wake waufumu udzakhazikika nthawi zonse.
15 The rod and reproof give wisdom, but a child freed from discipline puts his mother to shame.
Ndodo ndi chidzudzulo zimapatsa nzeru koma mwana womulekerera amachititsa amayi ake manyazi.
16 When wicked people are in power, transgression increases, but righteous people will see the downfall of those wicked people.
Oyipa akamalamulira zoyipa zimachuluka, koma anthu olungama adzaona kugwa kwa anthu oyipawo.
17 Discipline your son and he will give you rest; he will bring delights into your life.
Umulange mwana wako ndipo adzakupatsa mtendere ndi kusangalatsa mtima wako.
18 Where there is no prophetic vision the people run wild, but the one who keeps the law is blessed.
Ngati uthenga wochokera kwa Yehova supezeka anthu amangochita zofuna zawo; koma wodala ndi amene amasunga malamulo.
19 A slave will not be corrected by words, for though he understands, there will be no response.
Munthu wantchito sangalangizidwe ndi mawu okha basi; ngakhale awamvetse mawuwo sadzatha kuchitapo kanthu.
20 See a man who is hasty in his words? There is more hope for a fool than for him.
Ngakhale munthu wa uchitsiru nʼkuti ndiponi popeza chikhulupiriro chilipo kuposa munthu wodziyesa yekha kuti ndi wanzeru poyankhula.
21 One who pampers his slave from youth, at the end of it there will be trouble.
Ngati munthu asasatitsa wantchito wake kuyambira ali mwana, potsirizira adzapeza kuti wantchitoyo wasanduka mlowachuma wake.
22 An angry person stirs up strife and a master of rage commits many sins.
Munthu wamkwiyo amayambitsa mikangano, ndipo munthu waukali amachita zolakwa zambiri.
23 A person's pride brings him low, but one who has a humble spirit will be given honor.
Kunyada kwa munthu kudzamutsitsa, koma munthu wodzichepetsa amalandira ulemu.
24 One who shares with a thief hates his own life; he hears the curse and says nothing.
Woyenda ndi munthu wakuba ndi mdani wa moyo wake womwe; amalumbira koma osawulula kanthu.
25 The fear of man makes a snare, but the one who trusts in Yahweh will be protected.
Kuopa munthu kudzakhala ngati msampha, koma aliyense amene amadalira Yehova adzatetezedwa.
26 Many are those who seek the face of the ruler, but from Yahweh is justice for a person.
Anthu ambiri amafunitsitsa kuti wolamulira awakomere mtima, koma munthu amaweruzidwa mwachilungamo ndi thandizo la Yehova basi.
27 An unjust man is an abomination to righteous people, but the one whose way is upright is detestable to the wicked person.
Anthu olungama amanyansidwa ndi anthu achinyengo; koma anthu oyipa amanyansidwa ndi anthu a mtima wowongoka.