< Proverbs 27 >
1 Do not boast about tomorrow, for you do not know what a day may bring.
Usamanyadire za mawa, pakuti sudziwa zimene zidzachitike pa tsikulo.
2 Let someone else praise you and not your own mouth; a stranger and not your own lips.
Munthu wina akutamande, koma osati wekha; mlendo akakutamanda, ndiponi koma osati ndi pakamwa pako.
3 Consider the heaviness of a stone and the weight of sand— the provocation of a fool is heavier than both.
Mwala ndi wolemera ndipo mchenganso ndi wolemera kwambiri, koma makani a chitsiru ndi oposa zonsezo kulemera kwake.
4 There is the cruelty of rage and the flood of anger, but who is able to stand before jealousy?
Mkwiyo umadzetsa nkhanza ndipo kupsa mtima kumachititsa zoopsa. Koma nsanje imachita zoopsa zopambana.
5 Better is an open rebuke than hidden love.
Kudzudzula munthu poyera nʼkwabwino kuposa chikondi chobisika.
6 Faithful are the wounds caused by a friend, but an enemy may kiss you profusely.
Munthu amene amakukonda ngakhale akupweteke zili bwino, koma mdani wako amakupsompsona mwachinyengo.
7 A person who has eaten to the full rejects even a honeycomb, but to the hungry person, every bitter thing is sweet.
Iye amene wakhuta amayipidwa ndi chisa cha uchi, koma kwa munthu wanjala ngakhale chimene chili chowawa chimamukomera.
8 Like a bird that wanders from its nest is a man who strays from where he lives.
Munthu amene wasochera ku nyumba kwake, ali monga mbalame imene yasochera pa chisa chake.
9 Perfume and incense make the heart rejoice, but the sweetness of a friend comes from his sincere counsel.
Mafuta ndi zonunkhira zimasangalatsa mtima, ndipo kukoma mtima kwa bwenzi kwagona pa malangizo ake.
10 Do not forsake your friend and your friend's father, and do not go to your brother's house on the day of your calamity. Better is a neighbor who is nearby than a brother who is far away.
Usasiye bwenzi lako ndiponso bwenzi la abambo ako, ndipo usapite ku nyumba ya mʼbale wako pamene wakumana ndi mavuto; mnzako wokhala naye pafupi amaposa mʼbale wako wokhala kutali.
11 Be wise, my son, and make my heart rejoice; then I will give back an answer to the one who mocks me.
Mwana wanga, khala wanzeru, ndipo ukondweretse mtima wanga; pamenepo ine ndidzatha kuyankha aliyense amene amandinyoza.
12 A prudent man sees trouble and hides himself, but the naive people go on and suffer because of it.
Munthu wochenjera akaona choopsa amabisala, koma munthu wopusa amangopitirira ndipo amakumana ndi mavuto.
13 Take a garment of one who has put up security for a stranger, and hold it in pledge when he puts up security for an immoral woman.
Utenge chovala cha munthu amene waperekera mlendo chikole; ngati chigwiriro chifukwa waperekera chikole mlendo wosadziwika.
14 Whoever gives his neighbor a blessing with a loud voice early in the morning, that blessing will be considered to be a curse!
Ngati munthu apatsa mnzake moni mofuwula mmamawa kwambiri, anthu adzamuyesa kuti akutemberera.
15 A quarreling wife is like the constant dripping on a rainy day;
Mkazi wolongolola ali ngati mvula yamvumbi.
16 restraining her is like restraining the wind, or trying to catch oil in your right hand.
Kumuletsa mkazi wotereyu zimenezi zili ngati kuletsa mphepo kapena kufumbata mafuta mʼdzanja.
17 Iron sharpens iron; in the same way, a man sharpens his friend.
Chitsulo chimanoledwa ndi chitsulo chinzake, chomwechonso munthu amanoledwa ndi munthu mnzake.
18 The one who tends a fig tree will eat its fruit, and the one who protects his master will be honored.
Amene amasamalira mtengo wamkuyu adzadya zipatso zake, ndipo iye amene amasamalira mbuye wake adzalandira ulemu.
19 Just as water reflects a person's face, so a person's heart reflects the person.
Monga momwe nkhope imaonekera mʼmadzi, chomwechonso mtima wa munthu umadziwika ndi ntchito zake.
20 Just as Sheol and Abaddon are never satisfied, so a man's eyes are never satisfied. (Sheol )
Manda sakhuta, nawonso maso a munthu sakhuta. (Sheol )
21 A crucible is for silver and a furnace is for gold; and a person is tested when he is praised.
Siliva amasungunulira mu uvuni ndipo golide mʼngʼanjo, chomwechonso munthu amadziwika ndi zomwe akudzitamandira nazo.
22 Even if you crush a fool with the pestle—along with the grain— yet his foolishness will not leave him.
Ngakhale utakonola chitsiru mu mtondo ndi musi ngati chimanga, uchitsiru wakewo sudzachoka.
23 Be sure you know the condition of your flocks and be concerned about your herds,
Uzidziwe bwino nkhosa zako momwe zilili. Kodi usamalire bwino ziweto zako?
24 for wealth is not forever. Does a crown endure for all generations?
Paja chuma sichikhala mpaka muyaya, ndipo ufumu sukhala mpaka mibado yonse.
25 You should know when the hay is gone and the new growth appears, and the time when the grass from the hills is gathered in.
Pamene udzu watha, msipu nʼkumera; ndipo atatuta udzu wa ku mapiri,
26 Those lambs will provide your clothing and the goats will provide the price of the field.
ana ankhosa adzakupatsani chovala ndipo pogulitsa mbuzi mudzapeza ndalama yogulira munda.
27 There will be goats' milk for your food—the food for your household— and nourishment for your servant girls.
Mudzakhala ndi mkaka wambuzi wambiri kuti muzidya inuyo ndi banja lanu ndi kudyetsa antchito anu aakazi.