< Proverbs 26 >
1 Like snow in summer or rain in harvest, so a fool does not deserve honor.
Ngati chisanu choti mbee nthawi yachilimwe kapena mvula nthawi yokolola, ndi momwe zilili ndi ulemu wowulandira chitsiru.
2 As the sparrow flitters and the swallow darts when they fly, so an undeserved curse does not alight.
Ngati timba wokhalira kuwuluka kapena namzeze wokhalira kuzungulirazungulira, ndi mmenenso limachitira temberero lopanda chifukwa, silichitika.
3 A whip is for the horse, a bridle is for the donkey and a rod is for the back of fools.
Mkwapulo ndi wokwapulira kavalo, chitsulo ndi cha mʼkamwa mwa bulu, choncho ndodo ndi yoyenera ku msana wa chitsiru.
4 Do not answer a fool according to his folly, or you will become like him.
Usayankhe chitsiru monga mwa uchitsiru wake, kuopa kuti ungadzakhale ngati chitsirucho.
5 Answer a fool and join in on his folly, so he will not become wise in his own eyes.
Koma nthawi zina umuyankhe monga mwa uchitsiru wake, kuopa kuti angamadziyese yekha wanzeru.
6 Whoever sends a message by the hand of a fool cuts off his own feet and drinks violence.
Kutuma chitsiru kuti akapereke uthenga kuli ngati kudzidula mapazi ndipo kumakuyitanira mavuto.
7 Like the legs of a paralytic which hang down is a proverb in the mouth of fools.
Monga miyendo ya munthu wolumala imene ilibe mphamvu ndi mmene ulili mwambi mʼkamwa mwa chitsiru.
8 Like tying a stone in a sling is giving honor to a fool.
Kupereka ulemu kwa chitsiru zili ngati kukulunga mwala mʼlegeni.
9 Like a thorn that goes into the hand of a drunkard is a proverb in the mouth of fools.
Monga umachitira mtengo waminga wobaya mʼdzanja la chidakwa ndi mmene ulili mwambi mʼkamwa mwa chitsiru.
10 Like an archer who wounds all those around him is one who hires a fool or hires anyone who passes by.
Munthu amene amalemba ntchito chitsiru chongoyendayenda, ali ngati woponya mivi amene angolasa anthu chilaselase.
11 As a dog returns to his own vomit, so is a fool who repeats his folly.
Chitsiru chimene chimabwerezabwereza uchitsiru wake chili ngati galu amene amabwerera ku masanzi ake.
12 Do you see someone who is wise in his own eyes? There is more hope for a fool than for him.
Munthu wa uchitsiru aliko bwino popeza pali chiyembekezo kuposana ndi munthu amene amadziyesa yekha kuti ndi wanzeru.
13 The lazy person says, “There is a lion on the road! There is a lion between the open places!”
Munthu waulesi amati, “Mu msewu muli mkango, mkango woopsa ukuyendayenda mʼmisewu!”
14 As the door turns on its hinges, so is the lazy person upon his bed.
Monga chitseko chimapita uku ndi uku pa zolumikizira zake, momwemonso munthu waulesi amangotembenukatembenuka pa bedi lake.
15 The lazy person puts his hand into the dish and yet he has no strength to lift it up to his mouth.
Munthu waulesi akapisa dzanja lake mu mʼbale; zimamutopetsa kuti alifikitse pakamwa pake.
16 The lazy person is wiser in his own eyes than seven men who respond with good judgment.
Munthu waulesi amadziyesa yekha wanzeru kuposa anthu asanu ndi awiri amene amayankha mochenjera.
17 Like one who takes hold of the ears of a dog, is a passerby who becomes angry at a dispute that is not his own.
Munthu wongolowera mikangano imene si yake ali ngati munthu wogwira makutu a galu wongodziyendera.
18 Like a madman who shoots burning arrows,
Monga munthu wamisala amene akuponya sakali zamoto kapena mivi yoopsa,
19 is the one who deceives his neighbor and says, “Was I not telling a joke?”
ndi momwe alili munthu wonamiza mnzake, amene amati, “Ndimangoseka chabe!”
20 For lack of wood, the fire goes out; and where there is no gossiper quarreling ceases.
Pakasowa nkhuni, moto umazima; chomwechonso pakasowa anthu amiseche mkangano umatha.
21 As charcoal is to burning coals and wood is to fire, so is a quarrelsome person for kindling strife.
Monga alili makala pa moto wonyeka kapena mmene zimachitira nkhuni pa moto, ndi mmene alili munthu wolongolola poyambitsa mikangano.
22 The words of a gossip are like delicious morsels; they go down into the inner parts of the body.
Mawu a munthu wamiseche ali ngati chakudya chokoma; chimene chimatsikira mʼmimba mwa munthu.
23 Like the glaze overlaying an earthen vessel so are burning lips and an evil heart.
Monga mmene chiziro chimakutira chiwiya chadothi ndi mmene mawu oshashalika amabisira mtima woyipa.
24 One who hates others disguises his feelings with his lips and he lays up deceit within himself.
Munthu wachidani amayankhula zabwino pamene mu mtima mwake muli chinyengo.
25 He will speak graciously, but do not believe him, for there are seven abominations in his heart.
Ngakhale wotereyu mawu ake ali okoma, koma usamukhulupirire, pakuti mu mtima mwake mwadzaza zonyansa.
26 Though his hatred is covered with deception, his wickedness will be exposed in the assembly.
Ngakhale amabisa chidani mochenjera, koma kuyipa kwakeko kudzaonekera poyera pa gulu la anthu.
27 Whoever digs a pit will fall into it and the stone will roll back on the one who pushed it.
Ngati munthu akumba dzenje, adzagweramo yekha; ngati munthu agubuduza mwala, udzamupsinja iye mwini.
28 A lying tongue hates the people it crushes and a flattering mouth brings about ruin.
Munthu wonama amadana ndi amene anawapweteka, ndipo pakamwa poshashalika pamabweretsa chiwonongeko.