< Proverbs 16 >
1 The plans of the heart belong to a person, but from Yahweh comes the answer from his tongue.
Zolinga za mu mtima ndi za munthu, koma kwa Yehova ndiye kumachokera yankho.
2 All of a person's ways are pure in his own eyes, but Yahweh weighs the spirits.
Zochita zonse za munthu zimaoneka zabwino pamaso pake, koma Yehova ndiye amasanthula zolinga zako.
3 Commit your works to Yahweh and your plans will succeed.
Pereka ntchito zako zonse mʼmanja mwa Yehova, ndipo zolinga zako zidzachitikadi.
4 Yahweh has made everything for its purpose, even the wicked for the day of trouble.
Yehova amachita zonse ndi cholinga chake, ngakhale anthu oyipa kuti aone tsiku latsoka.
5 Yahweh hates everyone who has an arrogant heart, but be sure of this, they will not go unpunished.
Munthu aliyense wodzikuza amamunyansa Yehova. Koma dziwani izi: Iwo sadzakhala osalangidwa.
6 By covenant faithfulness and trustworthiness iniquity is atoned for and by the fear of Yahweh people turn away from evil.
Chifukwa cha chikondi chosasinthika ndi kukhulupirika, munthu amakhululukidwa machimo ake; chifukwa cha kuopa Yehova munthu amapewa zoyipa.
7 When a person's ways are pleasing to Yahweh, he makes even that person's enemies to be at peace with him.
Pamene makhalidwe a munthu akondweretsa Yehova, ngakhale adani ake amakhala naye mwa mtendere.
8 Better is a little with what is right, than a large income with injustice.
Kuli bwino kukhala ndi zinthu pangʼono zozipeza mwachilungamo, kusiyana ndi kukhala ndi zinthu zambiri zozipeza popanda chilungamo.
9 In his heart a person plans out his way, but Yahweh directs his steps.
Mtima wa munthu umalingalira zochita, koma Yehova ndiye amakhazikitsa njira zake.
10 Insightful decisions are on the lips of a king, his mouth should not betray justice.
Mawu a mfumu ali ngati mawu ochokera kwa Mulungu; ndipo pakamwa pake sipalakwa poweruza mlandu.
11 Honest scales come from Yahweh; all the weights in the bag are his work.
Miyeso ndi masikelo achilungamo zimachokera kwa Yehova; miyala yonse yoyesera ya mʼthumba anayipanga ndi Yehova.
12 When kings do wicked things, that is something to be despised, for a throne is established by doing what is right.
Kuchita zoyipa kumanyansa mafumu, pakuti chilungamo ndiye maziko a ufumu wake.
13 A king delights in lips that say what is right and he loves the one who speaks directly.
Mawu owona amakondweretsa mfumu. Iyo imakonda munthu woyankhula choonadi.
14 A king's wrath is a messenger of death but a wise man will try to calm his anger.
Ukali wa mfumu ndi mthenga wa imfa, koma munthu wanzeru amawupepesa ukaliwo.
15 In the light of a king's face is life and his favor is like a cloud that brings a spring rain.
Kuwala kwa nkhope ya mfumu kumapatsa moyo; ndipo kukoma mtima kwake kuli ngati mitambo ya mvula nthawi ya chilimwe.
16 How much better it is to get wisdom than gold. To get understanding should be chosen more than silver.
Nʼkwabwino kwambiri kupeza nzeru kupambana golide. Kukhala womvetsa bwino zinthu nʼkwabwino kupambana ndi kukhala ndi siliva.
17 The highway of upright people turns away from evil; the one who protects his life guards his way.
Msewu wa munthu wowongoka mtima umapewa zoyipa; wopenyetsetsa kumene akupita amasunga moyo wake.
18 Pride comes before destruction and a haughty spirit before a downfall.
Kunyada kumafikitsa ku chiwonongeko, ndipo munthu wodzikuza adzagwa.
19 It is better to be humble among poor people than to divide the spoil with proud people.
Nʼkwabwino kukhala ndi mtima wodzichepetsa pakati pa anthu oponderezedwa, kusiyana ndi kugawana zolanda ndi anthu onyada.
20 Whoever contemplates what they are taught will find what is good, and those who trust in Yahweh will be blessed.
Munthu womvera malangizo zinthu zimamuyendera bwino, ndipo wodala ndi amene amadalira Yehova.
21 The one who is wise in heart is called discerning and sweetness of speech improves the ability to teach.
A mtima wanzeru amatchedwa ozindikira zinthu, ndipo mawu ake okoma amawonjezera nzeru.
22 Understanding is a fountain of life to the one who has it, but the instruction of fools is their foolishness.
Kumvetsa zinthu ndi kasupe wa moyo kwa iwo amene ali nako, koma uchitsiru umabweretsa chilango kwa zitsiru.
23 The heart of a wise person gives insight to his mouth and adds persuasiveness to his lips.
Mtima wanzeru umathandiza munthu kuyankhula mwa nzeru, ndipo mawu ake amawonjezera nzeru.
24 Pleasant words are a honeycomb— sweet to the soul and healing to the bones.
Mawu okometsera ali ngati chisa cha njuchi, amakoma mu mtima ndipo amalimbitsa thupi.
25 There is a way that seems right to a man, but its end is the way to death.
Pali njira ina yooneka ngati yowongoka kwa munthu koma kumatsiriziro kwake ndi imfa.
26 The laborer's appetite works for him; his hunger urges him on.
Njala ya munthu wantchito imamuthandiza kulimbikira; njalayo imamukakamiza kuchitapo kanthu.
27 A worthless person digs up mischief and his speech is like a scorching fire.
Munthu wopanda pake amakonzekera kuchita zoyipa ndipo mawu ake ali ngati moto wopsereza.
28 A perverse person stirs up conflict and a gossip separates close friends.
Munthu woyipa mtima amayambitsa mikangano, ndipo miseche imalekanitsa anthu okondana kwambiri.
29 A man of violence lies to his neighbor and leads him down a path that is not good.
Munthu wandewu amakopa mnansi wake, ndipo amamuyendetsa njira imene si yabwino.
30 The one who winks the eye is plotting perverse things; those who purse the lips will bring evil to pass.
Amene amatsinzinira maso ake amalingalira zinthu zokhota; amene amachita msunamo amakonzeka kuchita zoyipa.
31 Gray hair is a crown of glory; it is gained by living the right way.
Imvi zili ngati chipewa chaufumu chaulemerero; munthu amazipeza akakhala moyo wolungama.
32 It is better to be slow to anger than to be a warrior and one who rules his spirit is stronger than one who conquers a city.
Munthu wosapsa mtima msanga amaposa munthu wankhondo, munthu wowugwira mtima wake amaposa amene amalanda mzinda.
33 The lots are cast into the lap, but the decision is from Yahweh.
Maere amaponyedwa pa mfunga, koma ndiye Yehova amene amalongosola zonse.