< Proverbs 14 >
1 The wise woman builds her house, but a foolish woman tears it down with her own hands.
Mkazi wanzeru amamanga banja lake, koma mkazi wopusa amalimasula ndi manja ake omwe.
2 The one who walks uprightly fears Yahweh, but the one who is dishonest in his ways despises him.
Amene amayenda molungama amaopa Yehova, koma amene njira zake ndi zoyipa amanyoza Yehova.
3 From the mouth of a fool comes an offshoot of his pride, but the lips of the wise will preserve them.
Kuyankhula kwa chitsiru kumamuyitanira ndodo pa msana, koma milomo ya munthu wanzeru imamuteteza.
4 Where there are no cattle the feeding trough is clean, but an abundant crop can come by the strength of an ox.
Pakasowa ngʼombe zolima gome limakhala lopanda chakudya, koma pakakhala ngʼombe zamphamvu zakudya zimachulukanso.
5 A faithful witness does not lie, but a false witness breathes out lies.
Mboni yokhulupirika sinama, koma mboni yonyenga imayankhula zabodza.
6 A mocker seeks wisdom and there is none, but knowledge comes easy to the one who is discerning.
Wonyoza anzake amafunafuna nzeru koma osayipeza, koma munthu womvetsa bwino amadziwa zinthu msanga.
7 Walk away from a foolish person, for you will not find knowledge on his lips.
Khala kutali ndi munthu wopusa chifukwa sudzapeza mawu a nzeru.
8 The wisdom of the prudent person is to understand his own way, but the folly of fools is deception.
Nzeru za munthu wochenjera zagona pakuzindikira njira zake. Koma uchitsiru wa zitsiru umapusitsidwa ndi chinyengo chawo chomwe.
9 Fools mock when the guilt offering is sacrificed, but among the upright favor is shared.
Zitsiru zimanyoza za kulapa machimo, awo, koma kufuna kwabwino kumapezeka mwa anthu olungama.
10 The heart knows its own bitterness and no stranger shares its joy.
Mtima uliwonse umadziwa wokha zowawa zake, ndipo palibe wina aliyense angadziwe kukondwa kwake.
11 The house of wicked people will be destroyed, but the tent of upright people will flourish.
Nyumba ya munthu woyipa idzapasuka, koma tenti ya munthu wowongoka mtima idzakhazikika.
12 There is a way that seems right to a man, but its end only leads to death.
Pali njira ina yooneka ngati yabwino kwa munthu, koma kumatsiriziro kwake ndi ku imfa.
13 A heart can laugh but still be in pain and joy may end up being grief.
Ngakhale poseka mtima utha kumva kuwawa, ndipo mathero achimwemwe akhoza kukhala chisoni.
14 The one who is not faithful will get what his ways deserve, but a good person will get what is his.
Munthu wosakhulupirika adzalandira zogwirizana ndi ntchito yake, koma munthu wabwino adzalandira mphotho ya ntchito yake.
15 The one who is naive believes everything, but the prudent man thinks about his steps.
Munthu wopusa amakhulupirira chilichonse, koma munthu wochenjera amaganizira bwino mayendedwe ake.
16 A wise man fears and turns away from evil, but the fool confidently dismisses a warning.
Munthu wanzeru amaopa Mulungu ndipo amapewa zoyipa, koma munthu wopusa ndi wokula mtima amakhala wosasamala.
17 One who is quick to become angry does foolish things, and a person who makes evil schemes is hated.
Munthu wopsa mtima msanga amachita zinthu za uchitsiru, ndipo anthu amadana ndi munthu wachinyengo.
18 The naive inherit foolishness, but prudent people are crowned with knowledge.
Anthu opusa amalandira uchitsiru, koma anthu ochenjera amavekedwa chipewa cha ulemerero wa kudziwa zinthu.
19 Evil people will bow down before those who are good and those who are wicked will bow down at the gates of the righteous person.
Anthu oyipa adzagwada pamaso pa anthu abwino, ndipo anthu oyipa adzapempha thandizo kwa anthu olungama.
20 The poor person is hated even by his own companions, but the rich people have many friends.
Munthu wosauka ngakhale anansi ake omwe amamuda, koma munthu wolemera ali ndi abwenzi ambiri.
21 The one who shows contempt for his neighbor is sinning, but the one who shows favor to the poor is blessed.
Wonyoza mnansi wake ndi wochimwa koma ndi wodala amene amachitira chifundo anthu osowa.
22 Do not those who plot evil go astray? But those who plan to do good will receive covenant faithfulness and trustworthiness.
Kodi amene amakonzekera zoyipa sasochera? Koma amene amakonzekera zabwino anthu amawaonetsa chikondi ndi kukhulupirika.
23 With all hard work comes a profit, but when there is only talk, it leads to poverty.
Ntchito iliyonse imakhala ndi phindu, koma kuyankhulayankhula kumabweretsa umphawi.
24 The crown of wise people is their wealth, but the folly of fools brings them only more folly.
Chipewa chaulemu cha anthu a nzeru ndi chuma chawo chomwe, koma malipiro a zitsiru ndi uchitsiru.
25 A truthful witness saves lives, but a false witness breathes out lies.
Mboni yokhulupirika imapulumutsa miyoyo, koma mboni yabodza imaphetsa.
26 When someone fears Yahweh, he also has much confidence in him; these things will be like a strong place of protection for this man's children.
Amene amaopa Yehova ali ndi chitetezo chokwanira ndipo iye adzakhala pothawira pa ana ake.
27 The fear of Yahweh is a fountain of life, so that a person may turn away from the snares of death.
Kuopa Yehova ndiye kasupe wamoyo, kumathandiza munthu kuti apewe msampha wa imfa.
28 The glory of a king is found in the great number of his people, but without people the prince is ruined.
Gulu lalikulu la anthu ndiye ulemerero wa mfumu, koma popanda anthu kalonga amawonongeka.
29 A patient person has great understanding, but the quick-tempered person exalts folly.
Munthu wosapsa mtima msanga amamvetsa zinthu kwambiri, koma munthu wopsa mtima msanga amaonetsa uchitsiru wake.
30 A tranquil heart is life for the body, but envy rots the bones.
Mtima wodekha umapatsa thupi moyo, koma nsanje imawoletsa mafupa.
31 The one who oppresses the poor curses his Maker, but the one who shows favor to the needy honors him.
Amene amapondereza mʼmphawi amanyoza mlengi wake, koma wochitira chifundo munthu wosowa amalemekeza Mulungu.
32 The wicked person is brought down by his evil actions, but the righteous person has a refuge even in death.
Anthu oyipa adzakanthidwa chifukwa cha ntchito zawo zomwe, koma olungama adzatetezedwa mwa imfa yawo.
33 Wisdom rests in the heart of the discerning, but even among fools she lets herself be known.
Nzeru zimakhala mu mtima mwa anthu omvetsa zinthu, koma nzeru sipezeka mu mtima mwa zitsiru.
34 Doing what is right exalts a nation, but sin is a disgrace to any people.
Chilungamo chimakweza mtundu wa anthu, koma uchimo umachititsa manyazi mtundu uliwonse.
35 The favor of the king is with the servant who acts prudently, but his anger is for the one who acts shamefully.
Mfumu imasangalatsidwa ndi wantchito wanzeru, koma imachitira ukali wantchito wochititsa manyazi.