< Proverbs 10 >

1 The proverbs of Solomon. A wise son makes his father rejoice but a foolish son brings grief to his mother.
Miyambo ya Solomoni: Mwana wanzeru amakondweretsa abambo ake, koma mwana wopusa amamvetsa amayi ake chisoni.
2 Treasures accumulated by wickedness have no value, but doing what is right keeps you from death.
Chuma chochipeza mwachinyengo sichipindulitsa, koma chilungamo chimapulumutsa ku imfa.
3 Yahweh does not let the soul of the righteous person go hungry, but he frustrates the cravings of the wicked.
Yehova salola kuti munthu wolungama azikhala ndi njala; koma amalepheretsa zokhumba za anthu oyipa.
4 A lazy hand causes a person to be poor, but the hand of the diligent person gains riches.
Wochita zinthu mwaulesi amasauka, koma wogwira ntchito mwakhama amalemera.
5 A wise son gathers a crop in the summer, but it is disgraceful for him to sleep during harvest.
Amene amakolola nthawi yachilimwe ndi mwana wanzeru, koma amene amangogona nthawi yokolola ndi mwana wochititsa manyazi.
6 Gifts from God are upon the head of the righteous person, but the mouth of the wicked covers up violence.
Madalitso amakhala pa mutu wa munthu wolungama, koma pakamwa pa munthu woyipa pamaphimba chiwawa.
7 The righteous person makes those who remember him happy, but the name of the wicked will rot away.
Munthu wolungama anzake adzamukumbukira ngati mdalitso, koma dzina la munthu woyipa lidzayiwalika.
8 Those who are sensible accept commands, but a talkative fool will come to ruin.
Munthu wa mtima wanzeru amasamala malamulo, koma chitsiru chomangolongolola chidzawonongeka.
9 He who walks in integrity walks in safety, but the one who makes his ways crooked, he will be found out.
Munthu woyenda mwangwiro amayenda mosatekeseka; koma amene amayenda njira yokhotakhota adzadziwika.
10 He who winks the eye causes grief, but a talkative fool will be thrown down.
Aliyense wotsinzinira maso mwachinyengo amabweretsa mavuto, koma wodzudzula chitsiru molimba mtima amabweretsa mtendere.
11 The mouth of the righteous person is a water spring of life, but the mouth of the wicked covers up violence.
Pakamwa pa munthu wolungama ndi kasupe wamoyo, koma pakamwa pa munthu woyipa pamabisa chiwawa.
12 Hatred stirs up conflicts, but love covers over all offenses.
Udani umawutsa mikangano, koma chikondi chimaphimba zolakwa zonse.
13 Wisdom is found on the lips of a discerning person, but a rod is for the back of the one who has no sense.
Nzeru imapezeka pa milomo ya munthu wozindikira zinthu, koma pa msana pa munthu wopanda nzeru sipachoka chikwapu.
14 Wise men store up knowledge, but the mouth of a fool brings destruction near.
Anzeru amasunga chidziwitso koma pakamwa pa chitsiru pamatulutsa zowononga.
15 The wealth of a rich man is his fortified city; the poverty of the poor is their destruction.
Chuma cha munthu wolemera ndiye chitetezo chake; koma umphawi ndiye chiwonongeko cha osauka.
16 The wage of the righteous person leads to life; the profit of the wicked leads them to sin.
Moyo ndiye malipiro a munthu wolungama, koma phindu la anthu oyipa ndi uchimo ndi imfa.
17 There is a path to life for the one who follows discipline, but the one who rejects correction is led astray.
Wosamalira malangizo amayenda mʼnjira ya moyo, koma wonyoza chidzudzulo amasochera.
18 Whoever conceals hatred has lying lips, and whoever spreads slander is a fool.
Amene amabisa chidani chake ndi munthu wonama, ndipo amene amafalitsa miseche ndi chitsiru.
19 When there are many words, transgression is not lacking, but he who is careful in what he says is wise.
Mawu akachuluka zolakwa sizisowa, koma amene amasunga pakamwa pake ndi wanzeru.
20 The tongue of the righteous person is pure silver; there is little value in the heart of the wicked.
Mawu a munthu wolungama ali ngati siliva wabwino kwambiri, koma mtima wa munthu woyipa ndi wopanda phindu.
21 The lips of the righteous person nourish many, but fools die because of their lack of sense.
Milomo ya anthu olungama imalimbikitsa ambiri; koma chitsiru chimafa chifukwa chosowa nzeru.
22 The good gifts of Yahweh bring wealth and he adds no pain to it.
Mdalitso wa Yehova ndiwo umabweretsa chuma, ntchito za munthu siziwonjezerapo kanthu.
23 Wickedness is a game a fool plays, but wisdom is a pleasure to a man of understanding.
Kwa chitsiru kuchita zinthu zoyipa ndiye chinthu chomusangalatsa, koma kwa munthu womvetsa bwino zinthu nzeru ndiyo imamusangalatsa.
24 The fear of the wicked person will overtake him, but the desire of righteous people will be granted.
Chimene munthu woyipa amachiopa chidzamuchitikira; chimene munthu wolungama amachilakalaka adzachipeza.
25 The wicked are like the storm that passes by, and they are no more, but the righteous person is a foundation that lasts forever.
Pamene namondwe wawomba, anthu oyipa amachotsedwa, koma anthu olungama amakhazikika mpaka muyaya.
26 Like vinegar on the teeth and smoke in the eyes, so is the sluggard to those who send him.
Momwe amakhalira vinyo wosasa mʼkamwa ndi momwe umakhalira utsi mʼmaso, ndi momwenso amakhalira munthu waulesi kwa amene amutuma.
27 The fear of Yahweh prolongs life, but the years of the wicked will be short.
Kuopa Yehova kumatalikitsa moyo; koma zaka za anthu oyipa zidzafupikitsidwa.
28 The hope of righteous people is their joy, but the years of wicked people will be short.
Chiyembekezo cha olungama chimapatsa chimwemwe, koma chiyembekezo cha anthu ochimwa chidzafera mʼmazira.
29 The way of Yahweh protects those who have integrity, but it is destruction for the wicked.
Njira za Yehova ndi linga loteteza anthu ochita zabwino, koma wochita zoyipa adzawonongeka.
30 The righteous person will never be overthrown, but the wicked will not remain in the land.
Munthu wolungama sadzachotsedwa, pamalo pake koma oyipa sadzakhazikika pa dziko.
31 Out of the mouth of the righteous person comes the fruit of wisdom, but the perverse tongue will be cut out.
Pakamwa pa munthu wolungama pamatulutsa za nzeru, koma lilime lokhota lidzadulidwa.
32 The lips of the righteous person know what is acceptable, but the mouth of the wicked, they know what is perverse.
Milomo ya anthu olungama imadziwa zoyenera kuyankhula, koma pakamwa pa anthu ochimwa pamatulutsa zokhota zokhazokha.

< Proverbs 10 >