< Numbers 25 >

1 Israel stayed in Shittim, and the men began to prostitute themselves with women of Moab,
Aisraeli akukhala ku Sitimu, anayamba kuchita chigololo ndi akazi a ku Mowabu,
2 for the Moabites had invited the people to the sacrifices to their gods. So the people ate and bowed down to Moabite gods.
amene ankawayitana ku nsembe za milungu yawo. Anthuwo anadya chakudya chopereka kwa milungu ndi kupembedza milunguyo.
3 The men of Israel joined in worshiping Baal of Peor, and Yahweh's anger was kindled against Israel.
Motero Aisraeli anapembedza nawo Baala-Peori ndipo Yehova anawapsera mtima kwambiri.
4 Yahweh said to Moses, “Kill all the leaders of the people and hang them up before me to expose them in the daylight, so that my fierce anger may turn away from Israel.”
Pamenepo Yehova anawuza Mose kuti, “Tenga atsogoleri onse a anthu awa, uwaphe poyera, pamaso pa Yehova kuti mkwiyo waukulu wa Yehova uchoke pa Israeli.”
5 So Moses said to Israel's leaders, “Each of you must execute his people who have joined in worshiping Baal of Peor.”
Choncho Mose anawuza oweruza a Israeli kuti, “Aliyense wa inu ayenera kupha anthu ake amene anapembedza nawo Baala-Peori.”
6 Then one of the men of Israel came and brought among his family members a Midianite woman. This happened in the sight of Moses and all the community of the people of Israel, while they were weeping at the entrance to the tent of meeting.
Kenaka mwamuna wina wa ku Israeli anabweretsa ku banja lake mkazi wa Chimidiyani pamaso pa Mose ndi anthu onse a Israeli pamene ankalira pa khomo la tenti ya msonkhano.
7 When Phinehas son of Eleazar son of Aaron the priest, saw that, he rose up from among the community and took a spear in his hand.
Finehasi mwana wa Eliezara, mwana wa wansembe Aaroni ataona izi, anachoka pa msonkhanowo, natenga mkondo mʼdzanja lake.
8 He followed the Israelite man into the tent and thrust the spear through both of their bodies, both the Israelite man and the woman. So a plague that God had sent on the people of Israel stopped.
Ndipo anatsatira Mwisraeliyu mpaka mʼtenti yake. Anasolola mkondowo ndi kubaya awiriwo kupyola Mwisraeliyo mpaka mʼthupi la mkaziyo. Pamenepo mliri unaleka pakati pa Aisraeli.
9 Those who died by the plague were twenty-four thousand in number.
Pa mliriwo, anthu okwana 24,000 anafa.
10 Yahweh spoke to Moses and said,
Yehova anawuza Mose kuti,
11 “Phinehas son of Eleazar son of Aaron the priest, has turned my rage away from the people of Israel because he was passionate with my zeal among them. So I have not consumed the people of Israel in my fierceness.
“Finehasi mwana wa Eliezara, mwana wa wansembe Aaroni wabweza mkwiyo wanga pa Aisraeli chifukwa sanalole kuti wina aliyense apembedze mulungu wina koma Ine ndekha. Nʼchifukwa chake sindinawawononge mu mkwiyo wanga.
12 Therefore say, 'Yahweh says, “Look, I am giving to Phinehas my covenant of peace.
Tsono muwuze kuti ndikhazikitsa pangano langa la mtendere ndi iye.
13 For him and his descendants after him, it will be a covenant of an everlasting priesthood because he was zealous for me, his God. He has atoned for the people of Israel.”'”
Ndikupangana naye pangano la unsembe wosatha, iyeyo pamodzi ndi zidzukulu zake zonse, chifukwa sanalole kuti anthu awukire Ine Mulungu, ndipo anachita ntchito yopepesera machimo Aisraeli.”
14 Now the name of the Israelite man who was killed with the Midianite woman was Zimri son of Salu, a leader of an ancestor's family among the Simeonites.
Dzina la Mwisraeli yemwe anaphedwa ndi mkazi wa Chimidiyani anali Zimuri mwana wa Salu, mtsogoleri wa banja la Simeoni.
15 The name of the Midianite woman who was killed was Kozbi daughter of Zur, who was head of a tribe and family in Midian.
Ndipo dzina la mkazi wa Chimidiyani, yemwe anaphedwayo, linali Kozibi mwana wa Zuri, mtsogoleri wa fuko la ku Midiyaniko.
16 So Yahweh spoke to Moses and said,
Yehova anawuza Mose kuti,
17 “Treat the Midianites as enemies and attack them,
“Amidiyani ndi adani anu ndipo uwaphe,
18 for they treated you like enemies with their deceitfulness. They led you into evil in the case of Peor and in the case of their sister Kozbi, the daughter of a leader in Midian, who was killed on the day of the plague in the matter of Peor.”
chifukwa ankakuonani inu ngati adani awo pamene anakupusitsani pa nkhani ya ku Peori, ndiponso za mlongo wawo Kozibi, mwana wamkazi wa mtsogoleri wa Amidiyani, mkazi yemwe anaphedwa pamene mliri unabwera chifukwa cha zimene zinachitika ku Peori.”

< Numbers 25 >