< Nahum 3 >
1 Woe to the city full of blood! It is all full of lies and stolen property; victims are always in her.
Tsoka kwa mzinda wopha anthu, mzinda wodzaza ndi mabodza, mzinda wodzaza ndi anthu olanda zinthu anzawo, mu mzinda mʼmene simusowa anthu osautsidwa nthawi zonse!
2 But now there is the noise of whips and the sound of rattling wheels, prancing horses, and bounding chariots.
Kulira kwa zikwapu, mkokomo wa mikombero, kufuwula kwa akavalo ndiponso phokoso la magaleta!
3 There are attacking horsemen, flashing swords, glittering spears, heaps of corpses, great piles of bodies. There is no end to the bodies; their attackers stumble over them.
Kuthamanga kwa anthu okwera pa akavalo, kungʼanima kwa malupanga ndi kunyezimira kwa mikondo! Anthu ambiri ophedwa, milumilu ya anthu akufa, mitembo yosawerengeka, anthu akupunthwa pa mitemboyo.
4 This is happening because of the lustful actions of the beautiful prostitute, the expert in witchcraft, who sells nations through her prostitution, and peoples through her acts of witchcraft.
Zonsezi ndi chifukwa cha zilakolako za mkazi wachiwerewere, wokopa anthu uja, mkazi wochita zamatsenga, amene anakopa mitundu ya anthu ndi zachiwerewere zake, ndiponso anthu a mitundu ina ndi zaufiti zake.
5 “See, I am against you—this is the declaration of Yahweh of hosts—I will raise up your skirt over your face and show your private parts to the nations, your shame to the kingdoms.
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ine ndikutsutsana nawe. Ndidzakuvula chovala chako. Anthu a mitundu ina ndidzawaonetsa umaliseche wako ndipo udzachita manyazi pamaso pa maufumu onse.
6 I will throw disgusting filth on you and make you vile; I will make you someone that everyone will look at.
Ndidzakuthira zonyansa, ndidzakuchititsa manyazi ndiponso kukusandutsa chinthu choseketsa.
7 It will come about that everyone who looks at you will flee from you and say, 'Nineveh is destroyed; who will weep for her?' Where can I find anyone to comfort you?”
Onse amene adzakuona adzakuthawa ndipo adzati, ‘Ninive wasanduka bwinja, adzamulira ndani?’ Kodi ndingamupeze kuti munthu woti nʼkukutonthoza?”
8 Nineveh, are you better than Thebes, that was built on the Nile River, that had water around her, whose defense was the ocean, whose wall was the sea itself?
Kodi ndiwe wopambana Tebesi, mzinda wokhala mʼmbali mwa Nailo, wozunguliridwa ndi madzi? Mtsinjewo unali chitetezo chake, madziwo anali linga lake.
9 Cush and Egypt were her strength, and there was no end to it; Put and Libya were allies to her.
Mphamvu zake zinali Kusi ndi Igupto, Puti ndi Libiya anali ena mwa abwenzi ake.
10 Yet Thebes was carried away; she went into captivity; her young children were dashed in pieces at the head of every street; her enemies threw lots for her honorable men, and all her great men were bound in chains.
Komabe anthu a ku Tebesi anagwidwa ndipo anapita ku ukapolo. Ana ake anawaphwanyitsa pansi mʼmisewu yonse ya mu mzindamo. Anachita maere ogawana anthu ake otchuka, ndipo anthu ake onse amphamvu anamangidwa ndi maunyolo.
11 You also will become drunk; you will try to hide, and you will also look for a refuge from your enemy.
Iwenso Ninive udzaledzera; udzabisala ndipo udzafunafuna malo othawirako kuopa mdani.
12 All your fortresses will be like fig trees with the earliest ripe figs: if they are shaken, they fall into the mouth of the eater.
Malo ako onse otetezedwa ali ngati mitengo ya mkuyu yokhala ndi zipatso zoyambirira kucha; pamene agwedeza mitengoyo, nkhuyuzo zimagwera mʼkamwa mwa wofuna kuzidya.
13 See, the people among you are women; the gates of your land have been opened wide to your enemies; fire has devoured their bars.
Tayangʼana ankhondo ako, onse ali ngati akazi! Zipata za dziko lako zatsekukira adani ako; moto wapsereza mipiringidzo yake.
14 Go draw water for the siege; strengthen your fortresses; go into the clay and tread the mortar; pick up the molds for the bricks.
Tungani madzi woti mudzamwe nthawi ya kuzunguliridwa kwanu, limbitsani chitetezo chanu! Pondani dothi, ikani mʼchikombole, konzani khoma la njerwa!
15 Fire will devour you there, and the sword will destroy you. It will devour you as young locusts devour everything. Make yourselves as many as the young locusts, as many as the full-grown locusts.
Kumeneko moto udzakupserezani; lupanga lidzakukanthani ndipo lidzakuwonongani ngati likuwononga ziwala. Chulukanani ngati ziwala, chulukanani ngati dzombe!
16 You have multiplied your merchants more than the stars in the heavens; but they are like young locusts: they plunder the land and then fly away.
Mwachulukitsa chiwerengero cha anthu a malonda anu mpaka kupambana nyenyezi za mlengalenga, koma iwo ngati dzombe akuwononga dziko ndipo kenaka akuwuluka nʼkuchoka.
17 Your princes are as many as the full-grown locusts, and your generals are like swarms of them that camp in the walls on a cold day. But when the sun rises they fly away to no one knows where.
Akalonga ako ali ngati dzombe, akuluakulu ako ali ngati gulu la dzombe limene lamatirira pa khoma nthawi yozizira, koma pamene dzuwa latuluka limawuluka, ndipo palibe amene amadziwa komwe lapita.
18 King of Assyria, your shepherds are asleep; your rulers are lying down resting. Your people are scattered on the mountains, and there is no one to gather them.
Iwe mfumu ya ku Asiriya, abusa ako agona tulo; anthu ako olemekezeka amwalira. Anthu ako amwazikira ku mapiri popanda ndi mmodzi yemwe wowasonkhanitsa.
19 No healing is possible for your wounds. Your wounds are severe. Everyone who hears the news about you will clap their hands in joy over you. Who has escaped your constant wickedness?
Palibe chimene chingachize bala lako; chilonda chako sichingapole. Aliyense amene amamva za iwe amawomba mʼmanja chifukwa cha kugwa kwako, kodi alipo amene sanazilawepo nkhanza zako zosatha?