< Micah 7 >

1 Woe is me! I have become like the gathering of summer fruit, and like the grapes that have been gleaned; there is no grape cluster to eat, no ripe early fig that my soul desires.
Tsoka ine! Ndili ngati munthu wokunkha zipatso nthawi yachilimwe, pa nthawi yokolola mphesa; palibe phava lamphesa loti nʼkudya, palibe nkhuyu zoyambirira zimene ndimazilakalaka kwambiri.
2 Faithful people have disappeared from the land; there is no upright person in all mankind. They all lie in wait to shed blood; each one hunts his own brother with a net.
Anthu opembedza atha mʼdziko; palibe wolungama ndi mmodzi yemwe amene watsala. Anthu onse akubisalirana kuti aphane; aliyense akusaka mʼbale wake ndi khoka.
3 Their hands are very good at doing harm: the ruler asks for money, the judge is ready for bribes, and the powerful man is saying to others what he wants to obtain. Thus they plot together.
Manja awo onse ndi aluso pochita zoyipa; wolamulira amafuna mphatso, woweruza amalandira ziphuphu, anthu amphamvu amalamula kuti zichitike zimene akuzifuna, onse amagwirizana zochita.
4 The best of them is like a brier, the most upright is worse than a thorn hedge. It is the day foretold by your watchmen, the day of your punishment. Now is the time of their confusion.
Munthu wabwino kwambiri pakati pawo ali ngati mtengo waminga, munthu wolungama kwambiri pakati pawo ndi woyipa kuposa mpanda waminga. Tsiku limene alonda ako ananena lafika, tsiku limene Mulungu akukuchezera. Tsopano ndi nthawi ya chisokonezo chawo.
5 Do not trust any neighbor; put no confidence in any friend. Be careful about what you say even to the woman who lies in your arms.
Usadalire mnansi; usakhulupirire bwenzi. Usamale zoyankhula zako ngakhale kwa mkazi amene wamukumbatira.
6 For a son dishonors his father, a daughter rises up against her mother, and a daughter-in-law against her mother-in-law. A man's enemies are the people of his own house.
Pakuti mwana wamwamuna akunyoza abambo ake, mwana wamkazi akuwukira amayi ake, mtengwa akukangana ndi apongozi ake, adani a munthu ndi amene amakhala nawo mʼbanja mwake momwe.
7 But as for me, I will look to Yahweh. I will wait for the God of my salvation; my God will hear me.
Koma ine ndikudikira Yehova mwachiyembekezo, ndikudikira Mulungu Mpulumutsi wanga; Mulungu wanga adzamvetsera.
8 Do not rejoice over me, my enemy. After I fall, I will rise. When I sit in darkness, Yahweh will be a light for me.
Iwe mdani wanga, usandiseke! Ngakhale ndagwa, ndidzauka. Ngakhale ndikukhala mu mdima, Yehova ndiye kuwunika kwanga.
9 Because I sinned against Yahweh, I will bear his rage until he pleads my cause, and executes judgment for me. He will bring me to the light, and I will see him rescue me in his justice.
Ndidzapirira mkwiyo wa Yehova, chifukwa ndinamuchimwira, mpaka ataweruza mlandu wanga ndi kukhazikitsa chilungamo changa. Iye adzanditulutsa ndi kundilowetsa mʼkuwunika; ndidzaona chilungamo chake.
10 Then my enemy will see it, and shame will cover the one who said to me, “Where is Yahweh your God?” My eyes will look at her; she will be trampled down like the mud in the streets.
Ndipo mdani wanga adzaona zimenezi nadzagwidwa ndi manyazi, iye amene anandifunsa kuti, “Ali kuti Yehova Mulungu wako?” Ndidzaona kugonjetsedwa kwake ndi maso anga; ngakhale tsopano adzaponderezedwa ngati matope mʼmisewu.
11 A day to build your walls will come; on that day the boundaries will be extended very far.
Idzafika nthawi yomanganso makoma anu, nthawi yokulitsanso malire anu.
12 On that day your people will come to you, from Assyria and the cities in Egypt, from Egypt to the River, from sea to sea, and from mountain to mountain.
Nthawi imeneyo anthu adzabwera kwa inu kuchokera ku Asiriya ndi mizinda ya ku Igupto, ngakhale kuchokera ku Igupto mpaka ku Yufurate ndiponso kuchokera ku nyanja ina mpaka ku nyanja inanso kuchokera ku phiri lina mpaka ku phiri linanso.
13 But the land will be desolate because of the people who are living there, because of the fruit of their actions.
Dziko lapansi lidzasanduka chipululu chifukwa cha anthu okhala mʼdzikomo, potsatira zochita za anthuwo.
14 Shepherd your people with your rod, the flock of your inheritance. They live alone in a thicket, in the midst of a pastureland. Let them graze in Bashan and Gilead as in the old days.
Wetani anthu anu ndi ndodo yanu yowateteza, nkhosa zimene ndi cholowa chanu, zimene zili zokha mʼnkhalango, mʼdziko la chonde. Muzilole kuti zidye mu Basani ndi mu Giliyadi monga masiku akale.
15 As in the days when you came out of the land of Egypt, I will show them wonders.
“Ndidzawaonetsa zodabwitsa zanga, ngati masiku amene ndinawatulutsa mʼdziko la Igupto.”
16 The nations will see and be ashamed of all their power. They will put their hands on their mouths; their ears will be deaf.
Mitundu ya anthu idzaona zimenezi ndipo idzachita manyazi, ngakhale ali ndi mphamvu zotani. Adzagwira pakamwa pawo ndipo makutu awo adzagontha.
17 They will lick the dust like a snake, like creatures that crawl on the earth. They will come out of their dens with fear; they will come with fear to you, Yahweh our God, and they will be afraid because of you.
Adzabwira fumbi ngati njoka, ngati zolengedwa zomwe zimakwawa pansi. Adzabwera akunjenjemera kuchokera mʼmaenje awo; mwamantha adzatembenukira kwa Yehova Mulungu wathu ndipo adzachita nanu mantha.
18 Who is a God like you— who takes away sin, who passes over the transgression of the remnant of his inheritance? He does not keep his anger forever, because he delights in his covenant faithfulness.
Kodi alipo Mulungu wofanana nanu, amene amakhululukira tchimo ndi kuyiwala zolakwa za anthu otsala amene ndi cholowa chake? Inu simusunga mkwiyo mpaka muyaya koma kwanu nʼkuonetsa chikondi chosasinthika.
19 You will again have compassion on us; you will trample our iniquities under your feet. You will throw all our sins into the depths of the sea.
Inu mudzatichitiranso chifundo; mudzapondereza pansi machimo athu ndi kuponyera zolakwa zathu zonse pansi pa nyanja.
20 You will give truth to Jacob and covenant faithfulness to Abraham, as you swore to our ancestors in ancient days.
Mudzakhala wokhulupirika kwa Yakobo, ndi kuonetsa chifundo chanu kwa Abrahamu, monga munalonjeza molumbira kwa makolo athu masiku amakedzana.

< Micah 7 >