< Leviticus 17 >
1 Yahweh spoke to Moses, saying,
Yehova anawuza Mose kuti,
2 “Speak to Aaron and to his sons, and to all the people of Israel. Tell them what Yahweh has commanded:
“Uza Aaroni ndi ana ake, pamodzi ndi Aisraeli onse kuti, ‘Chimene Yehova walamula ndi ichi:
3 'Any man from Israel who kills an ox, lamb, or goat in the camp, or who kills it outside the camp, in order to sacrifice it—
Mwisraeli aliyense amene apha ngʼombe, mwana wankhosa kapena mbuzi mu msasa kapena kunja kwa msasa,
4 if he does not bring it to the entrance of the tent of meeting to offer it as a sacrifice to Yahweh before his tabernacle, that man is guilty of bloodshed. He has shed blood, and that man must be cut off from among his people.
mʼmalo mobwera nayo pa khomo la tenti ya msonkhano pamaso pa Yehova ndi kuyipereka kuti ikhale nsembe ya Yehova, ameneyo wapalamula mlandu wa magazi, wakhetsa magazi ndipo ayenera kuchotsedwa pakati pa anthu anzake.
5 The purpose of this command is so that the people of Israel will bring their sacrifices to Yahweh at the entrance to the tent of meeting, to the priest to be sacrificed as fellowship offerings to Yahweh, instead of offering sacrifices in an open field.
Izi zili choncho kuti Aisraeli azibwera ndi nyama zawo za nsembe zimene akanaphera ku malo kwina kulikonse. Aisraeli azibwera nazo nyamazo kwa Yehova, kwa wansembe wokhala pa khomo la tenti ya msonkhano ndipo aziphere pomwepo kuti zikhale nsembe za chiyanjano.
6 The priest will sprinkle the blood on Yahweh's altar at the entrance to the tent of meeting; he will burn the fat for it to produce a sweet aroma for Yahweh.
Wansembe awaze magazi ake pa guwa la Yehova limene lili pa khomo la tenti ya msonkhano ndipo atenthe mafuta ake kuti atulutse fungo lokomera Yehova.
7 The people must no longer offer their sacrifices to goat idols, for which they act as prostitutes. This will be a permanent statute for them throughout their people's generations.'
Motero asadzapherenso nsembe fano la mbuzi limene amachita nalo zadama. Limeneli ndi lamulo la muyaya kwa iwo ndi mibado ya mʼtsogolo.’”
8 You must say to them, 'Any man of Israel, or any foreigner who lives among them, who offers a burnt offering or sacrifice
“Uwawuze kuti, ‘Mwisraeli aliyense kapena mlendo amene amakhala pakati pawo akapereka nsembe yopsereza kapena nsembe ina iliyonse
9 and does not bring it to the entrance of the tent of meeting in order to sacrifice it to Yahweh, that man must be cut off from his people.
popanda kubwera nayo pa khomo la tenti ya msonkhano kudzayipereka pamaso pa Yehova, munthu ameneyo achotsedwe pakati pa anthu anzake.’”
10 If any person of the house of Israel, or any foreigner who lives among them consumes any blood, I will set my face against that person who consumes blood and I will cut him off from among his people.
“Mwisraeli aliyense kapena mlendo aliyense wokhala pakati panu amene adya magazi, ndidzamufulatira ndipo ndidzamuchotsa pakati pa anthu anzake.
11 For the life of an animal is in its blood. I have given its blood to you to make atonement on the altar for your lives, because it is the blood that makes atonement, for it is the blood that atones for the life.
Pakuti moyo wa cholengedwa chilichonse uli mʼmagazi, ndipo ndawupereka kwa inu kuti muzichitira mwambo wopepesera machimo a moyo wanu pa guwa. Pajatu magazi ndiwo amachotsa machimo chifukwa moyo uli mʼmenemo.
12 Therefore I said to the people of Israel that no one among you must eat blood, neither may any foreigner who lives among you eat blood.
Choncho ndikuwawuza Aisraeli kuti, ‘Pasapezeke aliyense wa inu wodya magazi, ngakhale mlendo wokhala pakati panu.’”
13 Anyone of the people of Israel, or any of the foreigners who live among them, who hunts and kills an animal or bird that may be eaten, that person must pour out its blood and cover the blood with earth.
“Mwisraeli aliyense kapena mlendo aliyense wokhala pakati panu amene amasaka ndi kupha nyama zakuthengo kapena mbalame zimene amadya, ataye magazi ake pansi ndi kuwakwirira ndi dothi,
14 For the life of each creature is its blood. That is why I said to the people of Israel, “You must not eat the blood of any creature, for the life of every living creature is its blood. Whoever eats it must be cut off.”
chifukwa moyo wa cholengedwa chilichonse uli mʼmagazi ake. Nʼchifukwa chake ndinawawuza Aisraeli kuti, ‘Musamadye magazi a cholengedwa chilichonse, chifukwa moyo wa cholengedwa chilichonse uli mʼmagazi. Aliyense wodya magaziwo ayenera kuchotsedwa pakati pa anthu anzake.
15 Every person who eats an animal that has died or that has been torn by wild animals, whether that person is native born or a foreigner living among you, he must wash his clothes and bathe himself in water, and he will be unclean until the evening. Then he will be clean.
“‘Munthu aliyense, kaya ndi mbadwa kapena mlendo, amene amadya chilichonse chofa chokha, kapena chojiwa ndi zirombo, achape zovala zake ndi kusamba, komabe adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo. Kenaka adzakhala woyeretsedwa.
16 But if he does not wash his clothes or bathe his body, then he must carry his guilt.'”
Koma ngati sachapa zovala zake ndi kusamba, adzasenzabe machimo ake.’”