< Judges 11 >

1 Now Jephthah the Gileadite was a mighty warrior, but he was the son of a prostitute. Gilead was his father.
Yefita wa ku Giliyadi anali wankhondo wa mphamvu. Iyeyu amayi ake anali mkazi wachiwerewere, ndipo abambo ake anali Giliyadi.
2 Gilead's wife also gave birth to his other sons. When his wife's sons grew up, they forced Jephthah to leave the house and said to him, “You are not going to inherit anything from our family. You are the son of another woman.”
Mkazi wake wa Giliyadi anabereka naye ana aamuna. Tsono ana amenewa atakula anapirikitsa Yefita ndi kumuwuza kuti, “Sudzalandirako cholowa mʼnyumba ya abambo athu chifukwa ndiwe mwana wa mkazi wina.”
3 So Jephthah fled from his brothers and lived in the land of Tob. Lawless men joined Jephthah and they came and went with him.
Choncho Yefita anathawa kuchoka kwa abale ake ndi kukakhala mʼdziko la Tobu. Kumeneko anakakopa ndi kusonkhanitsa anthu achabechabe ndipo anatuluka pamodzi kukasakaza zinthu.
4 Some days later, the people of Ammon made war against Israel.
Patapita nthawi Aamoni anadzachita nkhondo ndi Israeli.
5 When the people of Ammon made war against Israel, the elders of Gilead went to bring Jephthah back from the land of Tob.
Tsono pamene Aamoni ankathira nkhondo Aisraeli, akuluakulu a ku Giliyadi anapita kukamutenga Yefita ku dziko la Tobu.
6 They said to Jephthah, “Come and be our leader that we may fight with the people of Ammon.”
Iwo anati kwa iye, “Bwera ukhale mkulu wathu wankhondo kuti timenyane ndi Amoni.”
7 Jephthah said to the leaders of Gilead, “You hated me and forced me to leave my father's house. Why do you come to me now when you are in trouble?”
Yefita anawawuza Agiliyadi kuti, “Kodi inu suja munkadana nane ndi kundithamangitsa ku nyumba ya abambo anga? Nʼchifukwa chiyani lero mwabwera kwa ine pamene muli pa mavuto?”
8 The elders of Gilead said to Jephthah, “That is why we are turning to you now; come with us and fight with the people of Ammon, and you will become the leader over all who live in Gilead.”
Akuluakulu a ku Giliyadi aja anamuyankha kuti, “Chimene tabwerera kwa iwe ndi chakuti upite nafe kukamenyana ndi Aamoni, ndipo udzakhala wolamulira wa onse okhala mu Giliyadi.”
9 Jephthah said to the elders of Gilead, “If you bring me home again to fight against the people of Ammon, and if Yahweh gives us victory over them, I will be your leader.”
Yefita anawayankha akuluakulu a ku Giliyadi kuti, “Ngati mundibwezeranso kwathu kuti ndikachite nkhondo ndi Aamoni ndipo Yehova nʼkukandithandiza kuwagonjetsa, ndidzakhaladi wokulamulirani?”
10 The elders of Gilead said to Jephthah, “May Yahweh be witness between us if we do not do as we say!”
Akuluakulu a ku Giliyadi anamuyankha kuti, “Yehova akhale mboni pakati pa inu ndi ife, ngati sitidzachita monga mwa mawu anu.”
11 So Jephthah went with the elders of Gilead, and the people made him leader and commander over them. When he was before Yahweh in Mizpah, Jephthah repeated all the promises he made.
Choncho Yefita anapita nawo akuluakulu a ku Giliyadi aja, ndipo anthu a kumeneko anamusandutsa kukhala wowalamulira ndi mkulu wankhondo. Tsono Yefita anabwerezanso mawu omwewa pamaso pa Yehova ku Mizipa.
12 Then Jephthah sent messengers to the king of the people of Ammon, saying, “What is this conflict between us? Why have you come with force to take our land?”
Kenaka Yefita anatuma amithenga kwa mfumu ya Aamoni ndi funso lakuti, “Kodi ife takuchimwirani chiyani kuti muzichita nkhondo ndi dziko langa?”
13 The king of the people of Ammon answered to the messengers of Jephthah, “Because when Israel came up out of Egypt, they seized my land from the Arnon to the Jabbok, over to the Jordan. Now give back those lands in peace.”
Ndipo mfumu ya Aamoni inayankha amithenga a Yefita aja kuti, “Pamene Israeli amatuluka kuchokera mu Igupto, analanda dziko langa kuyambira ku mtsinje wa Arinoni mpaka ku mtsinje wa Yaboki mpakanso ku mtsinje wa Yorodani. Tsopano mundibwezere dziko langa mwamtendere.”
14 Again Jephthah sent messengers to the king of the people of Ammon,
Yefita anatumizanso amithenga akewo kwa mfumu ya Aamoni
15 and he said, “This is what Jephthah says: Israel did not take the land of Moab and the land of the people of Ammon,
kukanena kuti, Yefita akuti, “Israeli sanalande dziko la Mowabu kapena dziko la Aamoni.
16 but they came up from Egypt, and Israel went through the wilderness to the Sea of Reeds and on to Kadesh.
Koma pamene Aisraeli ankachoka ku Igupto anadzera njira ya ku chipululu mpaka ku Nyanja Yofiira nakafika ku Kadesi.
17 When Israel sent messengers to the king of Edom, saying, 'Please let us pass through your land,' the king of Edom would not listen. They also sent messengers to the king of Moab, but he refused. So Israel stayed at Kadesh.
Kenaka Israeli anatumiza amithenga kwa mfumu ya ku Edomu kuti, ‘Chonde tiloleni kuti tidutse mʼdziko lanu,’ Koma mfumu ya ku Edomu sinamvere zimenezo. Aisraeli anatumizanso amithenga kwa mfumu ya ku Mowabu, ndipo iyo inakananso. Choncho Israeli anakhala ku Kadesi.
18 Then they went through the wilderness and turned away from the land of Edom and the land of Moab, and they went along the east side of the land of Moab and they camped on the other side of the Arnon. But they did not go into the territory of Moab, for the Arnon was Moab's border.
“Pambuyo pake, Aisraeli ananyamuka ulendo kudzera ku chipululu nazungulira dziko la Edomu ndi dziko la Mowabu, ndipo anafika ku mmawa kwa dziko la Mowabu ndi kumanga zinthando zawo ku mbali ina ya mtsinje wa Arinoni. Iwo sanalowe mʼdziko la Mowabu, chifukwa mtsinje wa Arinoni ndiwo unali malire a dziko la Mowabu.
19 Israel sent messengers to Sihon, king of the Amorites, who ruled in Heshbon; Israel said to him, 'Please, let us pass through your land to the place that is ours.'
“Pambuyo pake Israeli anatumiza amithenga kwa Sihoni mfumu ya Aamori, amene amalamulira ku Hesiboni ndipo anati kwa iye, ‘Chonde tiloleni kuti tidutse mʼdziko lanu popita kwathu.’
20 But Sihon did not trust Israel to pass through his territory. So Sihon gathered all his army together and moved it to Jahaz, and there he fought against Israel.
Koma Sihoni sanalole Israeli kuti adzere mʼdziko mwake. Mʼmalo mwake Sihoni anasonkhanitsa ankhondo ake onse nakamanga msasa ku Yahazi ndipo anachita nkhondo ndi Israeli.
21 Then Yahweh, the God of Israel, gave Sihon and all his people into the hand of Israel and they defeated them. So Israel took all the land of the Amorites who lived in that country.
“Koma Yehova Mulungu wa Israeli anamupereka Sihoni pamodzi ndi anthu ake onse mʼmanja mwa Israeli, ndipo anawagonjetsa. Choncho Aisraeli analanda dziko lonse la Aamori amene amakhala mʼdzikolo.
22 They took over everything within the territory of the Amorites, from the Arnon to the Jabbok, and from the wilderness to the Jordan.
Analanda dziko lonse kuchokera ku Arinoni mpaka ku Yaboki ndiponso kuchokera ku chipululu mpaka ku mtsinje wa Yorodani.
23 So then Yahweh, the God of Israel, has driven out the Amorites before his people Israel, and should you now take possession of their land?
“Ndiye kuti Yehova Mulungu wa Aisraeli ndiye analanda dziko la Aamori, kuwalandirira anthu ake. Kodi inu mukufuna kutilanda dzikolo?
24 Will you not take over the land that Chemosh, your god, gives you? So whatever land Yahweh our God has given us, we will take over.
Bwanji inu osakhazikika mʼdziko limene Kemosi mulungu wanu anakupatsani, ifenso tikhazikike mʼdziko limene Yehova Mulungu wathu anatipatsa?
25 Now are you really better than Balak son of Zippor, king of Moab? Did he dare to have an argument with Israel? Did he ever wage war against them?
Kodi ndinu abwino kuposa Balaki mwana wa Zipori, mfumu ya Mowabu? Kodi iye anakanganapo kapena kuchita nkhondo ndi Israeli?
26 While Israel lived for three hundred years in Heshbon and its villages, and in Aroer and its villages, and in all the cities that are along the banks of the Arnon—why then did you not take them back during that time?
Pamene Aisraeli ankakhala mʼdziko la Hesiboni ndi mʼmidzi yake, mʼdziko la Aroeri ndi midzi yake, komanso mʼmizinda yonse imene ili mʼmbali mwa mtsinje wa Arinoni kwa zaka 300, nʼchifukwa chiyani inu simunalande malowo nthawi imeneyo?
27 I have not done you wrong, but you are doing me wrong by attacking me. Yahweh, the judge, will decide today between the people of Israel and the people of Ammon.”
Choncho ine sindinakuchimwireni. Koma inu mukundilakwira pomenyana nane. Yehova woweruza, ndiye aweruze lero mlandu wa pakati pa Aisraeli ndi Aamoni.”
28 But the king of the people of Ammon rejected the warning Jephthah sent him.
Koma mfumu ya Aamori, sinasamale mawu amene Yefita anatumiza kwa iyo.
29 Then the Spirit of Yahweh came on Jephthah, and he passed through Gilead and Manasseh, and passed through Mizpah of Gilead, and from Mizpah of Gilead he passed through to the people of Ammon.
Tsono Mzimu wa Yehova unatsikira pa Yefita. Ndipo iye ananyamuka nadzera ku Giliyadi ndi ku Manase. Anafika ku Mizipa mʼdziko la Giliyadi, ndipo kuchokera kumeneko anapita kukalimbana ndi Aamoni.
30 Jephthah made a vow to Yahweh and said, “If you give me victory over the people of Ammon,
Yefita analumbira kwa Yehova kuti, “Ngati mupereka Aamoni mʼmanja mwanga,
31 then whatever comes out of the doors of my house to meet me when I return in peace from the people of Ammon will belong to Yahweh, and I will offer it up as a burnt offering.”
aliyense amene atuluke pa khomo la nyumba yanga kudzandichingamira pobwerera nditagonjetsa Aamoni adzakhala wake wa Yehova, ndipo ndidzamupereka kuti akhale nsembe yopsereza.”
32 So Jephthah passed through to the people of Ammon to fight against them, and Yahweh gave him victory.
Kenaka Yefita anawolokera kwa Aamoni kukamenya nawo nkhondo, ndipo Yehova anawaperekadi mʼmanja mwake.
33 He attacked them and caused a great slaughter from Aroer as far as Minnith—twenty cities—and to Abel Keramim. So the people of Ammon were put under the control of the people of Israel.
Iye anawononga mizinda makumi awiri kuchokera ku Ariori mpaka pafupi ndi mzinda wa Miniti. Anapitirira mpaka ku Abeli-Keranimu. Choncho Aisraeli anagonjetsa Aamoni.
34 Jephthah came to his home at Mizpah, and there his daughter came out to meet him with tambourines and with dancing. She was his only child, and besides her he had neither son nor daughter.
Pambuyo pake Yefita anabwerera ku nyumba yake. Tsono anangoona mwana wake wamkazi akutuluka kudzamuchingamira akuyimba ngʼoma ndi kuvina. Uyu anali mwana yekhayo wa Yefita. Analibenso mwana wina wamwamuna kapena wamkazi.
35 As soon as he saw her, he tore his clothes and said, “Oh! My daughter! You have crushed me with sorrow, and you have become one who causes me pain! For I have made an oath to Yahweh, and I cannot turn back on my promise.”
Yefita ataona mwana wake uja, anangʼamba zovala zake ndi kulira, “Kalanga ine! Mwana wanga! Wandivulaza kwambiri ndipo iwe ndi gwero la mavuto anga. Ine ndinalumbira kwa Yehova ndi pakamwa pangapa ndipo sindingathe kubweza malumbiro angawo.”
36 She said to him, “My father, you have made a vow to Yahweh, do to me everything you promised, because Yahweh has taken vengeance for you against your enemies, the Ammonites.”
Mwanayo anayankha kuti, “Abambo, ngati munalonjeza kwa Yehova ndi pakamwa panu, chitani zimene munalonjezera pakuti Yehova wakuthandizani kulipsira adani anu Amowabu.”
37 She said to her father, “Let this promise be kept for me. Leave me alone for two months, that I may leave and go down to the hills and grieve over my virginity, I and my companions.”
Anatinso kwa abambo ake, “Ndikupempheni chinthu ichi: Mundilole ndikayendeyende ku mapiri miyezi iwiri ndizikalira pamodzi ndi anzanga chifukwa ndikufa ndikanali namwali wosadziwa mwamuna.”
38 He said, “Go.” He sent her away for two months. She left him, she and her companions, and they grieved her virginity in the hills.
Yefita anamuyankha kuti, “Pita.” Ndipo anamulola kuti apite miyezi iwiri. Tsono anapita kumapiri ndi atsikana anzake kukalira chifukwa cha unamwali wake.
39 At the end of two months she returned to her father, who did with her according to the promise of the vow he had made. Now she had never slept with a man, and it became a custom in Israel
Miyezi iwiri itatha iye anabwerera kwa abambo ake, ndipo anachitadi zimene analonjeza. Motero unakhala mwambo wa Aisraeli,
40 that the daughters of Israel every year, for four days, would retell the story of the daughter of Jephthah the Gileadite.
kuti atsikana a Israeli ankapita chaka chilichonse kukalira maliro a mwana wa mkazi wa Yefita, Mgiliyadi uja masiku makumi anayi pa chaka.

< Judges 11 >