< Job 36 >
1 Elihu continued on and said,
Ndipo Elihu anapitirira kuyankhula nati:
2 “Permit me to speak a little longer, and I will show you some things because I have a little more to say in defense of God.
“Mundilole pangʼono pokha ndipo ndikuonetsani kuti zilipo zambiri zoti ziyankhulidwe mʼmalo mwa Mulungu.
3 I will obtain my knowledge from far off; I will acknowledge that righteousness belongs to my Maker.
Nzeru zanga ndimazitenga kutali; ndidzaonetsa kulungama kwa Mlengi wanga.
4 For indeed, my words will not be false; someone who is mature in knowledge is with you.
Ndithudi mawu anga si abodza; wanzeru zangwiro ali ndi inu.
5 See, God is mighty, and despises no one; he is mighty in strength of understanding.
“Mulungu ndi wamphamvu, koma sanyoza anthu; Iye ndi wamphamvu, ndipo ndi wokhazikika pa cholinga chake.
6 He does not preserve the life of wicked people but instead does what is right for those who suffer.
Salola oyipa kuti akhalebe ndi moyo koma amapereka ufulu kwa anthu osautsidwa.
7 He does not withdraw his eyes from righteous people but instead sets them on thrones like kings forever, and they are lifted up.
Iye saleka kuyangʼanira anthu olungama; amawayika kuti alamulire pamodzi ndi mafumu ndipo amawalemekeza mpaka muyaya.
8 If they are bound in chains and trapped in cords of suffering,
Koma ngati anthu amangidwa ndi unyolo, ndipo akondwa ndi zingwe zamasautso,
9 then he reveals to them what they have done, and their transgressions and their pride.
Iye amawafotokozera zomwe anachita, kuti iwo anachimwa modzikuza.
10 He also opens their ears to his instruction, and commands them to turn back from iniquity.
Mulungu amawatsekula makutu kuti amve malangizo ake ndipo amawalamula kuti alape zoyipa zawo.
11 If they listen to him and worship him, they will spend their days in prosperity, their years in contentment.
Ngati iwo amumvera ndi kumutumikira, adzatsiriza masiku a moyo wawo mwamtendere, adzatsiriza zaka zawo mosangalala.
12 However, if they do not listen, they will perish by the sword; they will die because they have no knowledge.
Koma ngati samvera, adzaphedwa ndi lupanga ndipo adzafa osadziwa kanthu.
13 Those who are godless in heart store up their anger; they do not cry out for help even when God ties them up.
“Anthu osapembedza amasunga mkwiyo mu mtima mwawo; akawalanga, safuwulira kwa Iye kupempha thandizo.
14 They die in their youth; their lives end among the cultic prostitutes.
Amafa akanali achinyamata, pakati pa amuna achiwerewere a kumalo azipembedzo.
15 God rescues afflicted people by means of their afflictions; he opens their ears by means of their oppression.
Koma ovutika, Iye amawapulumutsa pa mavuto awo; Mulungu amawayankhula mʼmasautso awowo.
16 Indeed, he would like to draw you out of distress into a broad place where there is no hardship and where your table would be set with food full of fatness.
“Iye akukukopani inu kuti muchoke mʼmasautso, kuti mupite ku malo aakulu kumene kulibe chokutchingani, kumalo a mpumulo kumene kuli chakudya chabwino kwambiri.
17 But you are full of judgment on wicked people; judgment and justice have laid hold of you.
Koma tsopano inu mwapezeka wopalamula chifukwa cha kuyipa kwanu; chiweruzo ndi chilungamo chakugwerani.
18 Do not let your anger entice you to mockery, or the greatness of a ransom to turn you aside.
Muchenjere kuti wina asakukopeni ndi chuma; musalole kuti chiphuphu chachikulu chikusocheretseni.
19 Can your wealth benefit you, so that you will not be in distress, or can all the force of your strength help you?
Kodi chuma chanu kapena mphamvu zanu zonse zingakusungeni kotero kuti simungakhale pa masautso?
20 Do not desire the night, to commit sin against others, when peoples are cut off in their place.
Musalakalake kuti usiku ubwere, pakuti ndiyo nthawi imene anthu adzawonongeka.
21 Be careful that you do not turn to sin because you are being tested by suffering so that you will stay away from sinning.
Muchenjere kuti musatembenukire ku uchimo, chifukwa uchimowo ndiwo unabweretsa kuzunzika kwanu.
22 See, God is exalted in his power; who is a teacher like him?
“Taonani, Mulungu ndi wamkulu ndiponso ndi wamphamvu. Kodi ndi mphunzitsi uti amene angafanane naye?
23 Who has ever instructed him about his way? Who can ever say to him, 'You have committed unrighteousness?'
Kodi ndani amene anamuwuzapo Mulungu zoti achite, kapena kumuwuza kuti, ‘Inu mwachita chinthu cholakwa?’
24 Remember to praise his deeds, of which people have sung.
Kumbukirani kutamanda ntchito zake zimene anthu amaziyamika mʼnyimbo.
25 All people have looked on those deeds, but they see those deeds only from far away.
Anthu onse amaziona ntchitozo; anthuwo amaziona ali kutali.
26 See, God is great, but we do not understand him well; the number of his years is incalculable.
Ndithudi, Mulungu ndi wamkulu, sitimudziwa nʼpangʼono pomwe! Chiwerengero cha zaka zake nʼchosadziwika.
27 For he draws up the drops of water that he distills as rain from his vapor,
“Mulungu ndiye amakweza timadontho tamadzi kuthambo, timene timasungunuka nʼkukhala mvula;
28 which the clouds pour down and drop in abundance on mankind.
mitambo imagwetsa mvulayo ndipo mvulayo imavumbwa pa anthu mokwanira.
29 Indeed, can anyone understand the extensive spread of the clouds and the thunder from his hut?
Kodi ndani amene angadziwe momwe mitambo imayendera, momwe Iye amabangulira kuchokera kumalo ake?
30 See, he spreads his lightning around him and covers the roots of the sea.
Taonani momwe amawalitsira zingʼaningʼani pa malo ake onse, zimafika ngakhale pansi pa nyanja.
31 In this way he judges the peoples and gives food in abundance.
Umu ndi mmene Iye amalamulira mitundu ya anthu ndi kuwapatsa chakudya chochuluka.
32 He fills his hands with the lightning until he commands it to strike its mark.
Amadzaza manja ake ndi zingʼaningʼani, ndipo amazilamulira kuti zigwe pamalo pamene Iye akufuna.
33 Its thunder warns of the storm, the cattle can also hear it is coming.
Mabingu ake amalengeza za kubwera kwa mvula yamkuntho; ngʼombe nazo zimalengeza za kubwera kwake.