< Job 26 >

1 Then Job answered and said,
Pamenepo Yobu anayankha kuti,
2 “How you have helped one who has no power! How you have saved the arm that has no strength!
“Wamuthandizadi munthu wopanda mphamvu! Walimbitsadi dzanja la munthu wofowoka!
3 How you have advised one who has no wisdom and announced to him sound knowledge!
Wapereka malangizo kwa munthu amene alibe nzeru! Ndipotu waonetsadi nzeru zochuluka!
4 With whose help have you spoken these words? Whose spirit was it that came out from you?
Kodi wakuthandiza ndani kuti uyankhule mawu awa? Ndipo ndi mzimu wa yani umene unayankhula pakamwa pako?
5 The dead are made to tremble, those who are beneath the waters and all who dwell in them.
“Mizimu ya anthu akufa ikunjenjemera pansi pa madzi, ndi zonse zokhala mʼmadzimo.
6 Sheol is naked before God; destruction itself has no covering against him. (Sheol h7585)
Dziko la anthu akufa ndi lapululu pamaso pa Mulungu; chiwonongeko ndi chosaphimbidwa. (Sheol h7585)
7 He stretches out the northern skies over the empty space, and he hangs the earth over nothing.
Mulungu anayala thambo la kumpoto pa phompho; Iye anakoloweka dziko lapansi mʼmalo mwake pamene panali popanda nʼkanthu komwe.
8 He binds up the waters in his thick clouds, but the clouds are not torn under them.
Amasunga madzi ambiri mʼmitambo yake, koma mitamboyo siphulika chifukwa cha kulemera kwa madziwo.
9 He covers the surface of the moon and spreads his clouds on it.
Iye amaphimba mwezi wowala, amawuphimba ndi mitambo yake.
10 He has engraved a circular boundary on the surface of the waters as the line between light and darkness.
Mulungu anawalembera madzi malire wonga uta, kukhala malire pakati pa kuwunika ndi mdima.
11 The pillars of heaven tremble and are astonished at his rebuke.
Mizati yochirikiza mitambo yakumwamba imanjenjemera, ndi kudabwa pa kudzudzula kwake.
12 He calmed the sea with his power; by his understanding he shattered Rahab.
Ndi mphamvu zake anatontholetsa nyanja; ndi nzeru zake anakantha chirombo cha mʼmadzi chija chotchedwa Rahabe.
13 By his breath he made the skies clear; his hand pierced the fleeing serpent.
Ndi mpweya wake anayeretsa zamumlengalenga, dzanja lake linapha chinjoka chothawa chija.
14 See, these are but the fringes of his ways; how small a whisper do we hear of him! Who can understand the thunder of his power?”
Zimenezi ndi pangʼono chabe mwa ntchito yake; tingomva pangʼono za Iye ngati kunongʼona! Kodi ndani angathe kudziwa kukula kwa mphamvu zake?”

< Job 26 >