< Job 10 >

1 I am weary of my life; I will give free expression to my complaint; I will speak in the bitterness of my soul.
“Ine ndatopa nawo moyo wanga; choncho ndidzanena zodandaula zanga momasuka ndipo ndidzayankhula mwa kuwawidwa mtima kwanga.
2 I will say to God, 'Do not merely condemn me; show me why you accuse me.
Ndidzati kwa Mulungu wanga: Musandiweruze kuti ndine wolakwa, koma mundiwuze chifukwa chimene Inu mukukanganira ndi ine.
3 Is it good to you that you should oppress me, to despise the work of your hands while you smile on the plans of the wicked?
Kodi mumakondwera mukamandizunza, kunyoza ntchito ya manja anu, chonsecho mukusekerera ndi zochita za anthu oyipa?
4 Do you have eyes of flesh? Do you see like a man sees?
Kodi maso anu ali ngati a munthu? Kodi mumaona zinthu monga momwe amazionera munthu?
5 Are your days like the days of mankind or your years like the years of people,
Kodi masiku anu ali ngati masiku a munthu, kapena zaka zanu ngati zaka za munthu,
6 that you inquire after my iniquity and search after my sin,
kuti Inu mufufuze zolakwa zanga ndi kulondola tchimo langa,
7 although you know I am not guilty and there is no one who can rescue me from your hand?
ngakhale mukudziwa kuti sindine wolakwa ndiponso kuti palibe amene angandilanditse mʼdzanja lanu?
8 Your hands have framed and fashioned me together round about, yet you are destroying me.
“Munandiwumba ndi kundipanga ndi manja anu. Kodi tsopano Inu mudzatembenuka ndi kundiwononga?
9 Call to mind, I beg you, that you have fashioned me like clay; will you bring me into dust again?
Kumbukirani kuti munandipanga ndi dothi, kodi tsopano mundibwezeranso ku fumbi?
10 Have you not poured me out like milk and curdled me like cheese?
Suja munapatsa abambo anga mphamvu zoti andibale, suja munandikuza bwino mʼmimba mwa amayi anga?
11 You have clothed me with skin and flesh and knit me together with bones and sinews.
Munandikuta ndi khungu ndi mnofu ndi kundilumikiza pamodzi ndi mafupa ndi mitsempha?
12 You have granted me life and covenant faithfulness; your help has guarded my spirit.
Munandipatsa moyo ndi kundionetsa chifundo chanu, ndipo munasamalira bwino moyo wanga.
13 Yet these things you hid in your heart— I know that this is what you were thinking:
“Koma izi ndi zimene munabisa mu mtima mwanu, ndipo ndikudziwa kuti zinali mʼmaganizo anu:
14 that if I sinned, you would notice it; you would not acquit me of my iniquity.
Kuti ngati ndingachimwe mudzakhala mukundipenyetsetsa ndipo kuti simudzalola kuti ndisalangidwe chifukwa cha kulakwa kwanga.
15 If I have acted wickedly, woe to me; and even if I acted righteously, I could not lift up my head, since I am filled with disgrace— see my affliction!
Ngati ndili wolakwa, tsoka langa! Koma ngakhale ndili wosalakwa sindingathe kutukula mutu wanga, pakuti ndagwidwa ndi manyazi ndipo ndamizidwa mʼmavuto anga.
16 If my head were lifted up, you would stalk me like a lion; and again you would show yourself with marvellous acts of power against me.
Ndipo ndikatukula mutu wanga, Inu mumandisaka ngati mkango ndiponso mumandiopseza ndi mphamvu yanu.
17 You bring new witnesses against me and increase your anger against me; you attack me with fresh armies.
Mumabweretsa mboni zatsopano potsutsana nane ndipo mkwiyo wanu pa ine umanka nukulirakulira ndi magulu anu olimbana nane amanka nachulukirachulukira.
18 Why, then, have you brought me out of the womb? I wish I had given up my spirit and that no eye had ever seen me.
“Chifukwa chiyani Inu munalola kuti ndibadwe? Ndi bwino ndikanafa diso lililonse lisanandione.
19 I would have been as though I had never existed; I would have been carried from the womb to the grave.
Ndikanapanda kubadwa, kapena akanangonditenga nditabadwa kupita nane ku manda!
20 Are not my days only a few? Stop then, let me alone, so that I may have a little rest
Kodi masiku anga owerengeka sali pafupi kutha? Ndilekeni kuti ndipumule pangʼono pokha
21 before I go from where I will not return, to the land of darkness and of the shadow of death,
ndisanapite ku malo amene munthu sabwererako ku dziko la imfa ndi kwa mdima wandiweyani,
22 the land that is as dark as midnight, the land of the shadow of death, without any order, where the light is like midnight.'”
ku dziko la mdima wandiweyani ndi chisokonezo, kumene kuwala kumakhala ngati mdima.”

< Job 10 >