< Jeremiah 22 >

1 This is what Yahweh says, “Go down to the house of the king of Judah and proclaim this word there.
Yehova anandiwuza kuti, “Pita ku nyumba ya mfumu ya ku Yuda ndipo ukayiwuze kuti,
2 Say, 'King of Judah, listen to the word of Yahweh—you who sit on David's throne—you, and your servants, and your people who come through these gates.
‘Imva mawu a Yehova, iwe mfumu ya ku Yuda, amene umakhala pa mpando waufumu wa Davide; iwe, nduna zako pamodzi ndi anthu ako amene amalowera pa zipata izi.
3 Yahweh says this, “Perform justice and righteousness, and anyone who has been robbed—rescue him from the hand of the oppressor. Do not mistreat any foreigner in your land, or any orphan or widow. Do not commit violence or pour out innocent blood in this place.
Yehova akuti, uziweruza molungama ndi mosakondera. Uzipulumutsa munthu amene walandidwa katundu mʼdzanja la womuzunza. Usazunze kapena kupondereza mlendo, ana amasiye kapena akazi amasiye. Usaphe munthu wosalakwa pa malo pano.
4 For if you truly do these things, then kings sitting on David's throne will enter the gates of this house riding in a chariot and on horses, he, his servants, and his people!
Pakuti ngati udzamvera malamulo awa, ndiye kuti mafumu onse okhala pa mpando waufumu wa Davide azidzalowabe pa zipata za nyumba yaufumu ino, atakwera magaleta ndi akavalo, iwowo pamodzi ndi nduna zawo ndi anthu awo.
5 But if you do not listen to these words from me that I have announced—this is Yahweh's declaration—then this royal house will become a ruin.”'
Koma ngati sumvera malamulo awa, akutero Yehova, ndikulumbira pali Ine ndemwe kuti nyumba ino yaufumu idzasanduka bwinja.’”
6 For Yahweh says this concerning the house of the king of Judah, 'You are like Gilead, or like the summit of Lebanon to me. Yet I will turn you into a wilderness, into cities with no inhabitants.
Pakuti zimene Yehova akunena za nyumba yaufumu ya mfumu ya ku Yuda ndi izi: “Ngakhale iwe uli ngati Giliyadi kwa Ine, ngati msonga ya phiri la Lebanoni, komabe ndidzakusandutsa chipululu, ngati mizinda yopanda anthu.
7 For I have designated destroyers to come against you! Men with their weapons will cut off the best of your cedars and let them fall into the fire.
Ndidzatuma anthu oti adzakuwononge, munthu aliyense ali ndi zida zake, ndipo adzadula mikungudza yako yokongola nadzayiponya pa moto.
8 Then many nations will pass by this city. Each person will say to the next, “Why has Yahweh acted in this way toward this great city?”
“Pamene anthu a mitundu ina adzadutsa pa mzinda umenewu adzafunsana kuti, ‘Chifukwa chiyani Yehova wachita chinthu chotere pa mzinda waukuluwu?’
9 Then the other will answer, “Because they abandoned the covenant of Yahweh their God and bowed down to other gods and worshiped them.”
Ndipo yankho lake lidzakhala lakuti, ‘Chifukwa anasiya pangano limene anapangana ndi Yehova Mulungu wawo ndipo anapembedza ndi kutumikira milungu ina.’”
10 Do not weep for the one who is dead or mourn for him; but weep bitterly for him who is about to go away, because he will never return and see his native land again.'
Musayilire mfumu Yosiya, musamuyimbire nyimbo womwalirayo; mʼmalo mwake, mulire kwambiri chifukwa cha Yehowahazi amene wapita ku ukapolo, chifukwa sadzabwereranso kapena kuonanso dziko lake lobadwira.
11 For Yahweh says this about Jehoahaz son of Josiah king of Judah, who served as king instead of Josiah his father, 'He has gone from this place and will not come back.
Pakuti zimene Yehova akunena za Yehowahazi mwana wa Yosiya, amene anatenga mpando waufumu wa Yuda mʼmalo mwa abambo ake koma nʼkuwusiya ndi izi: “Iye sadzabwereranso.
12 He will die there in the place to where they have exiled him, and he will never again see this land.'
Iyeyo adzafera ku ukapoloko. Sadzalionanso dziko lino.”
13 Woe to him who builds his house by unrighteousness, his upper rooms by injustice, who makes his neighbor work for him for nothing, and he does not give him his wages;
“Tsoka kwa munthu womanga nyumba yake mopanda chilungamo, womanga zipinda zake zosanja monyenga, pogwiritsa ntchito abale ake mwathangata, osawapatsa malipiro a ntchito yawo.
14 he says, 'I will build for myself a large house with spacious upper rooms.' So he cuts out large windows for it, and he panels it with cedar, and he paints it red.
Munthuyo amati, ‘Ndidzadzimangira nyumba yayikulu ya zipinda zikuluzikulu zamʼmwamba.’ Kotero ndidzapanga mazenera akuluakulu, ndi kukhomamo matabwa a mkungudza ndi kukongoletsa ndi makaka ofiira.
15 Is this what makes you a good king, that you wanted to have boards of cedar? Did not your father also eat and drink, yet do justice and righteousness? Then things went well for him.
“Kodi kukhala ndi nyumba ya mkungudza wambiri zingachititse iwe kukhala mfumu? Ganiza za abambo ako. Suja anali ndi zonse zakudya ndi zakumwa. Abambo ako ankaweruza molungama ndi mosakondera, ndipo zonse zinkawayendera bwino.
16 He judged in favor of the poor and needy. It was good then. Is this not what it means to know me?—this is Yahweh's declaration.
Iye ankateteza anthu osauka ndi osowa, ndipo zonse zinkamuyendera bwino. Kodi zimenezi sindiye tanthauzo la kudziwa Ine?” akutero Yehova.
17 But there is nothing in your eyes and heart except worry for your unjust profit and for pouring out innocent blood, for producing oppression and crushing of others.
“Koma maso ako ndi mtima sizili penanso, koma zili pa phindu lachinyengo, pa zopha anthu osalakwa ndi pa kuzunza ndi pakulamulira mwankhanza.”
18 Therefore this is what Yahweh says about Jehoiakim son of Josiah, king of Judah: They will not lament for him, saying, 'Woe, my brother!' or 'Woe, my sister!' They will not lament for him, saying, 'Woe, master!' or 'Woe, majesty!'
Nʼchifukwa chake Yehova ponena za Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya ku Yuda akuti, “Anthu sadzamulira maliro kapena kunena kuti, ‘Kalanga ine, mʼbale wanga! Kalanga ine mlongo wanga! Anthu ake sadzamulira maliro kuti, Kalanga ine, mbuye wathu! Taonani ulemerero wake wapita!’
19 He will be buried with a donkey's burial, dragged away and thrown out beyond the gates of Jerusalem.
Adzayikidwa ngati bulu, kuchita kumuguguza ndi kukamutaya kunja kwa zipata za Yerusalemu.”
20 Go up Lebanon's mountains and shout. Lift your voice in Bashan. Shout from the Abarim mountains, for all of your friends will be destroyed.
“Tsono inu anthu a ku Yerusalemu, pitani ku mapiri a Lebanoni kuti mukalire mofuwula kumeneko, mawu anu akamveke mpaka ku Basani. Mulire mofuwula muli ku Abarimu chifukwa abwenzi ako onse awonongeka.
21 I spoke to you when you were safe, but you said, 'I will not listen.' This was your custom since your youth, for you have not listened to my voice.
Ndinakuchenjezani pamene munali pa mtendere. Koma inu munati, ‘Sindidzamvera.’ Umu ndi mmene mwakhala mukuchitira kuyambira mukali aangʼono. Simunandimvere Ine.
22 The wind will shepherd away all your shepherds, and your friends will go into captivity. Then you will certainly be ashamed and humiliated by all of your evil deeds.
Mphepo idzakuchotserani abusa anu onse, ndipo abwenzi anu adzatengedwa ku ukapolo. Pamenepo mudzachita manyazi ndi kunyozedwa chifukwa cha zoyipa zanu zonse.
23 You who live in 'Lebanon,' who is nestled in cedar buildings, how you will be pitied when the labor pains come upon you, pain like that of a woman in labor!”
Inu amene mumakhala mʼnyumba ya ku Lebanoni, amene munamanga nyumba zanu pakati pa mikungudza, mudzabuwula kwambiri pamene zowawa zidzakugwerani, zonga za mkazi pa nthawi yake yochira!
24 “As I live—this is Yahweh's declaration—even if you, Jehoiachin son of Jehoiakim, king of Judah, were the signet on my right hand, I would tear you off.
“Pali Ine wamoyo, akutero Yehova, ngakhale iwe, Yehoyakini mwana wa Yehoyakimu mfumu ya ku Yuda, ukanakhala ngati mphete ya ku dzanja langa lamanja, ndikanakuvula nʼkukutaya.
25 For I have given you to the hand of the ones seeking your life and to the hand of those before whom you are afraid, even to the hand of Nebuchadnezzar king of Babylon and the Chaldeans.
Ndidzakupereka kwa amene akufuna kukupha, amene iwe umawaopa. Ndidzakupereka kwa Nebukadinezara, mfumu ya ku Babuloni ndi anthu ake.
26 I will throw you and your mother who bore you into another land, a country where you were not born, and there you will die.
Iwe pamodzi ndi amayi ako amene anakubereka ndidzakupititsani ku dziko lachilendo. Ngakhale inu simunabadwire kumeneko, komabe mudzafera komweko.
27 About this land to which they will want to return, they will not come back here.
Simudzabwereranso ku dziko limene mudzafuna kubwerera.”
28 Is this a despised and shattered vessel? Is this man Jehoiachin a pot that pleases no one? Why have they thrown him and his descendants out, and have poured them out into a land that they did not know?
Kodi Yehoyakini wakhala ngati mbiya yonyozeka, yosweka imene anthu sakuyifunanso? Kodi nʼchifukwa chake iye pamodzi ndi ana ake, achotsedwa nʼkutayidwa ku dziko limene iwo sakulidziwa?
29 Land, Land, Land! Hear the word of Yahweh!
Iwe dziko, dziko, dziko, Imva mawu a Yehova!
30 Yahweh says this, 'Write about this man Jehoiachin: He will be childless. He will not prosper during his days, and no one among his descendants will achieve success or ever again sit on David's throne and rule over Judah.'”
Yehova akuti, “Munthu ameneyu mumutenge ngati wopanda ana, munthu amene sadzakhala wochita bwino pamoyo wake wonse, pakuti palibe ndi mmodzi yemwe mwa zidzukulu zake zomwe zidzachita bwino. Palibe amene adzathe kukhala pa mpando waufumu wa Davide ndi kulamulira Yuda.”

< Jeremiah 22 >