< Jeremiah 2 >
1 The word of Yahweh came to me, saying,
Yehova anandiwuza kuti,
2 “Go and proclaim in the hearing of Jerusalem. Say, 'Yahweh says this: I have called to mind on your behalf the covenant faithfulness in your youthfulness, your love at the time when we were engaged, when you went after me in the wilderness, the land that was not sown.
“Pita ukalengeze kwa anthu a ku Yerusalemu kuti Yehova akuti, “‘Ine ndikukumbukira mmene umakhulupirikira pa unyamata wako, mmene unkandikondera ngati momwe amachitira mkwatibwi, mmene unkanditsata mʼchipululu muja; mʼdziko losadzalamo kanthu.
3 Israel was set apart to Yahweh, the firstfruits of his harvest! All who ate from the firstfruits were held guilty; disaster came upon them—this is Yahweh's declaration.'”
Israeli anali wopatulika wa Yehova, anali ngati zipatso zake zoyamba kucha pa nthawi yokolola; onse amene anamuzunza anapezeka kuti ndi olakwa ndipo mavuto anawagwera,’” akutero Yehova.
4 Hear the word of Yahweh, house of Jacob, all you clans of the house of Israel.
Imvani mawu a Yehova, inu zidzukulu za Yakobo, inu mafuko onse a Israeli.
5 Yahweh says this, “What did your fathers find wrong with me, that they went far from following me? That they went after useless idols and became useless themselves?
Yehova akuti, “Kodi makolo anu anandipeza nʼcholakwa chanji, kuti andithawe? Iwo anatsata milungu yachabechabe, nawonso nʼkusanduka achabechabe.
6 They did not say, 'Where is Yahweh, who brought us up from the land of Egypt? Where is Yahweh, who led us to the wilderness, into the land of the Arabah and pits, in a land of drought and deep darkness, a land through which no one passes and where no one lives?'
Iwo sanafunse nʼkomwe kuti, ‘Kodi Yehova ali kuti, amene anatitulutsa mʼdziko la Igupto natitsogolera mʼchipululu mʼdziko lowuma ndi lokumbikakumbika, mʼdziko lopanda mvula ndi la mdima, dziko limene munthu sadutsamo ndipo simukhala munthu aliyense?’
7 But I brought you to the land of Carmel, to eat its fruit and other good things! Yet when you came, you defiled my land, you made my inheritance an abomination!
Ndinakufikitsani ku dziko lachonde kuti mudye zipatso zake ndi zabwino zake zina. Koma inu mutafika munaliyipitsa dziko langa ndi kusandutsa cholowa changa kukhala chonyansa.
8 The priest did not say, 'Where is Yahweh?' and the experts in the law did not care about me! The shepherds transgressed against me. The prophets prophesied for Baal and walked after unprofitable things.
Ansembe nawonso sanafunse kuti, ‘Yehova ali kuti?’ Iwo amene amaphunzitsa malamulo sanandidziwe; atsogoleri anandiwukira. Aneneri ankanenera mʼdzina la Baala, ndi kutsatira mafano achabechabe.
9 So I will still accuse you—this is Yahweh's declaration—and I will accuse your sons' sons.
“Chifukwa chake Ine ndidzakuyimbaninso mlandu,” akutero Yehova. “Ndipo ndidzayimbanso mlandu zidzukulu zanu.
10 For cross over to the coasts of Kittim and look. Send messengers out to Kedar and find out and see if there has ever before been anything like this.
Pitani kumadzulo ku chilumba cha Kitimu, ndipo mukaone, tumizani anthu ku Kedara kuti akafufuze bwino; ndipo muona kuti zinthu zoterezi sizinachitikepo nʼkale lomwe:
11 Has a nation exchanged gods, even though they were not gods? But my people have exchanged their glory for what cannot help them.
Kodi ulipo mtundu wa anthu uliwonse umene unasinthapo milungu yake? (Ngakhale kuti si milungu nʼkomwe). Koma anthu anga asinthitsa Mulungu wawo waulemerero ndi mafano achabechabe.
12 Shudder, heavens, because of this! Be shocked and horrified—this is Yahweh's declaration.
Inu mayiko akumwamba, dabwani ndi zimenezi, ndipo njenjemerani ndi mantha aakulu,” akutero Yehova.
13 For my people have committed two evils against me: They have abandoned the springs of living waters, and they have dug out cisterns for themselves, broken cisterns that cannot hold water.
“Popeza anthu anga achita machimo awiri: Andisiya Ine kasupe wa madzi a moyo, ndi kukadzikumbira zitsime zawo, zitsime zongʼaluka, zomwe sizingathe kusunga madzi.
14 Is Israel a slave? Was he born in his master's home? So why has he become plunder?
Israeli si wantchito kapena kapolo wobadwira mʼnyumba, ayi. Nanga nʼchifukwa chiyani amuwononga chotere?
15 Young lions roared against him. They made a lot of noise and made his land a horror. His cities are destroyed without any inhabitants.
Adani ake abangulira ndi kumuopseza ngati mikango. Dziko lake analisandutsa bwinja; mizinda yake anayitentha popanda wokhalamo.
16 Also, the people of Memphis and Tahpanhes will shave your skull.
Ndiponso Aigupto a ku Mefisi ndi a ku Tapanesi akuphwanyani mitu.
17 Did you not do this to yourselves when you abandoned Yahweh your God, while he was leading you along the way?
Zimenezitu zakuchitikirani chifukwa munasiya Yehova Mulungu wanu pamene Iye ankakutsogolerani pa njira yanu?
18 So now, why take the road to Egypt and drink the waters of Shihor? Why take the road to Assyria and drink the waters of the Euphrates River?
Tsopano mudzapindula chiyani mukapita ku Igupto, kukamwa madzi a mu Sihori? Ndipo mudzapindulanji mukapita ku Asiriya, kukamwa madzi a mu mtsinje wa Yufurate?
19 Your wickedness rebukes you, and your faithlessness punishes you. So think about it and understand that it is wicked and bitter when you forsake Yahweh your God, and have no fear of me—this is the declaration of Lord Yahweh of hosts.
Kuyipa kwanuko kudzakulangani; kubwerera mʼmbuyo kwanuko kudzakutsutsani. Tsono ganizirani bwino, popeza ndi chinthu choyipa kundisiya Ine Yehova Mulungu wanu; ndi chinthu chowawa ndithu kusandiopa Ine Mulungu wanu. Akutero Ambuye Yehova Wamphamvuzonse.
20 For I broke your yoke that you had in ancient days; I tore your fetters off you. Still you said, 'I will not serve!' since you bowed down on every high hill and beneath every leafy tree, you adulterer.
“Kuyambira kalekale inu munathyola goli lanu ndi kudula msinga zanu; munanena kuti, ‘Sitidzakutumikirani!’ Ndithudi, inu mwakhala ngati mkazi wachiwerewere. Mukupembedza milungu ina pa phiri lililonse lalitali ndiponso pansi pa mtengo uliwonse wa masamba ambiri.
21 I planted you as a choice vine, completely from pure seed. How then have you have changed yourself into a corrupt, worthless vine?
Ine ndinakudzala iwe ngati mtengo wampesa wosankhika; unali mpesa wabwino kwambiri ndi wodalirika. Nanga nʼchifukwa chiyani wasanduka mpesa wachabechabe wonga wa kutchire?
22 For even if you clean yourself in the river or wash with strong soap, your iniquity is a stain before me—this is the declaration of the Lord Yahweh.
Ngakhale utasamba ndi soda kapena kusambira sopo wambiri, kuthimbirira kwa machimo ako kumaonekabe pamaso panga,” akutero Ambuye Yehova.
23 How can you say, 'I am not defiled! I have not walked after the Baals'? Look at what you did in the valleys! Consider what you have done—you are a swift female camel running here and there,
“Iwe ukunena bwanji kuti, ‘Ine sindinadziyipitse; sindinatsatire Abaala’? Takumbukira mmene unkandichimwira mʼchigwa muja; zindikira bwino zomwe wachita. Iwe uli ngati ngamira yayikazi yaliwiro yomangothamanga uku ndi uku,
24 a wild donkey accustomed to the wilderness, in her heat sniffing the wind! Who can restrain her lust? None of the males need wear themselves out pursuing her; at mating time they will find her.
wakhala ngati mbidzi yozolowera mʼchipululu, yonka ninunkhiza pa nthawi yachisika. Ndani angayiretse chilakolako chakecho? Mphongo iliyonse yoyikhumba sidzavutika. Pa nthawi yachisika chakecho mphongoyo idzayipeza.
25 You must restrain your feet from becoming bare and your throat from being thirsty! But you have said, 'It is hopeless! No, I love strangers and go after them!'
Iwe usathamange, nsapato zingakuthere kuphazi ndi kukhosi kwako kuwuma ndi ludzu. Koma unati, ‘Zamkutu! Ine ndimakonda milungu yachilendo, ndipo ndidzayitsatira.’
26 Like the shame of a thief when he is found, so the house of Israel will be ashamed— they, their kings, their princes, and their priests and prophets!
“Monga momwe mbala imachitira manyazi pamene yagwidwa, moteronso nyumba ya Israeli idzachita manyazi; Aisraeliwo, mafumu ndi akuluakulu awo, ansembe ndi aneneri awo.
27 These are the ones who say to the tree, 'You are my father,' and to the stone, 'You gave birth to me.' For their back faces me and not their faces. Nevertheless, they say in the time of troubles, 'Arise and save us!'
Iwo amawuza mtengo kuti, ‘Iwe ndiwe abambo athu,’ ndipo amawuza mwala kuti, ‘Iwe ndiye amene unatibala.’ Iwo andifulatira Ine, ndipo safuna kundiyangʼana; Koma akakhala pa mavuto amati, ‘Bwerani mudzatipulumutse!’
28 Yet where are the gods that you made for yourselves? Let them arise if they wish to save you in your time of troubles, for your idols equal your cities in number, Judah!
Nanga ili kuti milungu yanu imene munadzipangira nokha? Ibweretu ngati ingathe kukupulumutsani pamene muli pamavuto! Inu anthu a ku Yuda, milungu yanu ndi yambiri kuchuluka kwake ngati mizinda yanu.
29 So why do you accuse me of doing wrong? All of you have sinned against me—this is Yahweh's declaration.
“Kodi mukundizengeranji mlandu? Nonse mwandiwukira,” akutero Yehova.
30 I have punished your people in vain. They would not accept discipline. Your sword has devoured your prophets like a destructive lion!
“Ine ndinalanga anthu ako popanda phindu; iwo sanaphunzirepo kanthu. Monga mkango wolusa, lupanga lanu lapha aneneri anu.
31 You who belong to this generation! Pay attention to my word, the word of Yahweh! Have I been a wilderness to Israel? Or a land of deep darkness? Why would my people say, 'Let us wander around, we will not go to you anymore'?
“Inu anthu a mʼbado uno, ganizirani bwino mawu a Yehova: “Kodi Ine ndinakhalapo ngati chipululu kwa Israeli kapena ngati dziko la mdima wandiweyani? Chifukwa chiyani anthu anga akunena kuti, ‘Ife tili ndi ufulu omayendayenda; sitidzabweranso kwa Inu’?
32 Will a virgin forget her jewelry, a bride her veils? Yet my people have forgotten me for days without number!
Kodi namwali amayiwala zokongoletsera zake, kapena kuyiwala zovala zake za ukwati? Komatu anthu anga andiyiwala masiku osawerengeka.
33 How well you make your way to look for love. You have even taught your ways to wicked women.
Mumadziwa bwino njira zopezera zibwenzi! Choncho ngakhale akazi oyipa omwe mumawaphunzitsa njira zanu.
34 The blood that was the life of innocent, poor people has been found on your clothes. These people were not discovered in acts of burglary.
Ngakhale pa zovala zako anthu amapezapo magazi a anthu osauka osalakwa. Anthuwo simunawapeze akuthyola nyumba. Komabe ngakhale zinthu zili chomwechi,
35 Yet you say, 'I am innocent; surely his anger has turned away from me.' But look! I will bring down judgment on you because you say, 'I have not sinned.'
inu mukunena kuti, ‘Ndife osalakwa, sadzatikwiyira.’ Ndidzakuyimbani mlandu chifukwa mukunena kuti, ‘Ife sitinachimwe.’
36 Why do you treat so very lightly this change in your ways? You will also be disappointed by Egypt, just as you were by Assyria.
Chifukwa chiyani mukunkabe nimusinthasintha njira zanu? Aigupto adzakukhumudwitsani monga momwe Asiriya anakuchititsani manyazi.
37 You will also go out from there dejected, with your hands on your head, for Yahweh has rejected the ones whom you trusted, so you will not be helped by them.”
Mudzachokanso kumeneko manja ali kunkhongo. Popeza Ine Yehova ndawakana anthu amene munkawadalira, choncho sadzakuthandizani konse.