< Jeremiah 14 >
1 This is the word of Yahweh that came to Jeremiah regarding the drought,
Awa ndi mawu amene Yehova anamuwuza Yeremiya onena za chilala:
2 “Let Judah mourn; let her gates fall apart. They are wailing for the land; their cries for Jerusalem are going up.
“Yuda akulira, mizinda yake ikuvutika; anthu ake adzigwetsa pansi mwachisoni, kulira kwa Yerusalemu kwakula.
3 Their mighty ones send out their servants for water. When they go to the trenches, they cannot find water. They all return unsuccessful; they cover their heads ashamed and dishonored.
Anthu awo wolemekezeka akutuma antchito awo kuti akatunge madzi. Apita ku zitsime osapezako madzi. Choncho amabwerera ndi mitsuko yopanda madzi. Amanyazi ndi othedwa nzeru adziphimba kumaso.
4 Because of this the ground is cracked, for there is no rain in the land. The plowmen are ashamed and cover their heads.
Popeza pansi pawumiratu chifukwa kulibe madzi, alimi ali ndi manyazi ndipo amphimba nkhope zawo.
5 For even the doe leaves her young in the fields and abandons them, for there is no grass.
Ngakhale mbawala yayikazi ikusiya mwana wake wakhanda ku thengo chifukwa kulibe msipu.
6 The wild donkeys stand on the bare plains and they pant in the wind like jackals. Their eyes fail to work, for there is no vegetation.”
Mbidzi zikuyima pa zitunda zopanda kanthu nʼkumapuma wefuwefu ngati nkhandwe; maso awo achita chidima chifukwa chosowa msipu.”
7 Even though our iniquities testify against us, Yahweh, act for the sake of your name. For our faithless actions increase; we have sinned against you.
Anthu akuti, “Ngakhale machimo athu akutitsutsa, koma Inu Yehova chitanipo kanthu chifukwa cha dzina lanu. Pakuti kusakhulupirika kwathu nʼkwakukulu; ife takuchimwirani.
8 You are the Hope of Israel, the one who saves him in the time of distress, why will you be like a stranger in the land, like a foreign wanderer who stretches out and spends just one night?
Inu Yehova amene Aisraeli amakukhulupirirani ndi amene mumawapulumutsa pa nthawi ya masautso, chifukwa chiyani mukukhala ngati mlendo mʼdziko muno? Chifukwa chiyani muli ngati wapaulendo amene akungogona tsiku limodzi?
9 Why are you like someone who is astounded, or like a warrior who has no power to rescue? You are in our midst, Yahweh, and your name is called over us. Do not leave us!
Chifukwa chiyani muli ngati munthu amene wadzidzimutsidwa, kapena ngati wankhondo amene alibe mphamvu yopulumutsa? Komabe Inu Yehova, muli pakati pathu, ndipo tikudziwika ndi dzina lanu; musatitaye ife!”
10 Yahweh says this to this people: “Since they love to wander, they have not held back their feet from doing so.” Yahweh is not pleased with them. Now he calls to mind their iniquity and has punished their sins.
Zimene Yehova akunena za anthuwa ndi izi: “Iwo amakonda kuyendayenda kwambiri; samatha kudziretsa. Nʼchifukwa chake Ine Yehova sindingawalandire, ndipo tsopano ndidzakumbukira zoyipa zawo ndi kuwalanga chifukwa cha machimo awo.”
11 Yahweh said to me, “Do not pray for good on behalf of this people.
Kenaka Yehova anandiwuza kuti, “Usawapempherere anthu awa kuti zinthu ziwayendere bwino.
12 For if they fast, I will not listen to their wailing, and if they offer up burnt offerings and food offerings, I will not take pleasure in them. For I will put an end to them by sword, famine, and plague.”
Ngakhale asale zakudya, Ine sindidzamva kulira kwawo; ngakhale apereke nsembe zopsereza ndi chopereka cha chakudya, sindidzazilandira. Mʼmalo mwake, ndidzawapha ndi lupanga, njala ndi mliri.”
13 Then I said, “Oh, Lord Yahweh! Behold! The prophets are saying to the people, 'You will not see the sword; there will be no famine for you, for I will give you true security in this place.'”
Koma ine ndinati, “Aa, Ambuye Yehova, aneneri amawawuza anthuwo kuti, sadzaphedwa ndi lupanga kapena kuvutika ndi njala. Koma kuti Inu mudzawapatsa mtendere wokhawokha pamalo pano.”
14 Yahweh said to me, “The prophets prophesy deceit in my name. I did not send them out, nor did I give them any command or speak to them. But deceitful visions and useless, deceitful divination coming from their own minds are what they are prophesying to you.”
Ndipo Yehova anandiwuza kuti, “Ndi zabodza kuti aneneriwa akunenera mʼdzina langa. Ine sindinawatume kapena kuwasankha kapenanso kuyankhula nawo. Iwo amakuwuzani zinthu zabodza zomwe amati anaziona mʼmasomphenya, kapena pogwiritsa ntchito mawula achabechabe. Zimene amayankhula ndi zongopeka mʼmutu mwawo.
15 Therefore Yahweh says this, “About the prophets prophesying in my name but whom I did not send out—those who say there will be no sword or famine in this land: These prophets will perish by sword and famine.
Nʼchifukwa chake Ine Yehova ndikuti aneneri amenewa akulosera mʼdzina langa pamene Ine sindinawatume. Iwo amati simudzafa pa nkhondo kapena ndi njala mʼdziko muno. Koma tsono ndi iwowo, aneneriwa amene adzafe pa nkhondo kapena ndi njala.
16 Then the people to whom they prophesied will be thrown out in the streets of Jerusalem because of famine and sword, for there will be no one to bury them—them, their wives, their sons, or their daughters—for I will pour out their wickedness on them.
Ndipo anthu amene anawaloserawo adzaponyedwa mʼmisewu ya mu Yerusalemu atafa ndi njala ndi lupanga. Sipadzapezeka wowayika mʼmanda popeza iwowo, akazi awo, ana awo aamuna, onse adzakhala atafa. Ine ndidzawagwetsera chilango chowayenera.
17 Say this word to them: 'Let my eyes flow with tears, night and day. Do not let them stop, for there will be a great collapse of the virgin daughter of my people— a great and incurable wound.
“Awuze mawu awa: “‘Maso anga akugwetsa misozi kosalekeza usana ndi usiku; chifukwa anthu anga okondedwa apwetekeka kwambiri, akanthidwa kwambiri.
18 If I go out to the field, there are the ones who were killed by the sword! If I come to the city, there are the diseases that are caused by famine. Both the prophet and the priest wander about the land, and they do not know.'”
Ndikapita kuthengo, ndikuona amene aphedwa ndi lupanga; ndikapita mu mzinda, ndikuona amene asakazidwa ndi njala. Ngakhale aneneri pamodzi ndi ansembe onse atengedwa.’”
19 Have you completely rejected Judah? Do you hate Zion? Why will you afflict us when there is no healing for us? We hoped for peace, but there was nothing good— and for a time of healing, but see, there is only terror.
Kodi anthu a ku Yuda mwawakana kwathunthu? Kodi mtima wanu wanyansidwa nawo anthu a ku Ziyoni? Chifukwa chiyani mwatikantha chotere kuti sitingathenso kuchira? Ife tinayembekezera mtendere koma palibe chabwino chomwe chabwera, tinayembekezera kuchira koma panali kuopsezedwa kokhakokha.
20 We admit, Yahweh, our offenses, the iniquity of our ancestors, for we have sinned against you.
Inu Yehova, ife tikuvomereza kuyipa kwathu ndiponso kulakwa kwa makolo athu; ndithu ife tinakuchimwiranidi.
21 Do not reject us! For the sake of your name, do not make your glorious throne a disgrace. Remember and do not break your covenant with us.
Musatikane kuopa kuti dzina lanu linganyozedwe; musanyoze mpando wanu waufumu waulemerero. Kumbukirani pangano lanu ndi ife ndipo musachiphwanye.
22 Do any of the worthless idols of the nations bring rain? Or can the skies themselves send down showers? Are you not the one, Yahweh our God? We wait for you, for you are the one who does all these things.
Mwa milungu yachabechabe ya anthu a mitundu ina, kodi pali mulungu amene angagwetse mvula? Ife chikhulupiriro chathu chili pa Inu, popeza Inu nokha ndinu Yehova Mulungu wathu amene mukhoza kuchita zimenezi.