< Isaiah 38 >
1 In those days Hezekiah was sick to the point of dying. So Isaiah son of Amoz, the prophet, came to him, and said to him, “Yahweh says, 'Set your house in order; for you will die, not live.'”
Nthawi imeneyo Mfumu Hezekiya anadwala ndipo anali pafupi kufa. Mneneri Yesaya mwana wa Amozi anapita kukamuona ndipo anati “Yehova akuti: Konza bwino nyumba yako, pakuti ukufa; suchira.”
2 Then Hezekiah turned his face to the wall and prayed to Yahweh.
Hezekiya anatembenuka nayangʼana kukhoma, napemphera kwa Yehova kuti,
3 He said, “Please, Yahweh, call to mind how I have faithfully walked before you with my whole heart, and how I have done what was good in your sight.” Then Hezekiah wept loudly.
“Inu Yehova, kumbukirani momwe ndayendera pamaso panu mokhulupirika ndi modzipereka ndipo ndakhala ndikuchita zabwino pamaso panu.” Ndipo Hezekiya analira mosweka mtima.
4 Then the word of Yahweh came to Isaiah, saying,
Ndipo Yehova analamula Yesaya kuti:
5 “Go and say to Hezekiah, the leader of my people, 'This is what Yahweh, the God of David your ancestor, says: I have heard your prayer, and I have seen your tears. See, I am about to add fifteen years to your life.
“Pita kwa Hezekiya ndipo ukamuwuze kuti, ‘Yehova, Mulungu wa kholo lake Davide akuti: Ndamva pemphero lako ndipo misozi yako ndayiona; ndidzakuwonjezera zaka 15 pa moyo wako.
6 Then I will rescue you and this city from the hand of the king of Assyria, and I will defend this city.
Ndipo ndidzakupulumutsa, iwe pamodzi ndi mzindawu mʼdzanja la mfumu ya ku Asiriya, Ine ndidzawuteteza mzindawu.
7 This will be the sign to you from Yahweh, that I will do what I have promised.
“‘Ichi ndi chizindikiro cha Yehova kwa iwe kutsimikiza kuti Yehova adzachita zimene walonjeza:
8 Look, I will cause the shadow on the stairs of Ahaz to go back ten steps.'” So the shadow went back ten steps of the stairs on which it had advanced.
Chithunzithunzi chimene dzuwa likuchititsa pa makwerero a Ahazi ndidzachibweza mʼmbuyo makwerero khumi.’” Ndipo chithunzithunzi chinabwerera mʼmbuyo makwerero khumi.
9 This was the written prayer of Hezekiah king of Judah, when he had been sick and then recovered:
Ndakatulo ya Hezekiya mfumu ya ku Yuda imene analemba atadwala ndi kuchira:
10 “I said that halfway through my life I will go through the gates of Sheol; I am sent there for the rest of my years. (Sheol )
Ine ndinaganiza kuti ndidzapita ku dziko la akufa pamene moyo ukukoma. (Sheol )
11 I said that I will no longer see Yahweh, Yahweh in the land of the living; I will no longer look on mankind or the inhabitants of the world.
Ndinaganiza kuti, “Sindidzaonanso Yehova, mʼdziko la anthu amoyo, sindidzaonanso mtundu wa anthu kapena kukhala pamodzi ndi amene amakhala pa dziko lapansi lino.
12 My life is removed and carried away from me like a shepherd's tent; I have rolled up my life like a weaver; you are cutting me off from the loom; between day and night you are ending my life.
Nyumba yanga yasasuka ndipo yachotsedwa. Ngati tenti ya mʼbusa mwapindapinda moyo wanga, ngati munthu wowomba nsalu; kuyambira usana mpaka usiku mwakhala mukundisiya.
13 I cried out until the morning; like a lion he breaks all my bones. Between day and night you are ending my life.
Ndinkalira kupempha chithandizo usiku wonse mpaka mmawa; koma Inu Yehova munaphwanya mafupa anga ngati mkango, ndipo mwakhala mukundisiya.
14 Like a swallow I chirp; I coo like a dove; my eyes grow tired with looking upward. Lord, I am oppressed; help me.
Ndinkalira ngati namzeze kapena chumba, ndinkabuwula ngati nkhunda yodandaula. Maso anga anatopa nʼkuyangʼana mlengalenga. Inu Ambuye, ine ndili mʼmavuto bwerani mudzandithandize!”
15 What shall I say? He has both spoken to me, and has done it; I will walk slowly all my years because I am overcome with grief.
Koma ine ndinganene chiyani? Yehova wayankhula nane, ndipo Iye ndiye wachita zimenezi. Chifukwa cha kuwawa kwa mtima wanga, ine ndidzayenda modzichepetsa masiku amoyo wanga onse.
16 Lord, the sufferings you send are good for me; may my life be given back to me; you have restored my life and health.
Ambuye, masiku anga ali mʼmanja mwanu. Mzimu wanga upeza moyo mwa Inu. Munandichiritsa ndi kundikhalitsa ndi moyo.
17 It was for my benefit that I experienced such grief. You have rescued me from the pit of destruction; for you have thrown all my sins behind your back.
Ndithudi, ine ndinamva zowawa zotere kuti ndikhale ndi moyo; Inu munandisunga kuti ndisapite ku dzenje la chiwonongeko chifukwa mwakhululukira machimo anga onse.
18 For Sheol does not thank you; death does not praise you; those who go down into the pit do not hope in your trustworthiness. (Sheol )
Pakuti akumanda sangathe kukutamandani, akufa sangayimbe nyimbo yokutamandani. Iwo amene akutsikira ku dzenje sangakukhulupirireni. (Sheol )
19 The living person, the living person, he is the one who gives you thanks, as I do this day; a father makes known to children your trustworthiness.
Amoyo, amoyo okha ndiwo amakutamandani, monga mmene ndikuchitira ine lero lino; abambo amawuza ana awo za kukhulupirika kwanu.
20 Yahweh is about to save me, and we will celebrate with music all the days of our lives in the house of Yahweh.”
Yehova watipulumutsa. Tiyeni tiyimbe ndi zoyimbira za zingwe masiku onse a moyo wathu mʼNyumba ya Yehova.
21 Now Isaiah had said, “Let them take a lump of figs and put it on the boil, and he will recover.”
Yesaya anati, “Anthu atenge mʼbulu wankhunyu ndipo apake pa chithupsacho ndipo Hezekiya adzachira.”
22 Hezekiah also had said, “What will be the sign that I should go up to the house of Yahweh?”
Hezekiya nʼkuti atafunsa kuti, “Kodi chizindikiro chako nʼchiyani chotsimikiza kuti ndidzapita ku Nyumba ya Yehova?”