< Isaiah 25 >

1 Yahweh, you are my God; I will exalt you, I will praise your name; for you have done wonderful things, things planned long ago, in perfect faithfulness.
Yehova ndinu Mulungu wanga; ine ndidzakukwezani ndi kutamanda dzina lanu, pakuti mwachita zodabwitsa zimene munakonzekeratu kalekale mokhulupirika kwambiri.
2 For you have made the city a heap, a fortified city, a ruin, and a fortress of strangers into no city.
Inu mwasandutsa mzinda uja kukhala mulu wamiyala. Ndipo mzinda wamalinga wasanduka bwinja, linga la anthu achilendo lero si mzindanso ndipo sidzamangidwanso.
3 Therefore a strong people will glorify you; a city of ruthless nations will fear you.
Nʼchifukwa chake anthu amphamvu adzakulemekezani; mizinda ya mitundu ya anthu ankhanza idzakuopani.
4 For you have been a place of safety for the one who is poor, a shelter for the one who is needy in his distress— a shelter from the storm and a shade from the heat. When the breath of the ruthless was like a storm against a wall,
Inu mwakhala ngati populumukira pa anthu osauka, mwakhala ngati kobisalirako munthu wovutika pa nthawi ya masautso ake. Mwakhala ngati pobisalirapo pa nthawi ya mphepo yamkuntho ndi mthunzi pa nthawi ya dzuwa. Pakuti anthu ankhanza ali ngati mphepo yamkuntho yowomba pa khoma,
5 and like heat in a dry land, you subdued the noise of foreigners, as the heat is subdued by the shade of a cloud, so the song of the ruthless ones is answered.
ndiponso ngati kutentha mʼdziko lowuma. Inu mumaletsa phokoso la anthu achilendo. Monga momwe mthunzi wa mtambo umachepetsa kutentha, inu munaletsa nyimbo za anthu ankhanza.
6 On this mountain Yahweh of hosts will make for all peoples a feast of fat things, of choice wines, of tender meats, a feast on the lees.
Pa phiri ili Yehova Wamphamvuzonse adzakonzera anthu a mitundu yonse madyerero a zakudya zokoma ndi vinyo wabwino. Phwando la nyama yonona ndi vinyo wabwino kwambiri.
7 He will destroy on this mountain the covering over all peoples, the web woven over all the nations.
Iye adzachotsa kulira kumene kwaphimba anthu ngati nsalu. Adzachotsa chinsalu chimene chakuta mitundu yonse ya anthu.
8 He will swallow up death forever, and the Lord Yahweh will wipe away tears from off all faces; the disgrace of his people he will take away from all the earth, for Yahweh has spoken it.
Yehova adzathetsa imfa mpaka muyaya, Ambuye Yehova adzapukuta misozi mʼmaso mwa munthu aliyense; adzachotsa manyazi a anthu ake pa dziko lonse lapansi, Yehova wayankhula.
9 It will be said on that day, “Look, this is our God; we have waited for him, and he will save us. This is Yahweh; we have waited for him, we will be glad and rejoice in his salvation.”
Tsiku limenelo iwo adzati, “Ndithudi, uyu ndiye Mulungu wathu; ife tinamudalira ndipo anatipulumutsa. Uyu ndiye Yehova, ife tinamudalira; tiyeni tikondwe ndi kusangalala chifukwa watipulumutsa.”
10 For on this mountain the hand of Yahweh will rest; and Moab will be trampled down in his place, even as straw is trampled down in a pit filled with manure.
Yehova adzateteza phiri limeneli ndi dzanja lake; ndipo Amowabu adzawapondereza pomwe alilipo, ngati mmene amapondera manyowa mʼdzenje.
11 They will spread their hands in the midst of it, as a swimmer spreads his hands to swim. But Yahweh will bring down their pride in spite of the skill of their hands.
Amowabuwo adzatambasula manja awo mʼmenemo, ngati mmene amachitira munthu wosambira. Koma Mulungu adzathetsa kunyada kwawo ngakhale luso la manja awo.
12 Your high fortress walls he will bring down to the ground, to the dust.
Iye adzagumula malinga awo ataliatali ndipo adzawagwetsa ndi kuwaponya pansi, pa fumbi penipeni.

< Isaiah 25 >