< Hosea 3 >

1 Yahweh said to me, “Go again, love a woman, loved by her husband, but who is an adulteress. Love her just as I, Yahweh, love the people of Israel, although they turn to other gods and love raisin cakes.”
Yehova anati kwa ine, “Pita kamukondenso mkazi wako, ngakhale ali pa chibwenzi ndi wina ndi kuti ndi wachigololo. Mukonde iyeyo monga momwe Yehova amakondera Aisraeli, ngakhale iwo amapita kukapembedza milungu ina ndi kukonda nsembe za keke zamphesa zowuma.”
2 So I bought her for myself for fifteen pieces of silver and a homer and a lethek of barley.
Motero ndinamukwatira popereka ndalama khumi ndi zisanu zasiliva, ndiponso mitanga isanu ndi iwiri ya barele.
3 I said to her, “You must live with me many days. You will not be a prostitute or belong to any other man. In the same way, I will be with you.”
Kenaka ndinamuwuza mkaziyo kuti, “Ukhale nane masiku ambiri; usachitenso zachiwerewere kapena chigololo ndi munthu wina, ndipo ine ndidzakhala nawe.”
4 For the people of Israel will live for many days without a king, prince, sacrifice, stone pillar, ephod or household idols.
Pakuti Aisraeli adzakhala masiku ambiri opanda mfumu kapena kalonga, osapereka nsembe kapena kuyimika miyala yachipembedzo, wopanda efodi kapena fano.
5 Afterward the people of Israel will return and seek Yahweh their God and David their king, and in the last days, they will come trembling before Yahweh and his goodness.
Pambuyo pake Aisraeli adzabwerera ndi kufunafuna Yehova Mulungu wawo ndi Davide mfumu yawo. Adzabwera kwa Yehova akunjenjemera ndipo adzalandira madalitso mʼmasiku awo otsiriza.

< Hosea 3 >