< Genesis 5 >

1 This is the record of the descendants of Adam. On the day that God created mankind, he made them in his own likeness.
Ndondomeko ya mibado ya Adamu ndi iyi: Pamene Mulungu analenga munthu, anamulenga mʼchifaniziro cha Mulungu.
2 Male and female he created them. He blessed them and named them mankind when they were created.
Iye analenga mwamuna ndi mkazi. Anawadalitsa ndipo anawatcha “Munthu.”
3 When Adam had lived 130 years, he became the father of a son in his own likeness, after his image, and he called his name Seth.
Pamene Adamu anali ndi zaka 130, anabereka mwana wamwamuna wofanana naye ndipo anamutcha Seti.
4 After Adam became the father of Seth, he lived eight hundred years. He became the father of more sons and daughters.
Atabadwa Seti, Adamu anakhala ndi moyo zaka zina 800 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
5 Adam lived 930 years, and then he died.
Zaka zonse za Adamu zinali 930 ndipo anamwalira.
6 When Seth had lived 105 years, he became the father of Enosh.
Pamene Seti anali ndi zaka 105, anabereka Enosi.
7 After he became the father of Enosh, he lived 807 years and became the father of more sons and daughters.
Atabadwa Enosi, Seti anakhala ndi moyo zaka zina 807 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
8 Seth lived 912 years, and then he died.
Zaka zonse za Seti zinali 912 ndipo anamwalira.
9 When Enosh had lived ninety years, he became the father of Kenan.
Pamene Enosi anali ndi zaka 90, anabereka Kenani.
10 After he became the father of Kenan, Enosh lived 815 years. He became the father of more sons and daughters.
Atabadwa Kenani, Enosi anakhala ndi moyo zaka zina 815 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
11 Enosh lived 905 years, and then he died.
Zaka zonse za Enosi pamodzi zinali 905 ndipo anamwalira.
12 When Kenan had lived seventy years, he became the father of Mahalalel.
Pamene Kenani anali ndi zaka 70, anabereka Mahalaleli.
13 After he became the father of Mahalalel, Kenan lived 840 years. He became the father of more sons and daughters.
Atabadwa Mahalaleli, Kenani anakhala ndi moyo zaka zina 840 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
14 Kenan lived 910 years, and then he died.
Zaka zonse za Kenani zinali 910, ndipo anamwalira.
15 When Mahalalel had lived sixty-five years, he became the father of Jared.
Pamene Mahalaleli anali ndi zaka 65, anabereka Yaredi.
16 After he became the father of Jared, Mahalalel lived 830 years. He became the father of more sons and daughters.
Atabadwa Yaredi, Mahalaleli anakhala ndi moyo zaka zina 830 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
17 Mahalalel lived 895 years, and then he died.
Zaka zonse za Mahalaleli zinali 895 ndipo anamwalira.
18 When Jared had lived 162 years, he became the father of Enoch.
Pamene Yaredi anali ndi zaka 162, anabereka Enoki.
19 After he became the father of Enoch, Jared lived eight hundred years. He became the father of more sons and daughters.
Atabadwa Enoki, Yaredi anakhala ndi moyo zaka zina 800 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
20 Jared lived 962 years, and then he died.
Zaka zonse za Yaredi zinali 962 ndipo anamwalira.
21 When Enoch had lived sixty-five years, he became the father of Methuselah.
Pamene Enoki anali ndi zaka 65, anabereka Metusela.
22 Enoch walked with God three hundred years after he became the father of Methuselah. He became the father of more sons and daughters.
Atabadwa Metusela, Enoki anayenda ndi Mulungu zaka 300 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
23 Enoch lived 365 years.
Zaka zonse za Enoki zinali 365.
24 Enoch walked with God, and then he was gone, for God took him.
Enoki anayenda ndi Mulungu; ndipo iye sanaonekenso chifukwa Mulungu anamutenga.
25 When Methuselah had lived 187 years, he became the father of Lamech.
Pamene Metusela anali ndi zaka 187, anabereka Lameki.
26 After he became the father of Lamech, Methuselah lived 782 years. He became the father of more sons and daughters.
Ndipo atabadwa Lameki, Metusela anakhala ndi moyo zaka zina 782 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
27 Methuselah lived 969 years. Then he died.
Zaka zonse za Metusela zinali 969, ndipo anamwalira.
28 When Lamech had lived 182 years, he became the father of a son.
Pamene Lameki anali ndi zaka 182, anabereka mwana wamwamuna.
29 He called his name Noah, saying, “This one will give us rest from our work and from the painful labor of our hands, which we must do because of the ground that Yahweh has cursed.”
Ndipo anamutcha Nowa ndipo anati, “Iyeyu adzatipumulitsa ku ntchito zathu zolemetsazi, zolima nthaka imene Yehova anayitemberera.”
30 Lamech lived 595 years after he became the father of Noah. He became the father of more sons and daughters.
Atabadwa Nowa, Lameki anakhala zaka zina 595 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
31 Lamech lived 777 years. Then he died.
Zaka zonse za Lameki zinali 777, ndipo kenaka anamwalira.
32 After Noah had lived five hundred years, he became the father of Shem, Ham, and Japheth.
Pamene Nowa anali ndi zaka 500, anabereka Semu, Hamu ndi Yafeti.

< Genesis 5 >