< Genesis 38 >

1 It came about at that time that Judah left his brothers and stayed with a certain Adullamite, whose name was Hirah.
Pa nthawi imeneyi, Yuda anasiyana ndi abale ake napita kukakhala ndi munthu wina wa ku Adulamu wotchedwa Hira.
2 He met there a daughter of a Canaanite man whose name was Shua. He married her and slept with her.
Kumeneko, Yuda anaona mwana wamkazi wa munthu wina wa Chikanaani wotchedwa Suwa. Anamukwatira nagona naye malo amodzi.
3 She became pregnant and had a son. He was named Er.
Iye anatenga pathupi, nabala mwana wamwamuna amene anamutcha Eri.
4 She became pregnant again and had a son. She called his name Onan.
Anatenganso pathupi nabala mwana wa mwamuna ndipo anamutcha Onani.
5 She again had a son and called his name Shelah. It was at Kezib where she gave birth to him.
Anaberekanso mwana wina wamwamuna ndipo anamutcha Sela. Ameneyu anabadwa Yuda ali ku Kezibi.
6 Judah found a wife for Er, his firstborn. Her name was Tamar.
Yuda anamupezera mkazi mwana wake woyamba uja Eri, ndipo dzina la mkaziyo linali Tamara.
7 Er, Judah's firstborn, was wicked in the sight of Yahweh. Yahweh killed him.
Koma ntchito zoyipa za Eri, mwana wachisamba wa Yuda zinayipira Yehova. Choncho Mulungu anamulanga ndi imfa.
8 Judah said to Onan, “Sleep with your brother's wife. Do the duty of a brother-in-law to her, and raise up a child for your brother.”
Pamenepo Yuda anati kwa Onani, “Kwatira mkazi wamasiye wa mʼbale wako. Ulowe chokolo kuti mʼbale wako akhale ndi mwana.”
9 Onan knew that the child would not be his. Whenever he slept with his brother's wife, he spilled the semen on the ground so he would not have a child for his brother.
Koma Onani anadziwa kuti mwanayo sadzakhala wake. Choncho nthawi zonse pamene amagona naye mkaziyo, ankatayira umuna pansi kuti asamuberekere mwana mʼbale wake.
10 What he did was evil in the sight of Yahweh. Yahweh killed him also.
Zimene ankachitazi zinayipira Yehova. Choncho anamulanganso ndi imfa.
11 Then Judah said to Tamar, his daughter-in-law, “Remain a widow in your father's house until Shelah, my son, grows up.” For he feared, “He might also die, just like his brothers.” Tamar left and lived in her father's house.
Kenaka Yuda anati kwa mpongozi wake Tamara, “Bwererani ku nyumba ya abambo anu ndi kukhala kumeneko ngati wamasiye mpaka mwana wanga Sela atakula.” Ananena izi chifukwa ankaopa kuti Sela angafenso ngati abale ake aja. Choncho Tamara anapita kukakhala ku nyumba ya abambo ake.
12 After a long time, Shua's daughter, the wife of Judah, died. Judah was comforted and went up to his sheepshearers at Timnah, he and his friend Hirah the Adullamite.
Patapita nthawi yayitali, Batishua, mkazi wa Yuda anamwalira. Yuda atatha kulira maliro a mkazi wake, anapita, iyeyu pamodzi ndi bwenzi lake Hira, Mwadulamu uja, ku Timna kumene ankameta nkhosa zawo.
13 Tamar was told, “Look, your father-in-law is going up to Timnah to shear his sheep.”
Tamara atamva kuti apongozi ake akupita ku Timna kukameta nkhosa,
14 She took off the clothing of her widowhood and covered herself with her veil and wrapped herself. She sat in the gate of Enaim, which is by the road to Timnah. For she saw that Shelah had grown up but she had not been given to him as a wife.
iye anavula zovala zake za umasiye, nadziphimba nkhope ndi nsalu kuti asadziwike, ndipo anakhala pansi pa chipata cha ku Enaimu popita ku Timna. Tamara anachita izi chifukwa anaona kuti ngakhale Selayo anali atakula tsopano, iye sanaperekedwe kuti amulowe chokolo.
15 When Judah saw her he thought that she was a prostitute because she had covered her face.
Yuda atamuona anangomuyesa mkazi wadama chabe, chifukwa anadziphimba nkhope.
16 He went to her by the road and said, “Come, please let me sleep with you”—for he did not know that she was his daughter-in-law—and she said, “What will you give me so you can sleep with me?”
Tsono anapita kwa mkaziyo pamphepete pa msewu paja nati, “Tabwera ndigone nawe.” Apa Yuda sankadziwa kuti mkazi uja anali mpongozi wake. Ndiye mkazi uja anamufunsa Yuda nati, “Mudzandipatsa chiyani kuti ndigone nanu?”
17 He said, “I will send you a young goat from the flock.” She said, “Will you give me a pledge until you send it?”
Iye anati, “Ndidzakutumizira kamwana kambuzi ka mʼkhola mwanga.” Mkaziyo anayankha kuti, “Chabwino, ndavomera, koma mungandipatse chikole mpaka mutanditumizira mbuziyo?”
18 He said, “What pledge can I give you?” She replied, “Your seal and cord, and the staff that is in your hand.” He gave them to her and slept with her, and she became pregnant by him.
Iye anati, “Ndikupatse chikole chanji?” Mkaziyo anayankha, “Mundipatse mphete yanuyo, chingwe chanucho pamodzi ndi ndodo imene ili mʼdzanja lanulo.” Choncho anazipereka kwa iye nagona naye ndipo anatenga pathupi.
19 She got up and went away. She took off her veil and put on the clothing of her widowhood.
Kenaka Tamara anachoka, navula nsalu anadziphimba nayo ija, navalanso zovala zake za umasiye zija.
20 Judah sent the young goat by his friend the Adullamite in order that he might receive the pledge back from the woman's hand, but he did not find her.
Tsono Yuda anatuma bwenzi lake Mwadulamu uja ndi kamwana kambuzi kaja kuti akapereke kwa mkazi wadama uja, ndi kuti akatero amubwezere chikole chake chija. Koma atafika sanamupezepo.
21 Then the Adullamite asked the men of the place, “Where is the cultic prostitute who was at Enaim by the road?” They said, “There has not been a cultic prostitute here.”
Anawafunsa anthu a komweko, “Kodi mkazi wadama uja amene ankakhala pambali pa msewu wa ku Enaimu, ali kuti?” Iwo anayankha, “Sipanakhalepo mkazi wa dama aliyense pano.”
22 He returned to Judah and said, “I did not find her. Also, the men of the place said, 'There has not been a cultic prostitute here.'”
Choncho anabwerera kwa Yuda nati, “Sindinamupeze mkazi uja. Kuwonjeza apo, anthu a kumeneko amati, ‘Sipanakhalepo mkazi wadama pano.’”
23 Judah said, “Let her keep the things, that we not be put to shame. Indeed, I sent this young goat, but you did not find her.”
Pamenepo Yuda anati, “Mulekeni atenge zinthuzo zikhale zake, kuopa kuti anthu angatiseke. Ine sindinalakwe, ndinamutumizira kamwana kambuzika, koma simunamupeze.”
24 It came about after about three months that it was told to Judah, “Tamar your daughter-in-law has committed prostitution, and indeed, she is pregnant by it.” Judah said, “Bring her here and let her be burned.”
Patapita miyezi itatu, Yuda anawuzidwa kuti, “Mpongozi wanu Tamara anachita zadama, ndipo zotsatira zake nʼzakuti ali ndi pathupi.” Yuda anati, “Kamutulutseni ndipo mukamutenthe kuti afe!”
25 When she was brought out, she sent to her father-in-law a message, “By the man who owns these I am pregnant.” She said, “Determine please whose these are, the seal and cords and staff.”
Akumutulutsa, iye anatuma mawu kwa apongozi ake. Anati, “Ndili ndi pathupi pa munthu amene ndi mwini wake wa zinthu izi. Taziyangʼanitsitsani, kodi mwini wa khoza, chingwe ndi ndodo yoyenderayi ndi yani?”
26 Judah recognized them and said, “She is more righteous than I am, since I did not give her as a wife to Shelah, my son.” He did not sleep with her again.
Yuda anazizindikira zinthuzo ndipo anati, “Uyu ndi wolungama kuposa ine, chifukwa sindinamupereke kwa mwana wanga Sela.” Ndipo Yuda sanagone nayenso.
27 It came about at the time for her to give birth that, behold, twins were in her womb.
Pamene Tamara nthawi inamukwanira yoti abeleke, mʼmimbamo munali mapasa.
28 It came about as she was giving birth one put out a hand, and the midwife took a scarlet thread and tied it on his hand and said, “This one came out first.”
Pamene ankabereka, mmodzi wa iwo anatulutsa dzanja lake. Choncho mzamba anatenga kawulusi kofiira nakamangirira pa mkono pa mwanayo nati, “Uyu ndiye anayamba kubadwa.”
29 But then he drew back his hand, and, behold, his brother came out first. The midwife said, “How you have broken out!” So he was named Perez.
Koma pamene anabweza mkonowo, mʼbale wake anabadwa ndipo mzamba anati, “Wachita kudziphotcholera wekha njira chonchi!” Ndipo anamutcha Perezi.
30 Then his brother came out, who had the scarlet thread upon his hand, and he was named Zerah.
Pambuyo pake mʼbale wake amene anali ndi ulusi wofiira pa mkono wake uja anabadwa ndipo anapatsidwa dzina lakuti Zera.

< Genesis 38 >