< Genesis 27 >
1 When Isaac was old and his eyes were dim so that he could not see, he called Esau, his older son, and said to him, “My son.” He said to him, “Here I am.”
Isake atakalamba maso ake anachita khungu mwakuti sankatha kuona. Iye anayitana mwana wake wamkulu Esau nati kwa iye, “Mwana wanga.” Iye anayankha, “Ine abambo.”
2 He said, “See here, I am old. I do not know the day of my death.
Isake anati, “Tsopano ine ndakalamba, ndipo sindidziwa tsiku langa lakufa.
3 Therefore take your weapons, your quiver and your bow, and go out to the field and hunt game for me.
Tsono tenga zida zako, muvi wako ndi uta, pita kuthengo ukandiphere nyama.
4 Make delicious food for me, the sort that I love, and bring it to me so I can eat it and bless you before I die.”
Undikonzere chakudya chabwino monga muja ndimakonderamu ndipo ubwere nacho kwa ine kuti ndidye ndi kuti ndikudalitse ndisanamwalire.”
5 Now Rebekah heard it when Isaac spoke to Esau his son. Esau went to the field to hunt for game and bring it back.
Koma Rebeka amamvetsera pamene Isake amayankhula ndi mwana wake Esau. Esau atanyamuka kupita kuthengo kukaphera abambo ake nyama,
6 Rebekah spoke to Jacob her son and said, “See here, I heard your father speak to Esau your brother. He said,
Rebeka anati kwa mwana wake Yakobo, “Taona ndamva abambo ako akuwuza mʼbale wako Esau kuti,
7 'Bring me game and make me delicious food, that I may eat it and bless you in the presence of Yahweh before my death.'
‘Bweretsere nyama yakutchire ndipo undikonzere chakudya chokoma kuti ndidye; kuti ndikudalitse pamaso pa Yehova ndisanamwalire.’
8 Now therefore, my son, obey my voice as I command you.
Tsopano mwana wanga, mvetsetsa ndipo uchite zimene ndikuwuze:
9 Go to the flock, and bring me two good young goats; and I will make delicious food from them for your father, just like he loves.
Pita ku khola, ukatenge ana ambuzi abwino awiri, kuti ndikonzere abambo ako chakudya chokoma monga amakondera.
10 You will take it to your father, so that he may eat it, so that he may bless you before his death.”
Kenaka upite nacho chakudyacho kwa abambo ako kuti adye ndi kukudalitsa asanafe.”
11 Jacob said to Rebekah his mother, “See, Esau my brother is a hairy man, and I am a smooth man.
Koma Yakobo anati kwa Rebeka amayi ake, “Komatu mʼbale wanga Esau ndi munthu wa khungu la ubweya zedi, ndipo ine ndine munthu wa khungu losalala.
12 Perhaps my father will touch me, and I will seem to him as a deceiver. I will bring a curse upon me and not a blessing.”
Mwina abambo anga adzandikhudza, ndipo ndidzaoneka kuti ndawapusitsa. Tsono ndizadzitengera temberero mʼmalo mwa madalitso.”
13 His mother said to him, “My son, let any curse fall on me. Just obey my voice, and go, bring them to me.”
Amayi ake anati kwa iye, “Mwana wanga, temberero limenelo ligwere ine. Iwe ungochita zimene ine ndikukuwuza; pita kanditengere timbuzito.”
14 So Jacob went and got the young goats and brought them to his mother, and his mother made delicious food, just like his father loved.
Choncho anapita nakatenga timbuzito ndi kubwera nato kwa amayi ake. Choncho Rebeka anaphika chakudya chokoma monga momwe Isake amakondera.
15 Rebekah took the best clothes of Esau, her older son, which were with her in the house, and put them on Jacob, her younger son.
Tsono Rebeka anatenga zovala zabwino kwambiri za Esau mwana wake wamkulu zimene zinali mʼnyumba namuveka Yakobo.
16 She put the skins of the young goats on his hands and on the smooth part of his neck.
Anamuvekanso manja ake ndi khosi lake ndi zikopa za mwana wambuzi.
17 She put the delicious food and the bread that she had prepared into the hand of her son Jacob.
Kenaka, anamupatsa Yakobo chakudya chokoma chija chimene anaphika pamodzi ndi buledi.
18 Jacob went to his father and said, “My father.” He said, “Here I am; who are you, my son?”
Yakobo anapita kwa abambo ake ndipo anati, “Abambo anga.” Ndipo anayankha, “Eya, kodi ndiwe mwana wanga uti?”
19 Jacob said to his father, “I am Esau your firstborn; I have done as you said to me. Now sit up and eat some of my game, that you may bless me.”
Yakobo anati kwa abambo ake, “Ndine Esau mwana wanu woyamba. Ndachita monga munandiwuzira. Chonde dzukani ndi kukhala tsonga kuti mudyeko nyama ndakukonzeraniyi kuti tsono mundidalitse.”
20 Isaac said to his son, “How is it that you have found it so quickly, my son?” He said, “Because Yahweh your God brought it to me.”
Isake anafunsa mwana wake, “Wayipeza msanga chotere bwanji mwana wanga?” Iye anayankha, “Yehova Mulungu wanu anandithandiza kuti ndiyipeze.”
21 Isaac said to Jacob, “Come near me, so I may touch you, my son, and learn whether you are my true son Esau or not.”
Pamenepo Isake anati kwa Yakobo, “Tabwera pafupi ndikukhudze mwana wanga, kuti ndidziwedi ngati uli mwana wanga Esau kapena ayi.”
22 Jacob went over to Isaac his father; and Isaac touched him and said, “The voice is Jacob's voice, but the hands are the hands of Esau.”
Yakobo anasendera kufupi ndi abambo ake Isake ndipo anamukhudza nati, “Mawuwa ndi mawu a Yakobo koma mikonoyi ndi mikono ya Esau.”
23 Isaac did not recognize him, because his hands were hairy, like his brother Esau's hands, so Isaac blessed him.
Sanamuzindikire, popeza mikono yake inali ndi ubweya ngati ya mʼbale wake Esau; choncho anamudalitsa.
24 He said, “Are you really my son Esau?” He replied, “I am.”
Isake anafunsa, “Kodi ndiwedi mwana wanga Esau?” Yakobo anayankha, “Inde ndine.”
25 Isaac said, “Bring the food to me, and I will eat of your game, so that I may bless you.” Jacob brought the food to him. Isaac ate, and Jacob brought him wine, and he drank.
Ndipo iye anati, “Mwana wanga, patseko nyama yakoyo ndidye kuti ndikudalitse.” Yakobo anabwera ndi nyama ija kwa Isake ndipo anadya. Kenaka anamupatsanso vinyo ndipo anamwa.
26 Then his father Isaac said to him, “Come near now and kiss me, my son.”
Tsono Isake anati kwa Yakobo, “Bwera kuno mwana wanga undipsompsone.”
27 Jacob came near and kissed him, and he smelled the smell of his clothes and blessed him. He said, “See, the smell of my son is like the smell of a field that Yahweh has blessed.
Choncho anapita namupsompsona. Apa Isake anamva fungo la zovala zake, ndipo anamudalitsa nati, “Haa, fungo la mwana wanga lili ngati fungo la munda umene Yehova waudalitsa.
28 May God give you a portion of the dew of heaven, a portion of the fatness of the earth, and plenty of grain and new wine.
Mulungu akugwetsere mame akumwamba ndipo minda yako ibale tirigu wambiri ndi vinyo watsopano.
29 May peoples serve you and nations bow down to you. Be master over your brothers, and may your mother's sons bow down to you. May every one who curses you be cursed; may every one who blesses you be blessed.”
Mitundu ya anthu ikutumikire iwe ndipo anthu akugwadire iwe. Ukhale wolamula abale ako, ndipo ana aamuna a amayi ako akugwadire. Amene akutemberera iwe atembereredwe ndipo amene adalitsa iwe adalitsike.”
30 As soon as Isaac had finished blessing Jacob, and Jacob had scarcely gone out from the presence of Isaac his father, Esau his brother came in from his hunting.
Isake atatsiriza kudalitsa Yakobo, atangochoka pamaso pa abambo akewo, Esau anabwera kuchokera kosaka kuja.
31 He also made delicious food and brought it to his father. He said to his father, “Father, get up and eat some of your son's game, so that you may bless me.”
Nayenso anakonza chakudya chokoma nabwera nacho kwa abambo ake. Ndipo anati kwa iye, “Chonde abambo, dzukani mukhale tsonga kuti mudye nyamayi ndi kuti mundidalitse.”
32 Isaac his father said to him, “Who are you?” He said, “I am your son, your firstborn, Esau.”
Abambo ake, Isake, anamufunsa kuti, “Ndiwe yani?” Iye anayankha, “Ndine mwana wanu woyamba Esau.”
33 Isaac trembled very much and said, “Who was it that hunted this game and brought it to me? I ate it all before you came, and I have blessed him. Indeed, he will be blessed.”
Isake ananjenjemera kwambiri nati, “Nanga ndani uja anakapha nyama kutchire nʼkudzandipatsa? Ine ndadya kale, ndadya nyamayo iwe utangotsala pangʼono kubwera ndipo ndamudalitsa ndipo adzakhaladi wodalitsika.”
34 When Esau heard the words of his father, he cried with a very great and bitter cry, and said to his father, “Bless me, me also, my father.”
Esau atamva mawu a abambo ake, analira mokweza ndi mowawidwa mtima nati kwa abambo ake, “Inenso dalitseni abambo anga!”
35 Isaac said, “Your brother came here deceitfully and has taken away your blessing.”
Koma iye anati, “Mʼbale wako anabwera mwachinyengo ndipo watenga madalitso ako.”
36 Esau said, “Is he not rightly named Jacob? For he has cheated me these two times. He took away my birthright, and, see, now he has taken away my blessing.” Then he said, “Have you not reserved a blessing for me?”
Esau anati, “Kodi nʼchifukwa chake iyeyu dzina lake lili Yakobo eti? Aka nʼkachiwiri kundinyenga: Anatenga ukulu wanga, pano watenga madalitso anga!” Kenaka anafunsa, “Kodi simunandisungireko ena madalitsowo?”
37 Isaac answered and said to Esau, “Look, I have made him your master, and I have given to him all his brothers as servants, and I have given him grain and new wine. What more can I do for you, my son?”
Koma Isake anamuyankha nati, “Ndamudalitsa iye kuti akhale wokulamulira iwe. Ndaperekanso abale ake onse kuti akhale omutumikira iye, ndipo ndamudalitsa ndi tirigu wambiri, ndi vinyo watsopano. Ndiye ndingakuchitirenso chiyani mwana wanga?”
38 Esau said to his father, “Have you not even one blessing for me, my father? Bless me, even me too, my father.” Esau wept loudly.
Esau anati kwa abambo ake, “Kodi muli ndi dalitso limodzi lokhali, abambo anga? Inenso mundidalitse chonde abambo anga!” Pomwepo Esau analira mokuwa.
39 Isaac his father answered and said to him, “Look, the place where you live will be far from the richness of the earth, away from the dew of the sky above.
Tsono Isake abambo ake anamuyankha kuti, “Malo ako okhalapo sadzabala dzinthu, ndipo mvula sidzagwa pa minda yako.
40 By your sword you will live, and you will serve your brother. But when you rebel, you will shake his yoke from off your neck.”
Udzakhala ndi moyo podalira lupanga ndipo udzatumikira mʼbale wako. Koma idzafika nthawi pamene udzakhala mfulu udzachotsa goli lake mʼkhosi mwako.”
41 Esau hated Jacob because of the blessing that his father had given him. Esau said in his heart, “The days of mourning for my father are near; after that I will kill my brother Jacob.”
Ndipo Esau anamusungira chiwembu Yakobo chifukwa cha madalitso amene abambo ake anamupatsa. Esau anati kwa iye yekha, “Masiku olira abambo anga ayandikira; pambuyo pake ndidzamupha mʼbale wangayu Yakobo.”
42 The words of Esau her older son were told to Rebekah. So she sent and called Jacob her younger son and said to him, “See, your brother Esau is consoling himself about you by planning to kill you.
Pamene Rebeka anamva zimene mwana wake wamkulu Esau ankaganiza, anayitanitsa Yakobo nati kwa iye, “Mʼbale wako Esau akulingalira zakuti akuphe kuti akulipsire.
43 Now therefore, my son, obey me and flee to Laban, my brother, in Haran.
Tsopano mwana wanga, chita zimene ndinene: Nyamuka tsopano, uthawire kwa mlongo wanga Labani ku Harani.
44 Stay with him for a while, until your brother's fury subsides,
Ukakhale naye kwa kanthawi mpaka mkwiyo wa mʼbale wako utatsika.
45 until your brother's anger turns away from you, and he forgets what you have done to him. Then I will send and bring you back from there. Why should I lose you both in one day?
Tsono mkwiyo wa mʼbale wakoyo ukadzatsika ndi kuyiwala zonse wamuchitirazi, ndidzatuma munthu kuti adzakutenge. Nanga nditayirenji nonse awiri nthawi imodzi?”
46 Rebekah said to Isaac, “I am weary of life because of the daughters of Heth. If Jacob takes one of the daughters of Heth as a wife, like these women, some of the daughters of the land, what good will my life be to me?”
Tsono Rebeka anati kwa Isake, “Ine sindikukondwera nawo anamwali a Chihiti. Ndipo ngati Yakobo angapeze mbeta kuno mwa anamwali a Chihitiwa, ndiye kuli bwino kungofa.”