< Ezekiel 17 >

1 The word of Yahweh came to me, saying,
Yehova anayankhula nane kuti,
2 “Son of man, present a riddle and speak a parable to the house of Israel.
“Iwe mwana wa munthu, aphere mwambi anthu a Israeli ndi kuwawuza fanizo.
3 Say, 'The Lord Yahweh says this: A large eagle with large wings and long pinions, full of feathers, and that was multicolored went to Lebanon and took hold of the top of a cedar tree.
Uwawuze kuti Ambuye Yehova akuti, chiwombankhanga chachikulu, cha mapiko amphamvu, nthenga zitalizitali zamathothomathotho chinabwera ku Lebanoni. Chinagwira nthambi ya pamwamba pa mtengo wa mkungudza.
4 It broke off the tips of the branches and took them to the land of Canaan; he planted it in a city of merchants.
Chinabudula msonga yeniyeni ya nthambiyo nʼkupita nayo ku dziko lamalonda ndipo anakayika mu mzinda wa anthu amalonda.
5 He also took some seed of the land and planted it in fertile soil. He placed it beside a large body of water like a willow.
“‘Kenaka chinatenga mbewu ina ya mʼdziko ndi kukayidzala ku malo a chonde kumene kunali madzi ambiri. Anayidzala ngati mmene amadzalira mtengo wa msondozi.
6 Then it sprouted and became a spreading vine low to the ground. Its branches turned toward him, and its roots grew under it. So it became a vine and produced branches and sent out shoots.
Ndipo inaphuka nisanduka mtengo wa mpesa wotambalala chamʼmunsi. Nthambi zake zinaloza mmwamba kumene kunali chiwombankhangacho, koma mizu yake inalowa pansi. Kotero unakhala mtengo wamphesa ndipo unasanduka wa nthambi ndiponso wa masamba ambiri.
7 But there was another great eagle with large wings and many feathers. Behold! This vine turned its roots toward the eagle, and it spread out its branches toward the eagle from the place it had been planted so it would be watered.
“‘Koma panali chiwombankhanga chinanso chachikulu, cha mapiko amphamvu ndi cha nthenga zambiri. Tsopano mtengo wamphesa uja unakhotetsera mizu yake kwa chiwombankhangacho kuchokera pa malo amene unadzalidwa ndipo unatambalitsa nthambi zake kwa chiwombankhangacho kufuna kuthiridwa madzi.
8 It had been planted in good soil beside a large body of water so it would produce branches and sprout fruit, to become a magnificent vine.'
Koma mtengowo unadzalidwa kale pa nthaka yabwino mʼmbali mwa madzi kuti ukhale ndi nthambi zambiri, ubereke zipatso ndi kukhala wokongola.’
9 Say to the people, 'The Lord Yahweh says this: Will it prosper? Will it not be uprooted and stripped of its fruit so that it withers, and all its fresh growth will wither? No strong arm or many people will be needed to pull it out by its roots.
“Ukawawuze Aisraeli kuti, ‘Ambuye Wamphamvuzonse akuti: Kodi udzakula bwino? Kodi chiwombankhanga chija sichidzawuzula mizu ndi kubudula nthambi zake kuti ufote? Masamba ake onse anthete adzafota. Sipadzafunika dzanja lamphamvu kapena anthu ambiri kuti awuzule.
10 So behold! After it has been planted, will it grow? Will it not wither when the eastern wind touches it? It will completely wither away in the garden plot where it sprouted.'”
Ngakhale utawokedwa pena, kodi udzaphuka? Kodi sudzafoteratu mphepo ya kummawa ikadzawomba, kufotera pa malo pamene anawuwokerapo?’”
11 Then the word of Yahweh came to me, saying,
Kenaka Yehova anandiyankhula nati:
12 “Speak to the rebellious house, 'Do you not know what these things mean? Behold! The king of Babylon came to Jerusalem and took her king and her princes and brought them to him in Babylon.
“Tawafunsa anthu owukirawa kuti, ‘kodi mukudziwa tanthauzo la zinthu zimenezi?’ Uwafotokozere kuti, ‘Mfumu ya Babuloni inapita ku Yerusalemu ndikukatengako mfumu ndi anthu ake otchuka ndi kubwera nawo ku Babuloni.
13 Then he took a royal descendant, made a covenant with him, and brought him under an oath. He took away the powerful people of the land,
Ndipo anatenga mmodzi wa banja laufumu ndi kuchita naye mgwirizano, ndipo anamulumbiritsa kuti akhale womvera. Inatenganso akulu onse a mʼdzikomo
14 so the kingdom might become lowly and not lift itself up. By keeping his covenant the land will survive.
kuti ufumu wa dzikolo utsitsidwe, usadzaphukenso, koma kuti ukhalepobe posunga pangano limene unachita.
15 But the king of Jerusalem rebelled against him by sending his ambassadors to Egypt to acquire horses and an army. Will he succeed? Will the one doing these things escape? If he breaks the covenant, will he escape?
Koma mfumu inawukira mfumu ya ku Babuloni potumiza nthumwi ku dziko la Igupto kukatenga akavalo ndi gulu lalikulu la nkhondo. Kodi mfumu yotereyi ingapambane? Kodi wochita zinthu zoterezi angapulumuke? Kodi angaphwanye mgwirizano ndi kupulumuka?
16 As I live!—this is the Lord Yahweh's declaration—he will surely die in the land of the king who made him king, the king whose oath he despised, and whose covenant he broke. He will die in the middle of Babylon.
“‘Ndithu pali Ine wamoyo, akutero Ambuye Yehova, mfumuyo idzafera ku Babuloni, mʼdziko la mfumu imene inayika pa mpando waufumu. Inapeputsa lumbiro lake nʼkuphwanya pangano limene inachita ndi mfumu inayo.
17 Pharaoh with his mighty army and a great company of men will not help him in battle, when ramps are constructed and siege walls are built up to cut off many lives.
Farao ndi gulu lake lankhondo lamphamvu sadzatha kumuthandiza pa nkhondo, pamene mfumu ya Babuloni idzapanga mitumbira ya nkhondo ndi nsanja za nkhondo kuti iwononge miyoyo yambiri.
18 For the king despised his oath by breaking the covenant. Behold, he reached out with his hand to make a promise and yet he did all these things. He will not escape.
Mfumu ya ku Yuda inanyoza lumbiro lake pophwanya pangano. Inalonjeza komabe sinatsatire malonjezo ake. Choncho sidzapulumuka.
19 Therefore the Lord Yahweh says this: As I live, was it not my oath that he despised and my covenant that he broke? So I will bring his punishment on his head!
“‘Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndithu pali Ine wamoyo, Ine ndidzalanga mfumu imeneyi chifukwa inanyoza lumbiro langa, ndi kuphwanya pangano langa.
20 I will spread my net out over him, and he will be caught in my hunting net. Then I will bring him to Babylon and execute judgment on him there for his treason that he committed when he betrayed me!
Ndidzayitchera ukonde ndipo idzakodwa mu msampha wanga. Ndidzapita nayo ku Babuloni ndi kuyilanga kumeneko chifukwa inali yosakhulupirika kwa Ine.
21 All of his refugees in his armies will fall by the sword, and the ones who remain will be scattered in every direction. Then you will know that I am Yahweh; I have declared this would happen.”
Asilikali ake onse amene akuthawa adzaphedwa ndi lupanga, ndipo opulumuka adzabalalitsidwa ku mbali zonse. Ndipo iwo adzadziwa kuti Ine Yehova ndayankhula.
22 The Lord Yahweh says this, 'So I myself will take away the highest part of the cedar tree, and I will plant it away from its tender branches. I will break it off, and I myself will plant it on a high mountain.
“‘Ambuye Yehova akuti: Ine mwini ndidzatenga nthambi pamwamba penipeni pa mkungudza ndi kuyidzala; ndidzathyola nthambi yanthete kuchokera pa nthambi zapamwamba penipeni ndi kuyidzala pamwamba pa phiri lalitali.
23 I will plant it on the mountains of Israel so it will bear branches and produce fruit, and it will become a majestic cedar so that every winged bird will live under it. They will nest in the shade of its branches.
Ndidzayidzaladi pa phiri lalitali la Israeli. Idzaphuka nthambi ndi kubereka zipatso. Choncho idzasanduka mkungudza wamphamvu. Mbalame za mtundu uliwonse zidzamanga zisa zawo mʼmenemo; zidzapeza malo okhala mu mthunzi wa nthambi zake.
24 Then all the trees of the field will know that I am Yahweh. I bring down the high trees and I raise up the low trees. I wither the watered tree and I cause the dried tree to bloom. I am Yahweh, I have declared that this will happen; and I have done it.'”
Mitengo yonse yakuthengo idzadziwa kuti Ine ndine Yehova amene ndimafupikitsa mitengo yayitali ndi kutalikitsa mitengo yayifupi. Ndimawumitsa mitengo yabiriwiri ndi kubiriwitsa mitengo yowuma. “‘Ine Yehova ndayankhula zimenezi, ndipo ndidzazichita.’”

< Ezekiel 17 >