< Ezekiel 13 >

1 Again, the word of Yahweh came to me, saying,
Yehova anayankhulanso nane kuti,
2 “Son of man, prophesy against the prophets who are prophesying in Israel, and say to those who are prophesying out of their own imaginations, 'Listen to the word of Yahweh.
“Iwe mwana wa munthu unenere modzudzula aneneri a Israeli amene akunenera za kukhosi kwawo. Uwawuze iwowa kuti, ‘Imvani mawu a Yehova!’
3 The Lord Yahweh says this: Woe to the foolish prophets who follow their own spirit, but who have seen nothing!
Ambuye Yehova akuti, ‘Tsoka kwa aneneri opusa amene amangonenera zopeka ngakhale kuti sanaone kanthu konse!’
4 Israel, your prophets have been like jackals in the wastelands.
Iwe Israeli, aneneri ako ali ngati nkhandwe pa mabwinja.
5 You have not gone to the breaks in the wall around the house of Israel in order to repair it, in order to resist in battle on the day of Yahweh.
Simunakwere khoma kuti mukakonze mʼmene munagumuka, kuti Aisraeli adziteteze kolimba pa nkhondo pa tsiku la Yehova.
6 The people have false visions and make false predictions, those who say, “Such and such is Yahweh's declaration.” Yahweh has not sent them, but they nevertheless have made people hope that their messages would come true.
Masomphenya awo ndi achabe ndipo kuwombeza kwawo ndi kwabodza. Iwo amati, ‘Yehova akutero,’ pomwe Yehova sanawatume. Komabe iwo amayembekezera kuti zimene ayankhulazo zichitikadi.
7 Have you not had false visions and made false predictions, you who say, “Such and such is Yahweh's declaration” when I myself have not spoken?'
Koma Ine ndikuti masomphenya anu ngachabechabe ndi zimene mwawombedzazo nʼzabodza. Mumanena kuti, ‘Akutero Yehova,’ pamene sindinayankhule nʼkomwe.
8 Therefore the Lord Yahweh says this, 'Because you have had false visions and have told lies—therefore this is the Lord Yahweh's declaration against you:
“Tsono Ine Ambuye Wamphamvuzonse ndikukutsutsani chifukwa cha zoyankhula zanu zonama ndi masomphenya anu abodzawo. Ndikutero Ine Yehova.
9 My hand will be against the prophets who have lying visions and who make false predictions. They will not be in the assembly of my people, or enrolled in the record of the house of Israel; they must not go to the land of Israel. For you will know that I am the Lord Yahweh!
Ndidzalanga aneneri amene amanenera zabodza za zinthu zimene amati anaziona mʼmasomphenya. Sadzakhala nawo mʼbwalo la anthu anga ndipo mayina awo sadzalembedwa mu kawundula wa nzika za Israeli. Sadzalowa nawo mʼdziko la Israeli. Pamenepo mudzadziwa kuti Ine ndine Ambuye Yehova.
10 Because of this, and because they led my people astray and said, “Peace!” when there is no peace, they are building a wall that they will paint with whitewash.'
“Popeza kuti aneneri asocheretsa anthu anga pomanena kuti, ‘Kuli mtendere’ pamene mtendere palibe; ndiponso anthu akamanga khoma iwo nʼkumalipaka njereza,
11 Say to those who are whitewashing the wall, 'It will fall down; there will be a downpour of rain, and I will send hailstones to make it fall down, and a windstorm wind to break it down.
choncho ufotokozere amene alipaka njerezawo kuti khomalo lidzagwa. Mvula idzagwa mwamphamvu, kudzagwa matalala akuluakulu, ndipo kudzawomba mphepo yamkuntho.
12 See, the wall will fall down. Have others not said to you, “Where is the whitewash that you put on it?”
Pamene khomalo lagwa, kodi anthu sadzakufunsani kuti, ‘Kodi njereza yemwe munapaka uja ali kuti?’
13 Therefore the Lord Yahweh says this: I will bring a windstorm in my rage, and there will be floods of rain in my wrath! Hailstones in my rage will completely destroy it.
“Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti: Mwa ukali ndidzakunthitsa mphepo ya mkuntho. Ndidzagwetsa matalala akuluakulu ndili ndi ukali ndipo ndidzavumbwitsa mvula yamphamvu ndi mkwiyo mpaka khomalo litawonongeka kotheratu.
14 For I will tear down the wall that you have covered with whitewash, and I will demolish it to the ground and lay bare its foundations. So it will fall, and you will be annihilated in the middle of it all. Then you will know that I am Yahweh.
Ndidzagwetsa khoma limene munalipaka njerezalo. Ndidzaligumuliratu mpaka pansi kotero kuti maziko ake adzaoneka. Khomalo likadzagwa, inu mudzawonongekamo; ndipo mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
15 For I will annihilate in my fury the wall and those who whitewashed it. I will say to you, “The wall exists no more, nor do the people who whitewashed it—
Kotero ndidzagwiritsa ntchito mkwiyo wanga pa khomali ndi pa amene analipaka njereza. Pambuyo pake ndidzakuwuzani kuti, ‘Khoma lagwa pamodzi ndi amene analipaka njereza.
16 the prophets of Israel who prophesied about Jerusalem and who had visions of peace for her. But there is no peace!—this is the Lord Yahweh's declaration.”'
Agwanso aneneri a Yerusalemu amene ankalosa za Yerusalemu nʼkumati anaona mʼmasomphenya za mtendere wa Yerusalemu pamene mtendere kunalibe konse, akutero Ambuye Wamphamvuzonse.’
17 So you, son of man, set your face against the daughters of your people who prophesy out of their own minds, and prophesy against them.
“Tsono iwe mwana wa munthu, yankhulapo pa nkhani za akazi amene ali pakati pa anthu ako. Iwo amanenera zopeka za mʼmutu mwawo. Tsono adzudzule.
18 Say, 'The Lord Yahweh says this: Woe to the women who sew magic charms onto every part of their hand and make veils for their heads of every size, used to hunt down people. Will you hunt down my people but save your own lives?
Uwawuze kuti, ‘Ambuye Yehova akuti: Tsoka kwa akazi amene amasoka zithumwa zapamkono, amenenso amasoka nsalu za kumutu za anthu. Kodi mufuna kukola mitima ya anthu anga, inuyo nʼkupulumutsa moyo wanu?
19 You have profaned me among my people for handfuls of barley and crumbs of bread, to kill people who should not die, and to preserve the lives of those who should not continue to live, because of your lies to my people who heard you.
Ponamiza anthu anga amene amamva za mabodza anu, inu mwapha anthu amene sanayenera kufa ndipo mwasiya ndi moyo amene sanayenera kukhala ndi moyo.
20 Therefore the Lord Yahweh says this: I am against the magic charms that you have used to ensnare the people's lives as if they were birds. Indeed, I will tear them from your arms; and the people whom you have trapped like birds—I will let them go free.
“‘Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ine ndikudana ndi zithumwa zanu zimene mumakokera nazo mitima ya anthu ngati mbalame. Ndidzazingʼamba kudzichotsa pa mikono yanu. Choncho ndidzapulumutsa miyoyo ya anthu amene munawakola ngati mbalame.
21 I will tear away your veils and rescue my people from your hand, so they will no longer be trapped in your hands. You will know that I am Yahweh.
Ndidzangʼamba nsalu zanu za matsengazo ndi kupulumutsa anthu anga mʼmanja mwanu, ndipo simudzakhalanso ndi mphamvu yowakolera. Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
22 Because you discourage the heart of the righteous person with lies, even though I did not desire his discouragement, and because you encourage instead the actions of the wicked person so that he will not turn from his way to save his life—
Popeza kuti munatayitsa mtima anthu olungama ngakhale sindinafune kuti ataye mtima; ndipo munalimbitsa anthu oyipa kuti asaleka machimo awo motero sakutha kupulumutsa moyo wawo,
23 therefore you will no longer have false visions or continue to make predictions, for I will rescue my people out of your hand. You will know that I am Yahweh.'”
choncho inu simudzaonanso masomphenya abodza kapena kuwombeza. Ine ndidzapulumutsa anthu anga mʼmanja mwanu. Ndipo pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’”

< Ezekiel 13 >