< Exodus 11 >
1 Then Yahweh said to Moses, “There is still one more plague that I will bring on Pharaoh and Egypt. After that, he will let you go from here. When he finally lets you go, he will drive you away completely.
Tsopano Yehova anati kwa Mose, “Ine ndidzalanga Farao pamodzi ndi Aigupto onse ndi mliri umodzi wotsiriza. Zikadzachitika izi iye adzakulolani kuti mutuluke mʼdziko lino. Ndithu pamene azidzakutulutsani adzachita ngati akukuyingitsani.
2 Instruct the people that every man and woman is to ask of his or her neighbor for articles of silver and articles of gold.”
Awuze anthu kuti mwamuna aliyense ndi mkazi aliyense apemphe kwa mnansi wake ziwiya zasiliva ndi golide.”
3 Now Yahweh had made the Egyptians eager to please the Israelites. Moreover, the man Moses was very impressive in the sight of Pharaoh's servants and the people of Egypt.
Tsono Yehova anachititsa Aigupto kuti akomere mtima Aisraeli. Komanso Mose anali wotchuka kwambiri mʼdziko la Igupto, pamaso pa nduna za Farao ndi anthu onse.
4 Moses said, “Yahweh says this: 'About midnight I will go throughout Egypt.
Tsono Mose anawuza Farao kuti, “Pakati pa usiku, Yehova adzayenda pakati pa anthu a ku Igupto.
5 All the firstborn in the land of Egypt will die, from the firstborn of Pharaoh, who sits on his throne, to the firstborn of the slave girl who is behind the handmill grinding it, and to all the firstborn of the cattle.
Ndipo mwana aliyense wamwamuna wachisamba adzafa, kuyambira mwana wamwamuna wa Farao amene amakhala pa mpando waufumu, mpaka mwana wamwamuna wachisamba wa mdzakazi wake amene ali naye pa mtondo, komanso ana oyamba a ziweto.
6 Then there will be a great wailing throughout all the land of Egypt, such as has never been nor ever will be again.
Kudzakhala kulira kwakukulu mʼdziko lonse la Igupto, kumene sikunachitikepo ndipo sikudzachitikanso.
7 But not even a dog will bark against any of the people of Israel, against either man or beast. In this way you will know that I am treating the Egyptians and the Israelites differently.'
Koma pakati pa Aisraeli, ngakhale galu sadzawuwa munthu aliyense kapena chiweto!” Kotero mudzadziwa kuti Yehova ndiye wasiyanitsa pakati pa Igupto ndi Israeli.
8 All these servants of yours, Pharaoh, will come down to me and bow down to me. They will say, 'Go, you and all the people who follow you!' After that I will go out.” Then he went out from Pharaoh in great anger.
Nduna zanu zonse zidzabwera kwa ine, kugwada pamaso panga ndi kunena kuti, “Pita iwe ndi anthu ako onse amene akukutsatirawa! Zimenezi zikadzachitika ine ndidzachoka.” Ndipo Mose anachoka kwa Farao atakwiya kwambiri.
9 Yahweh said to Moses, “Pharaoh will not listen to you. This is so that I will do many amazing things in the land of Egypt.”
Yehova ananena kwa Mose kuti, “Farao adzakana kukumvera, kuti zodabwitsa zanga zichuluke mʼdziko la Igupto.”
10 Moses and Aaron did all these wonders before Pharaoh. But Yahweh hardened Pharaoh's heart, and Pharaoh did not let the people of Israel go out of his land.
Mose ndi Aaroni anachita zodabwitsa zonsezi pamaso pa Farao koma Yehova anawumitsa mtima wa Farao, ndipo sanalole kuti Aisraeli atuluke mʼdziko lake.