< Ecclesiastes 10 >
1 As dead flies cause perfume to stink, so a little folly can overpower wisdom and honor.
Monga ntchentche zakufa zimayika fungo loyipa mʼmafuta onunkhira, choncho kupusa pangʼono kumawononganso nzeru ndi ulemu.
2 The heart of a wise person tends to the right, but the heart of a fool tends to the left.
Mtima wa munthu wanzeru umamutsogolera bwino, koma mtima wa munthu wopusa umamusocheretsa.
3 When a fool walks down a road, his thinking is deficient, proving to everyone he is a fool.
Chitsiru ngakhale chikamayenda mu msewu, zochita zake ndi zopanda nzeru ndipo chimaonetsa aliyense kuti icho ndi chitsirudi.
4 If the emotions of a ruler rise up against you, do not leave your work. Calm can quiet down great outrage.
Ngati wolamulira akukwiyira, usachoke pa ntchito yako; kufatsa kumakonza zolakwa zazikulu.
5 There is an evil that I have seen under the sun, a kind of error that comes from a ruler:
Pali choyipa chimene ndinachiona pansi pano, kulakwitsa kumene kumachokera kwa wolamulira:
6 Fools are given leadership positions, while successful men are given low positions.
Zitsiru amazipatsa ntchito zambiri zapamwamba, pamene anthu olemera amawapatsa ntchito zotsika.
7 I have seen slaves riding horses, and successful men walking like slaves on the ground.
Ndaona akapolo atakwera pa akavalo, pamene akalonga akuyenda pansi ngati akapolo.
8 Anyone who digs a pit can fall into it, and whenever someone breaks down a wall, a snake can bite him.
Amene amakumba dzenje adzagwamo yekha; amene amabowola khoma adzalumidwa ndi njoka.
9 Whoever cuts out stones can be hurt by them, and the man who chops wood is endangered by it.
Amene amaphwanya miyala adzapwetekedwa ndi miyalayo; amene amawaza nkhuni adzapwetekedwa nazo.
10 If an iron blade is dull, and a man does not sharpen it, then he must use more strength, but wisdom provides an advantage for success.
Ngati nkhwangwa ili yobuntha yosanoledwa, pamafunika mphamvu zambiri potema, koma luso limabweretsa chipambano.
11 If a snake bites before it is charmed, then there is no advantage for the charmer.
Nʼkopanda phindu kudziwa kuseweretsa njoka ngati njokayo yakuluma kale.
12 The words of a wise man's mouth are gracious, but the lips of a fool consume him.
Mawu a pakamwa pa munthu wanzeru ndi okondweretsa, koma chitsiru chidzawonongedwa ndi milomo yake yomwe.
13 As words begin to flow from a fool's mouth, foolishness comes out, and at the end his mouth flows with wicked madness.
Chitsiru chimayamba ndi mawu opusa; potsiriza pake zoyankhula zake ndi zamisala
14 A fool multiplies words, but no one knows what is coming. Who knows what is coming after him?
ndipo chitsiru chimachulukitsa mawu. Palibe amene amadziwa zimene zikubwera mʼtsogolo, ndani angamuwuze zomwe zidzachitika iye akadzafa?
15 The toil of fools wearies them, so that they do not even know the road to town.
Chitsiru chimatopa msanga ndi ntchito yochepa; ndipo sichikhala ndi mphamvu zobwererera ku mudzi.
16 Woe to you, land, if your king is a young boy, and if your leaders begin feasting in the morning!
Tsoka kwa iwe, iwe dziko ngati mfumu yako ikali mwana, ndipo atsogoleri ako amakhala pa madyerero mmamawa.
17 But blessed are you, land, if your king is the son of nobles, and if your leaders eat at the right time, for strength, and not for drunkenness!
Wodala iwe, iwe dziko ngati mfumu yako ndi mwana wolemekezeka ndipo atsogoleri ako amadya pa nthawi yake, kuti apeze mphamvu osati kuti aledzere.
18 Because of laziness the roof sinks in, and because of idle hands the house leaks.
Ngati munthu ndi waulesi, denga lake limaloshoka; ngati manja ake ndi alobodo nyumba yake imadontha.
19 People prepare food for laughter, wine brings enjoyment to life, and money fills the need for everything.
Phwando ndi lokondweretsa anthu, ndipo vinyo ndi wosangalatsa moyo, koma ndalama ndi yankho la chilichonse.
20 Do not curse the king, not even in your mind, and do not curse rich people in your bedroom. For a bird of the sky might carry your words; whatever has wings can spread the matter.
Usanyoze mfumu ngakhale mu mtima mwako, kapena kutukwana munthu wachuma mʼchipinda chako, pakuti mbalame yamlengalenga itha kutenga mawu ako nʼkukafotokoza zomwe wanena.