< Deuteronomy 23 >

1 No man injured by crushing or cutting off may enter the assembly of Yahweh.
Mwamuna aliyense wofulidwa kapena woduka chiwalo chachimuna asalowe nawo mu msonkhano wa Yehova.
2 No illegitimate child may belong to the assembly of Yahweh; as far as to the tenth generation of his descendants, none of them may belong to the assembly of Yahweh.
Aliyense wobadwa mʼbanja losavomerezeka, kapena mdzukulu wake wina aliyense, ngakhale mibado khumi pambuyo pake, asalowe mu msonkhano wa Yehova.
3 An Ammonite or a Moabite may not belong to the assembly of Yahweh; as far as to the tenth generation of his descendants, none of them may belong to the assembly of Yahweh.
Mwamoni kapena Mmowabu asalowe mu msonkhano wa anthu a Yehova ngakhale mibado khumi yobwera pambuyo pake.
4 This is because they did not meet you with bread and with water on the road when you had come out of Egypt, and because they hired against you Balaam son of Beor from Pethor in Aram Naharaim, to curse you.
Pakuti iwowa sanabwere kudzakulonjerani ndi chakudya kapena madzi pamene mumadutsa pochokera ku Igupto, mʼmalo mwake anakalemba ganyu Balaamu mwana wa Beori wochokera ku Petori ku Mesopotamiya kuti akutemberereni.
5 But Yahweh your God would not listen to Balaam; instead, Yahweh your God turned the curse into a blessing for you, because Yahweh your God loved you.
Komabe Yehova Mulungu wanu sanamvere Balaamu koma anatembenuza temberero kukhala dalitso kwa inu chifukwa Yehova Mulungu wanu amakukondani.
6 You must never seek their peace or prosperity, during all your days.
Musachite nawo mgwirizano uliwonse wa mtendere pa moyo wanu wonse.
7 You must not detest an Edomite, for he is your brother; you must not abhor an Egyptian, because you were a foreigner in his land.
Musapeputse Mwedomu pakuti ndi mʼbale wanu ndithu. Musapeputse Mwigupto chifukwa munali alendo mʼdziko lake.
8 The descendants of the third generation that are born to them may belong to the assembly of Yahweh.
Mʼbado wachitatu wa ana awo akhoza kulowa mu msonkhano wa anthu a Yehova.
9 When you march out as an army against your enemies, then you must keep yourselves from every evil thing.
Mukamakhala pa msasa pokonzekera adani anu, musayandikane ndi china chilichonse chodetsedwa.
10 If there is among you any man who is unclean because of what happened to him at night, then he must go out of the army's camp; he must not come back into the camp.
Wina mwa asilikali anu akadziwonongera ndi umuna usiku, ayenera kuchoka pa msasapo ndipo akhale kunja kwa msasa.
11 When evening comes, he must bathe himself in water; when the sun goes down, he will come back inside the camp.
Koma dzuwa likapendeka ayenera kusamba ndipo polowa dzuwa akhoza kubwerera ku msasa.
12 You must have a place also outside the camp to which you will go;
Mukonze malo kunja kwa msasa kumene mukhoza kukadzithandizirako.
13 and you will have something among your tools to dig with; when you squat down to relieve yourself, you must dig with it and then put back the earth and cover up what has come out from you.
Pakati pa zida zanu muzikhala ndi china chokumbira, ndipo pokadzithandiza muzikumba kadzenje ndi kukwirira chimbudzi chanu.
14 For Yahweh your God walks in the midst of your camp to give you victory and to give your enemies into your hand. Therefore your camp must be holy, so that he may not see any unclean thing among you and turn away from you.
Pakuti Yehova Mulungu wanu amayendayenda ku msasa wanu kukutchinjirizani ndi kupereka adani anu kwa inu. Nʼchifukwa chake msasa wanu uzikhala wopatulika kuti mwina angaone china chonyansa nabwerera osakuyandikirani.
15 You must not give back to his master a slave who has escaped from his master.
Ngati kapolo wathawa mbuye wake nakabisala kwanu, musamuperekenso kwa mbuye wakeyo.
16 Let him live with you, in whatever town he chooses. Do not oppress him.
Mumulole akhale pakati panu, paliponse pamene angakonde, mʼmudzi umene angasankhe ndipo musamupondereze.
17 There must be no cultic prostitute among any of the daughters of Israel, neither must there be a cultic prostitute among the sons of Israel.
Pasapezeke Mwisraeli wamwamuna kapena wamkazi wochita chiwerewere ku Nyumba ya Mulungu.
18 You must not bring the wages of a prostitute or the wages of a dog into the house of Yahweh your God for any vow; for both these are abominations to Yahweh your God.
Musabweretse malipiro a wachiwerewere wamkazi kapena wamwamuna Mʼnyumba ya Yehova Mulungu wanu kudzapereka za malumbiro aliwonse, chifukwa Yehova Mulungu wanu amadana ndi zimenezi.
19 You must not lend on interest to your fellow Israelite—interest of money, interest of food, or the interest of anything that is lent on interest.
Musamalipitse mʼbale wanu chiwongoladzanja, kaya pa ndalama, kapena pa chakudya, kapena pa china chilichonse choti nʼkupereketsa chiwongoladzanja.
20 To a foreigner you may lend on interest; but to your fellow Israelite you must not lend on interest, so that Yahweh your God may bless you in all that you put your hand to, in the land which you are going in to possess.
Mlendo mukhoza kumulipitsa chiwongoladzanja koma osati mʼbale wanu Mwisraeli, kuti Yehova Mulungu wanu akudalitseni pa zochitika zanu zonse mʼdziko mukulowamoli.
21 When you make a vow to Yahweh your God, you must not be slow in fulfilling it, for Yahweh your God will surely require it of you; it would be sin for you not to fulfill it.
Mukalumbira kupereka kanthu kwa Yehova Mulungu wanu, musamachedwetse kupereka, chifukwa Yehova Mulungu wanu adzakufunsanibe kanthuko ndipo mudzapezeka wochimwa.
22 But if you will refrain from making a vow, it will be no sin for you.
Koma ngati mupewa kupanga mapangano simudzapezeka ochimwa.
23 That which has gone out from your lips you must observe and do; according as you have vowed to Yahweh your God, anything that you have freely promised with your mouth.
Zilizonse zimene mulumbira ndi pakamwa panu muzitsimikiza kuzichita, chifukwa mwalumbira mwaufulu pamaso pa Yehova Mulungu wanu ndi pakamwa panu.
24 When you go into your neighbor's vineyard, you may eat as many grapes as you desire, but do not put any in your basket.
Mukalowa mʼmunda wamphesa wa mnzanu mukhoza kudya mphesa mmene mungafunire koma musayike zina mʼdengu mwanu.
25 When you go into your neighbor's ripe grain, you may pluck the heads of grain with your hand, but do not put a sickle to your neighbor's ripe grain.
Mukalowa mʼmunda wa tirigu wa mʼbale wanu, mukhoza kutengako ngala mʼmanja mwanu, koma osasenga tirigu ndi chikwakwa.

< Deuteronomy 23 >