< Acts 10 >
1 Now there was a certain man in the city of Caesarea, Cornelius by name, a centurion of what was called the Italian Regiment.
Ku Kaisareya kunali munthu wina dzina lake Korneliyo, mkulu wa asilikali 100 wa gulu la Italiya.
2 He was a devout man, one who worshiped God with all his household; he gave much money to those in need, and he constantly prayed to God.
Iye ndi banja lake lonse amapembedza ndi kuopa Mulungu. Iye amathandiza osowa mowolowamanja ndipo amapemphera kwa Mulungu nthawi zonse.
3 About the ninth hour of the day, he clearly saw in a vision an angel of God coming to him. The angel said to him, “Cornelius!”
Tsiku lina, nthawi ili ngati 3 koloko masana, anaona masomphenya. Anaona bwino ndithu mngelo wa Mulungu, amene anabwera kwa iye ndi kuti, “Korneliyo.”
4 Cornelius stared at the angel and was very frightened and said, “What is it, sir?” The angel said to him, “Your prayers and your gifts to the poor have gone up as a memorial offering into God's presence.
Korneliyo anamuyangʼanitsitsa mngeloyo mwa mantha. Iye anafunsa kuti, “Nʼchiyani kodi Ambuye?” Mngelo anayankha kuti, “Mapemphero ako ndi zachifundo zako zafika pamaso pa Mulungu ngati chikumbutso.
5 Now send men to the city of Joppa to bring a man named Simon who is called Peter.
Tsopano tuma anthu apite ku Yopa kuti akayitane munthu dzina lake Simoni Petro.
6 He is staying with a tanner named Simon, whose house is by the seaside.”
Iye akukhala ndi Simoni mmisiri wa zikopa, amene nyumba yake ili mʼmbali mwa nyanja.”
7 When the angel who spoke to him had left, Cornelius called two of his house servants, and a devout soldier from among those who served him.
Mngeloyo anayankhula naye anachoka, Korneliyo anayitana antchito ake awiri ndiponso msilikali mmodzi wa iwo amene ankamutumikira yemwe ankapembedza Mulungu.
8 Cornelius told them all that had happened and sent them to Joppa.
Iye anawafotokozera zonse zimene zinachitika ndipo anawatuma kuti apite ku Yopa.
9 Now on the next day at about the sixth hour, as they were on their journey and were approaching the city, Peter went up upon the housetop to pray.
Mmawa mwake, nthawi ili ngati 12 koloko anthuwo atayandikira mzindawo, Petro anakwera pa denga kukapemphera.
10 He then became hungry and wanted something to eat, but while the people were cooking some food, he was given a vision,
Iye anamva njala ndipo anafuna chakudya, ndipo akukonza chakudyacho, iye anachita ngati wakomoka.
11 and he saw the sky open and a certain container descending, something like a large sheet coming down to the earth, let down by its four corners.
Iye anaona kuthambo kutatsekuka, ndi chinthu china chikutsitsidwa pansi chooneka ngati chinsalu chachikulu chomangidwa pa msonga zake zinayi.
12 In it were all kinds of four-footed animals and things that crawled on the earth, and birds of the sky.
Mʼmenemo munali nyama zonse zamiyendo inayi pamodzinso ndi zokwawa za dziko lapansi ndiponso mbalame zamlengalenga.
13 Then a voice spoke to him: “Rise, Peter, kill and eat.”
Petro anamva mawu akuti, “Petro, dzuka, ipha nudye.”
14 But Peter said, “Not so, Lord; for I have never eaten anything that was defiled and unclean.”
Petro anayankha kuti, “Ayi, Ambuye! Ine sindinadyepo kanthu kosayeretsedwa kapena konyansa.”
15 But the voice came to him again a second time: “What God has cleansed, do not call it defiled.”
Petro anamvanso kachiwiri mawu akuti, “Usachiyese chonyansa chimene Mulungu wachiyeretsa.”
16 This happened three times; then the container was immediately taken back up into the sky.
Zimenezi zinachitika katatu ndipo nthawi yomweyo chinsalu chija chinatengedwanso kupita kumwamba.
17 Now while Peter was very confused about what the vision that he had seen could mean, behold, the men who were sent by Cornelius stood before the gate, after they had asked their way to the house.
Petro akuganizira za tanthauzo la masomphenyawo, anthu amene Korneliyo anawatuma anapeza kumene kunali nyumba ya Simoni ndipo anayima pa chipata.
18 They called out and asked whether Simon, who was also called Peter, was staying there.
Iwo anayitana nafunsa ngati Simoni amene amadziwika ndi dzina loti Petro amakhala kumeneko.
19 While Peter was still thinking about the vision, the Spirit said to him, “Behold, three men are looking for you.
Petro akuganizirabe za masomphenyawo, Mzimu Woyera anati kwa iye, “Simoni, anthu atatu akukufunafuna.
20 Arise and go down and go with them. Do not hesitate to go with them, because I have sent them.”
Dzuka, tsika. Usakayike upite nawo pakuti ndawatuma ndine.”
21 So Peter went down to the men and said, “I am he whom you are seeking. Why have you come?”
Petro anatsika ndipo anati kwa anthuwo, “Amene mukufunayo ndine. Mwabwera kuno chifukwa chiyani?”
22 They said, “A centurion named Cornelius, a righteous man and one who worships God, and is well spoken of by all the nation of the Jews, was told by a holy angel of God to send for you to come to his house, so he could listen to a message from you.”
Anthuwo anayankha kuti, “Ife tachokera kwa Korneliyo, mkulu woyangʼanira asilikali 100. Iye ndi munthu wolungama ndiponso woopa Mulungu, amene amalemekezedwa ndi Ayuda onse. Mngelo woyera anamuwuza kuti mupite ku nyumba yake kuti akamve mawu amene inu mukanene.”
23 So Peter invited them to come in and stay with him. On the next morning he got up and went with them, and some of the brothers from Joppa accompanied him.
Pamenepo Petro anawalowetsa mʼnyumba ndipo anawasamala ngati alendo ake. Mmawa mwake Petro ananyamuka napita nawo ndipo abale ena a ku Yopa anapita naye pamodzi.
24 On the following day they came to Caesarea. Cornelius was waiting for them; he had called together his relatives and his close friends.
Tsiku linalo Petro anafika ku Kaisareya. Korneliyo anawadikirira ndipo anali atawasonkhanitsa pamodzi abale ake ndi abwenzi ake a pamtima.
25 It came about that when Peter entered, Cornelius met him and fell down at his feet to worship him.
Petro akulowa mʼnyumba, Korneliyo anakumana naye ndipo anadzigwetsa pa mapazi ake namulambira.
26 But Peter helped him up, saying, “Stand up! I too am a man.”
Koma Petro anamuyimiritsa nati, “Imirira, inenso ndine munthu ngati iwe.”
27 While Peter was talking with him, he went in and found many people gathered together.
Akuyankhula naye, Petro analowa mʼnyumba ndipo anapeza gulu lalikulu la anthu litasonkhana.
28 He said to them, “You yourselves know that it is not lawful for a Jewish man to associate with or to visit someone from another nation. But God has shown me that I should not call any man defiled or unclean.
Iye anawawuza kuti, “Inu mukudziwa bwino kuti ndi kutsutsana ndi lamulo ngati Myuda ayanjana ndi Mkunja kapena kuyendera wina aliyense wa mtundu wina. Koma Mulungu wandionetsa ine kuti ndisatchule munthu aliyense kuti ndi wosayenera kapena wonyansa.
29 That is why I came without arguing, when I was sent for. So I ask you why you sent for me.”
Nʼchifukwa chake ndabwera mosawiringula pamene munandiyitana. Tsopano ndikufunseni,” Mwandiyitanira chiyani?
30 Cornelius said, “Four days ago at this very hour, I was praying at the ninth hour in my house; and see, a man stood before me in bright clothing.
Komeliyo anayankha kuti, “Masiku anayi apitawo, nthawi yonga yomwe ino, 3 koloko masana ndimapemphera mʼnyumba mwanga. Mwadzidzidzi patsogolo panga panayimirira munthu wovala zovala zonyezimira.
31 He said, 'Cornelius, your prayer has been heard by God, and your gifts to the poor have reminded God about you.
Ndipo anati, ‘Korneliyo, Mulungu wamva mapemphero ako ndipo wakumbukira mphatso zako kwa osauka.
32 So send someone to Joppa, and call to you a man named Simon who is called Peter. He is staying in the house of a tanner named Simon, by the seaside.'
Tuma anthu ku Yopa akayitane Simoni wotchedwa Petro. Iye akukhala mʼnyumba ya Simoni mmisiri wazikopa amene amakhala mʼmbali mwa nyanja.’
33 So at once I sent for you. You are kind to have come. Now then, we are all here present in the sight of God, to hear everything that you have been instructed by the Lord to say.”
Nʼchifukwa chake ndinatumiza anthu nthawi yomweyo ndipo mwachita bwino kuti mwabwera. Tsopano ife tonse tili pano pamaso pa Mulungu kuti timve zonse zimene Ambuye akukulamulani kuti mutiwuze ife.”
34 Then Peter opened his mouth and said, “Truly, I perceive that God does not take anyone's side.
Ndipo Petro anayamba kuyankhula nati, “Zoonadi, tsopano ndazindikira kuti Mulungu sakondera.
35 Instead, in every nation anyone who worships and does righteous deeds is acceptable to him.
Koma amalandira anthu a mtundu uli wonse amene amaopa Iye ndiponso kuchita chilungamo.
36 You know the message that he sent to the people of Israel, when he announced good news about peace through Jesus Christ, who is Lord of all—
Uwu ndi uthenga umene Mulungu anatumiza kwa Aisraeli, kulalikira Uthenga Wabwino wamtendere mwa Yesu Khristu amene ndi Ambuye wa onse.
37 you yourselves know the events that took place, which occurred throughout all Judea, beginning in Galilee, after the baptism that John announced;
Inu mukudziwa zimene zinachitika ku Yudeya konse, kuyambira ku Galileya pambuyo pa ubatizo umene Yohane analalikira,
38 the events concerning Jesus of Nazareth, how God anointed him with the Holy Spirit and with power. He went about doing good and healing all who were oppressed by the devil, for God was with him.
kuti Mulungu, anamudzoza Yesu, wa ku Nazareti ndi Mzimu Woyera ndi mphamvu ndiponso mmene Iye anapita nachita zabwino ndi kuchiritsa onse amene anali pansi pa mphamvu ya mdierekezi, popeza kuti Mulungu anali naye.
39 We are witnesses of all the things Jesus did, both in the country of the Jews and in Jerusalem. They killed him by hanging him on a tree,
“Ife ndife mboni za zonse zimene anachita mʼdziko la Ayuda ndiponso ku Yerusalemu. Anamupha Iye pakumupachika pa mtengo,
40 but God raised him up on the third day and caused him to be seen,
koma Mulungu anamuukitsa kwa akufa pa tsiku lachitatu, ndipo analola kuti aonekere poyera.
41 not by all the people, but to the witnesses who were chosen beforehand by God—by us who ate and drank with him after he rose from the dead.
Iye sanaonekere kwa anthu onse koma kwa mboni zimene Mulungu anazisankhiratu, kwa ife amene timadya ndi kumwa naye atauka kwa akufa.
42 He commanded us to proclaim to the people and to testify that this is the one who has been chosen by God to be the Judge of the living and the dead.
Iye anatilamulira ife kuti tilalikire kwa anthu ndi kuchitira umboni kuti Iye ndiye amene Mulungu anamusankha kukhala woweruza wa amoyo ndi akufa.
43 It is to him that all the prophets bear witness, so that everyone who believes in him shall receive forgiveness of sins through his name.”
Aneneri onse achitira Iye umboni kuti aliyense amene akhulupirira Iye amakhululukidwa machimo chifukwa cha dzina lake.”
44 While Peter was still saying these things, the Holy Spirit fell on all of those who were listening to his message.
Petro akuyankhulabe mawu amenewa, Mzimu Woyera unatsikira pa onse amene amamva uthengawo.
45 The people who belonged to the circumcision group of believers—all of those who came with Peter—were amazed, because the gift of the Holy Spirit was poured out also on the Gentiles.
Abale a mdulidwe omwe anabwera ndi Petro anadabwa kuona kuti mphatso ya Mzimu Woyera yapatsidwanso kwa anthu a mitundu ina.
46 For they heard these Gentiles speak in other languages and praising God. Then Peter answered,
Pakuti anamva iwo akuyankhula mʼmalilime ndi kuyamika Mulungu. Ndipo Petro anati,
47 “Can anyone keep water from these people so they should not be baptized, these people who have received the Holy Spirit as well as we?”
“Kodi alipo amene angawaletse anthu awa kubatizidwa mʼmadzi? Iwotu alandira Mzimu Woyera monga ifenso.”
48 Then he commanded them to be baptized in the name of Jesus Christ. Then they asked him to stay with them for several days.
Tsono iye analamula kuti abatizidwe mʼdzina la Yesu Khristu. Ndipo anthu aja anamupempha Petro kuti akhale nawo masiku angapo.