< 2 Samuel 15 >

1 It came about after this that Absalom prepared a chariot and horses for himself, with fifty men to run before him.
Patapita nthawi, Abisalomu anadzipezera galeta ndi akavalo pamodzi ndi amuna makumi asanu amene amathamanga patsogolo pake.
2 Absalom would get up early and stand beside the road leading to the city gate. When any man had a dispute to come to the king for judgment, Absalom called to him and said, “From what city have you come?” Then the man would answer, “Your servant is from one of the tribes of Israel.”
Iye amadzuka mmamawa ndi kuyima pa njira yopita ku chipata cha mzinda. Munthu wina aliyense akakhala ndi zodandaula zopita nazo kwa mfumu kuti akaweruze, Abisalomu amamuyitana iye ndi kumufunsa kuti, “Kodi ukuchokera ku limodzi mwa mafuko a Israeli?”
3 So Absalom would say to him, “Look, your case is good and right, but there is no one empowered by the king to hear your case.”
Kenaka Abisalomu amanena kwa iye kuti, “Taona, madandawulo ako ndi abwino ndi oyenera, koma palibe woyimira mfumu woti akumvere.”
4 Absalom added, “I wish that I were made judge in the land, so that every man who had any dispute or cause might come to me, and I would bring him justice!”
Ndipo Abisalomu amawonjezera kunena kuti, “Ine ndikanangosankhidwa kukhala woweruza mʼdziko muno bwenzi munthu aliyense amene ali ndi madandawulo kapena milandu akubwera kwa ine ndipo ndikanaonetsetsa kuti chilungamo chachitika.”
5 So it came about that when any man came to Absalom to honor him, Absalom would put out his hand and take hold of him and kiss him.
Ndipo nthawi zonse amati munthu akasendera pafupi ndi kumugwandira, Abisalomu amatambalitsa dzanja lake, kumuyimiritsa munthuyo ndi kupsompsona.
6 Absalom acted in this way to all Israel who came to the king for judgment. So Absalom stole the hearts of the men of Israel.
Abisalomu amachitira izi Aisraeli onse amene amabwera kwa mfumu kuti adzaweruzidwe ndipo Abisalomuyo anagwira mtima anthu a mu Israeli.
7 It came about at the end of four years that Absalom said to the king, “Please let me go and pay a vow that I have made to Yahweh in Hebron.
Patapita zaka zinayi Abisalomu anati kwa mfumu, “Loleni ndipite ku Hebroni kuti ndikakwaniritse lonjezo limene ndinachita kwa Yehova.
8 For your servant made a vow while I was living at Geshur in Aram, saying,' If Yahweh will indeed bring me again to Jerusalem, then I will worship Yahweh.'”
Pamene mtumiki wanu amakhala ku Gesuri ku Aramu, anachita lonjezo ili: ‘Ngati Yehova adzandibweretsadi ku Yerusalemu, ndidzapembedza Yehovayo mu Hebroni.’”
9 So the king said to him, “Go in peace.” So Absalom arose and went to Hebron.
Mfumu inati kwa iye, “Pita mu mtendere” Kotero iye anapita ku Hebroni.
10 But then Absalom sent spies throughout all the tribes of Israel, saying, “As soon as you hear the sound of the trumpet, then you must say, 'Absalom is king in Hebron.'”
Ndipo Abisalomu anatuma amithenga ake mwamseri kwa mafuko onse a Israeli kukanena kuti, “Mukangomva kulira kwa malipenga pamenepo munene kuti, ‘Abisalomu ndiye mfumu mu Hebroni.’”
11 With Absalom went two hundred men from Jerusalem, who were invited. They went in their innocence, not knowing anything that Absalom had planned.
Anthu 200 ochokera mu Yerusalemu anapita naye Abisalomu. Iwo anayitanidwa monga alendo ndipo anapita osadziwa chilichonse pa nkhaniyi.
12 While Absalom offered sacrfices, he sent for Ahithophel from his hometown of Giloh. He was David's counselor. Absalom's conspiracy was strong, for the people following Absalom were constantly increasing.
Pamene Abisalomu amapereka nsembe, iye anayitanitsanso Ahitofele Mgiloni, mlangizi wa Davide, wa ku Gilo, kotero kuwukiraku kunakula kwambiri, ndipo anthu otsatira Abisalomu anapitirira kuchuluka.
13 A messenger came to David saying, “The hearts of the men of Israel are following after Absalom.”
Munthu wina anabweretsa uthenga ndi kudzamuwuza Davide kuti, “Mitima ya Aisraeli onse ili pa Abisalomu.”
14 So David said to all his servants who were with him at Jerusalem, “Arise and let us flee, or none of us will escape from Absalom. Prepare to leave immediately, or he will quickly overtake us, and he will bring down disaster on us and attack the city with the edge of the sword.”
Ndipo Davide anati kwa akuluakulu ake amene anali mu Yerusalemu. “Bwerani! Tiyeni tithawe, mwina palibe adzapulumuke kwa Abisalomu. Tiyeni tichoke msanga, mwina iye adzabwera msanga ndi kutipitirira, nʼkuwononga ife ndi mzinda wathu ndi lupanga.”
15 The king's servants said to the king, “Look, your servants are ready to do whatever our master the king decides.”
Akuluakulu a mfumu anamuyankha kuti, “Antchito anu ndi okonzeka kuchita chilichonse chimene mbuye wathu mfumu mukufuna kuchita.”
16 The king left and all his family after him, but the king left ten women, who were concubines, to keep the palace.
Mfumu inanyamuka pamodzi ndi banja lake lonse. Koma iye anasiya azikazi khumi kuti azisamalira nyumba yaufumu.
17 After the king went out and all the people after him, they stopped at the last house.
Kotero mfumu inanyamuka pamodzi ndi anthu onse oyitsatira, ndipo anayima pamalo pena chapatalipo.
18 All his army marched with him, and before him went all the Kerethites, and all the Pelethites, and all the Gittites—six hundred men who had followed him from Gath.
Ankhondo ake onse anayamba kuyenda pamaso pa Davide, ndipo Akereti ndi Apeleti, pamodzinso ndi Agiti okwanira 600 amene anamutsata kuchokera ku Gati, nawonso anayenda pamaso pake.
19 Then the king said to Ittai the Gittite, “Why will you come with us? Return and stay with the king, for you are a foreigner and an exile. Return to your own place.
Mfumu inati kwa Itai Mgiti, “Nʼchifukwa chiyani iwe ukupita ndi ife? Bwerera ndipo ukakhale ndi mfumu Abisalomu. Iwe ndiwe mlendo munthu wothawa kwawo.
20 Since you just left yesterday, why should I make you wander all over with us? I do not even know where I am going. So return and take your fellow countrymen back. May loyalty and faithfulness go with you.”
Wangobwera dzulo lomweli, lero ndikutenge kuti uziyendayenda ndi ife, pamene ine sindikudziwa kumene ndikupita? Bwerera, ndipo tenga abale ako. Chifundo ndi kukhulupirika zikhale nawe.”
21 But Ittai answered the king and said, “As Yahweh lives, and as my master the king lives, surely in whatever place where my master the king goes, there also will your servant go, whether that means living or dying.”
Koma Itai anayankha mfumu kuti, “Pali Yehova wamoyo, kulikonse kumene mbuye wanga mfumu mudzakhala, kaya ndi moyo kapena imfa, mtumiki wanu adzakhala komweko.”
22 So David said to Ittai, “Go ahead and continue with us.” So Ittai the Gittite marched with the king, along with all his men and all the families who were with him.
Davide anati kwa Itai, “Tiye pita nafe” Kotero Itai Mgiti anayenda pamodzi ndi anthu ake ndi mabanja amene anali naye.
23 All the country wept with a loud voice as all the people passed by over the Kidron Valley, and as the king also himself crossed over. All the people traveled on the road toward the wilderness.
Anthu onse a madera ozungulira analira mofuwula pamene anthu onsewo amadutsa. Mfumunso inawoloka chigwa cha Kidroni, ndipo anthu onse anayenda kulowera ku chipululu.
24 Even Zadok with all the Levites, carrying the ark of the covenant of God, were present. They set the ark of God down, and then Abiathar joined them. They waited until all the people had passed by out of the city.
Zadoki anali nawonso, ndipo Alevi onse amene anali naye ananyamula Bokosi la Chipangano la Mulungu. Iwo anayika pansi Bokosi la Mulungulo ndipo Abiatara ankapereka nsembe mpaka pamene anthu onse anamaliza kutuluka mu mzinda.
25 The king said to Zadok, “Carry the ark of God back into the city. If I find favor in the eyes of Yahweh, he will bring me back here and show me again the ark and the place where he lives.
Kenaka mfumu inati kwa Zadoki, “Tenga Bokosi la Mulungu ubwerere nalo mu mzinda. Ngati ndidzapeza chifundo pamaso pa Yehova, adzandibweretsa kuti ndilionenso ndi malo ake okhalamo.
26 But if he says, 'I am not pleased with you,' look, here am I, let him do to me whatever seems good to him.”
Koma iye anati, ‘Akapanda kukondwera nane,’ chabwino, andichite chimene chimukomere.”
27 The king also said to Zadok the priest, “Are you not a seer? Return into the city in peace, and your two sons with you, Ahimaaz your son, and Jonathan son of Abiathar.
Mfumu inatinso kwa wansembe Zadoki, “Kodi siwe mlosi? Bwerera mu mzinda mwamtendere pamodzi ndi mwana wako Ahimaazi ndi Yonatani mwana wa Abiatara. Iwe ndi Abiatara tengani ana anu awiri.
28 See, I will wait at the fords of the Arabah until word comes from you to inform me.”
Ine ndidzadikira powolokera Yorodani ku chipululu mpaka nditalandira mawu ochokera kwa iwe ondiwuza mmene zilili zinthu.”
29 So Zadok and Abiathar carried the ark of God back into Jerusalem, and they stayed there.
Kotero Zadoki ndi Abiatara ananyamula Bokosi la Mulungu lija nabwerera nalo ku Yerusalemu, ndipo anakakhala kumeneko.
30 But David ascended barefoot and weeping up the Mount of Olives, and he had his head covered. Every man of the people who were with him covered his head, and they went up weeping as they walked.
Koma Davide anapitirira ndi kukakwera phiri la Olivi akupita nalira. Anafunda kumutu koma sanavale nsapato. Anthu onse amene anali naye anafundanso kumutu, ndipo nawonso amalira pamene amapita.
31 Someone told David saying, “Ahithophel is among the conspirators with Absalom.” So David prayed, “O Yahweh, please turn Ahithophel's advice into foolishness.”
Tsono Davide anamva kuti, “Ahitofele ali pakati pa anthu owukira pamodzi ndi Abisalomu.” Choncho Davide anapemphera, “Inu Yehova, musandutse uphungu wa Ahitofele ukhale uchitsiru.”
32 It came about that when David arrived at the top of the road, where God used to be worshiped, Hushai the Arkite came to meet him with his coat torn and earth on his head.
Davide atafika pamwamba pa phiri pomwe anthu ankapembedzerapo Mulungu, Husai Mwariki anadzakumana naye atangʼamba mkanjo wake ndi kudzithira fumbi kumutu.
33 David said to him, “If you travel with me, then you will be a burden to me.
Davide anati kwa iye, “Ngati iwe upite ndi ine, udzakhala chondilemetsa.
34 But if you return to the city and say to Absalom, 'I will be your servant, king, as I have been your father's servant in time past, so will I now be your servant,' then you will confuse Ahithophel's advice for me.
Koma ngati ubwerera ku mzinda ndi kukanena kwa Abisalomu kuti, ‘Inu mfumu ine ndidzakhala wantchito wanu.’ Mʼmbuyomu ndinali wantchito wa abambo anu koma tsopano ndidzakhala wantchito wanu. Ukatero udzandithandiza kulepheretsa malangizo a Ahitofele.
35 Will you not have the priests Zadok and Abiathar with you? So whatever you hear in the king's palace, you must tell it to Zadok and Abiathar the priests.
Kodi ansembe, Zadoki ndi Abiatara, sakukhala nawe kumeneko? Ukawawuze zonse zimene umamva mʼnyumba yaufumu.
36 See that they have there with them their two sons, Ahimaaz, Zadok's son, and Jonathan, Abiathar's son. You must send to me by their hand everything that you hear.”
Ana awo awiri, Ahimaazi wa Zadoki, ndi Yonatani mwana wa Abiatara ali nawo pamodzi, uzikawatuma kwa ine ndi china chilichonse chimene ukamve.”
37 So Hushai, David's friend, came into the city as Absalom arrived and entered into Jerusalem.
Ndipo Husai bwenzi la Davide anafika ku Yerusalemu pamene Abisalomu amalowa mu mzinda.

< 2 Samuel 15 >