< 2 Kings 24 >
1 In Jehoiakim's days, Nebuchadnezzar king of Babylon attacked Judah; Jehoiakim became his servant for three years. Then Jehoiakim turned back and rebelled against Nebuchadnezzar.
Pa nthawi ya ulamuliro wa Yehoyakimu, Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anadzathira nkhondo dzikolo ndipo Yehoyakimu anakhala pansi pa ulamuliro wake zaka zitatu. Koma kenaka anasintha maganizo ake nawukira Nebukadinezara.
2 Yahweh sent against Jehoiakim bands of Chaldeans, Arameans, Moabites, and Ammonites; he sent them against Judah to destroy it. This was in conformity with the word of Yahweh that had been spoken through his servants the prophets.
Yehova anatumiza magulu a Ababuloni, Aaramu, Amowabu ndi Aamoni, kudzathira nkhondo Yuda. Iye anawatumiza kudzawononga Yuda molingana ndi mawu amene Yehova ananeneratu kudzera mwa aneneri ake.
3 It was certainly at the mouth of Yahweh that this came on Judah, to remove them out of his sight, because of the sins of Manasseh, all that he did,
Ndithu, izi zinachitikira Yuda monga momwe Yehova analamulira nʼcholinga choti awachotse pamaso pake chifukwa cha machimo a Manase ndi zonse zimene anachita,
4 and also because of the innocent blood that he shed, for he filled Jerusalem with innocent blood. Yahweh was not willing to pardon that.
kuphatikizapo kukhetsa magazi a anthu osalakwa. Chifukwa iye anadzaza Yerusalemu ndi magazi a anthu osalakwa ndipo Yehova sanafune kumukhululukira.
5 As for the other matters concerning Jehoiakim, and all that he did, are they not written in the book of the events of the kings of Judah?
Ntchito zina za Yehoyakimu ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
6 Jehoiakim slept with his ancestors, and Jehoiachin his son became king in his place.
Yehoyakimu anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake. Ndipo Yehoyakini mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
7 The king of Egypt did not attack any more out of his land, because the king of Babylon had conquered all the lands that had been controlled by the king of Egypt, from the brook of Egypt to the Euphrates River.
Mfumu ya Igupto sinatulukenso mʼdziko lake chifukwa mfumu ya Babuloni inalanda mayiko onse kuchokera ku Mtsinje wa ku Igupto mpaka ku Mtsinje wa Yufurate.
8 Jehoiachin was eighteen years old when he began to reign; he reigned in Jerusalem three months. His mother's name was Nehushta; she was the daughter of Elnathan of Jerusalem.
Yehoyakini anakhala mfumu ali ndi zaka 18 ndipo analamulira mu Yerusalemu miyezi itatu. Amayi ake anali Nehusita mwana wa Elinatani wa ku Yerusalemu.
9 He did what was evil in the sight of Yahweh; he did all that his father had done.
Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova monga anachitira abambo ake.
10 At that time the army of Nebuchadnezzar king of Babylon attacked Jerusalem and besieged the city.
Nthawi imeneyo ankhondo a Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anabwera ku Yerusalemu nazinga mzindawo ndi misasa ya nkhondo
11 Nebuchadnezzar king of Babylon came to the city while his soldiers were besieging it,
ndipo Nebukadinezara anafika ku mzindawo pamene ankhondo ake anawuzinga.
12 and Jehoiachin the king of Judah went out to the king of Babylon, he, his mother, his servants, his princes, and his officers. The king of Babylon captured him in the eighth year of his own reign.
Yehoyakini mfumu ya Yuda pamodzi ndi amayi ake, atumiki ake, anthu ake olemekezeka ndiponso akuluakulu onse anadzipereka kwa mfumu ya ku Babuloni. Mfumu ya Babuloni inagwira Yoyakini ukapolo mʼchaka chachisanu ndi chitatu cha ufumu wake.
13 Nebuchadnezzar took out from there all the valuable things in the house of Yahweh, and those in the king's palace. He cut into pieces all the golden objects that Solomon king of Israel had made in the temple of Yahweh, as Yahweh had said would happen.
Monga ananenera Yehova, Nebukadinezara anachotsa chuma chonse cha mʼNyumba ya Yehova ndiponso cha mʼnyumba ya mfumu ndipo anatenga ziwiya zonse zagolide za ku Nyumba ya Yehova zimene Solomoni mfumu ya Israeli anapanga.
14 He took into exile all Jerusalem, all the leaders, and all the fighting men, ten thousand captives, and all the craftsmen and the smiths. No one was left except the poorest people in the land.
Anatenga anthu onse a mu Yerusalemu kupita nawo ku ukapolo. Akuluakulu onse pamodzi ndi anthu ankhondo, anthu onse aluso ndi amisiri osula onse pamodzi analipo 10,000. Osauka okha ndiye anatsala mʼdzikomo.
15 Nebuchadnezzar took Jehoiachin into exile at Babylon, as well as the king's mother, wives, officers, and the chief men of the land. He took them into exile from Jerusalem to Babylon.
Nebukadinezara anatenga Yehoyakini ngati kapolo kupita naye ku Babuloni. Mu Yerusalemu anatenganso amayi a mfumu, akazi ake, akuluakulu ake ndiponso anthu olemekezeka mʼdzikomo.
16 All the fighting men, seven thousand in number, and one thousand craftsmen and blacksmiths, all of them fit for fighting—the king of Babylon brought these men into exile at Babylon.
Mfumu ya Babuloni inatumizanso ku Babuloni anthu ankhondo 70,000, anthu amphamvu ndi okonzeka kupita ku nkhondo, anthu aluso ndi amisiri osula 1,000.
17 The king of Babylon made Mattaniah, Jehoiachin's father's brother, king in his place, and changed his name to Zedekiah.
Iye analonga ufumu Mataniya, malume wa Yoyakini mʼmalo mwake ndipo anasintha dzina lake kuti akhale Zedekiya.
18 Zedekiah was twenty-one years old when he began to reign; he reigned eleven years in Jerusalem. His mother's name was Hamutal; she was the daughter of Jeremiah from Libnah.
Zedekiya anakhala mfumu ali ndi zaka 21 ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 11. Amayi ake anali Hamutali mwana wa Yeremiya wa ku Libina.
19 He did what was evil in the sight of Yahweh; he did all that Jehoiakim had done.
Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova monga anachitira Yehoyakimu.
20 Through Yahweh's anger, all these events happened in Jerusalem and Judah, until he drove them out of his presence. Then Zedekiah rebelled against the king of Babylon.
Zonsezi zinachitikira Yerusalemu ndi Yuda chifukwa cha mkwiyo wa Mulungu ndipo pa mapeto pake anawachotsa pamaso pake. Ndipo Zedekiya anawukira mfumu ya Babuloni.