< 2 Chronicles 6 >

1 Then Solomon said, “Yahweh has said that he would live in thick darkness,
Pamenepo Solomoni anati, “Yehova anati adzakhala mʼmitambo yakuda;
2 but I have built you a lofty residence, a place for you to live in forever.”
ine ndakumangirani Nyumba yokongola kwambiri, malo woti muzikhalamo mpaka muyaya.”
3 Then the king turned around and blessed all the assembly of Israel, while all the assembly of Israel was standing.
Aisraeli onse ali chiyimire pomwepo, mfumu inatembenuka ndi kuwadalitsa.
4 He said, “May Yahweh, the God of Israel, be praised, who spoke to David my father, and has fulfilled it with his own hands, saying,
Ndipo inati, “Atamandike Yehova, Mulungu wa Israeli amene wachita ndi dzanja lake zimene analonjeza ndi pakamwa pake kwa Davide abambo anga. Pakuti Iye anati,
5 'Since the day that I brought my people out of the land of Egypt, I chose no city out of all the tribes of Israel in which to build a house, in order for my name to be there. Neither did I choose any man to be prince over my people Israel.
‘Kuyambira tsiku limene ndinatulutsa anthu anga ku Igupto, sindinasankhe mzinda wina uliwonse pa fuko lina lililonse la Aisraeli kuti kumeneko andimangire Nyumba kuti ndizikhalamo kapena munthu wina aliyense kuti akhale mtsogoleri wa Aisraeli anthu anga.
6 However, I have chosen Jerusalem, so that my name might be there, and I have chosen David to be over my people Israel.'
Koma tsopano ndasankha Yerusalemu kuti Dzina langa likhale kumeneko ndiponso ndasankha Davide kuti alamulire anthu anga Aisraeli.’
7 Now it was in the heart of David my father, to build a house for the name of Yahweh, the God of Israel.
“Abambo anga Davide anali ndi maganizo mu mtima mwawo oti amangire Nyumba Yehova Mulungu wa Israeli.
8 But Yahweh said to David my father, 'In that it was in your heart to build a house for my name, you did well for it to be in your heart.
Koma Yehova ananena kwa abambo anga Davide kuti, ‘Popeza zinali mu mtima mwako kumangira Nyumba dzina langa, unachita bwino kukhala ndi maganizo amenewa mu mtima mwakomo.
9 Nevertheless, you must not build the house; instead, your son, one who will come from your loins, will build the house for my name.'
Komatu si iwe amene udzamanga Nyumba ya Mulungu koma mwana wako, mwana amene iwe udzabereke. Iyeyo ndiye amene adzandimangire Nyumba.’
10 Yahweh has carried out the word that he had said, for I have arisen in the place of David my father, and I sit on the throne of Israel, as Yahweh promised. I have built the house for the name of Yahweh, the God of Israel.
“Yehova wasunga zimene analonjeza. Ine ndalowa mʼmalo mwa abambo anga Davide, ndipo tsopano ndili pa mpando waufumu wa Israeli, monga momwe Yehova analonjezera, ndipo ndamangira nyumba Dzina la Yehova Mulungu wa Israeli.
11 I have placed the ark there, in which is Yahweh's covenant, which he made with the people of Israel.”
Mʼmenemo ndayikamo Bokosi la Chipangano, mmene muli pangano la Yehova limene anapangana ndi ana a Israeli.”
12 Solomon stood before the altar of Yahweh in the presence of all the assembly of Israel, and spread out his hands.
Pamenepo Solomoni anayimirira patsogolo pa guwa lansembe la Yehova patsogolo pa gulu lonse la Aisraeli ndipo anakweza manja ake.
13 For he had made a bronze platform, five cubits long, five cubits wide, and three cubits high. He had placed it in the middle of the courtyard. He stood on it and knelt down before all the assembly of Israel, and then he spread out his hands toward the heavens.
Iyeyo anali atapanga nsanja yamkuwa, kutalika kwake kunali mamita awiri, mulifupi mwake munali mamita awiri, msinkhu wake unali mita imodzi ndi theka ndipo nsanjayo anayimika pakati pa bwalo lakunja. Iye anayimirira pa nsanjapo nagwada pamaso pa gulu lonse la Aisraeli ndipo anakweza manja ake kumwamba.
14 He said, “Yahweh, God of Israel, there is no God like you in the heavens or on the earth, who keeps covenant and steadfast love with your servants who walk before you with all their heart;
Iye anati, “Inu Yehova, Mulungu wa Israeli, palibe Mulungu wofanana nanu kumwamba kapena pa dziko. Inu amene mumasunga pangano ndi kuonetsa chikondi chosasinthika kwa atumiki anu amene amayenda pamaso panu ndi mtima wawo wonse.
15 you who have kept with your servant David my father, what you promised him. Yes, you spoke with your mouth and have fulfilled it with your hand, as it is today.
Inu mwasunga lonjezo lanu kwa abambo anga Davide, mtumiki wanu. Inde zimene munalonjeza ndi pakamwa panu, mwazikwaniritsa ndi manja anu monga mmene tikuonera lero lino.
16 Now then, Yahweh, God of Israel, carry out what you have promised to your servant David my father, when you said, 'You will not fail to have a man in my sight to sit on the throne of Israel, if only your descendants are careful to walk in my law, as you have walked before me.'
“Ndipo tsopano, Inu Yehova Mulungu wa Israeli, sungani zimene munalonjeza kwa abambo anga Davide, mtumiki wanu pamene munati, ‘Sudzasowa munthu wokhala pamaso panga pa mpando waufumu wa Israeli, ngati ana ako adzasamalira mayendedwe awo ndi kusunga malamulo anga monga iwe wachitira.’
17 Now then, Yahweh, God of Israel, let your word be confirmed, which you have spoken to your servant David.
Ndipo tsopano Inu Yehova, Mulungu wa Israeli, lolani kuti mawu anu akwaniritsidwe amene munalonjeza mtumiki wanu Davide.
18 But will God actually live with mankind on the earth? Look, the entire universe and heaven itself cannot contain you—how much less can this temple that I have built!
“Kodi Mulungu angakhaledi pa dziko lapansi ndi munthu? Mlengalenga ngakhale kumwamba kwenikweni sikungakukwaneni. Nanga kuli bwanji ndi Nyumba iyi imene ndamanga!
19 Yet please respect this prayer of your servant and his request, Yahweh my God; listen to the cry and prayer that your servant prays before you.
Koma Inu Yehova, Mulungu wanga, imvani pemphero ndi pembedzero la mtumiki wanu. Imvani kulira ndi pemphero la mtumiki wanu limene ndikupempha pamaso panu.
20 May your eyes be open toward this temple day and night, the place where you promised to put your name. May you listen to the prayer your servant prays toward this place.
Maso anu azikhala otsekuka kuyangʼana Nyumba ino usana ndi usiku, malo ano amene Inu munati mudzayikamo Dzina lanu, imvani pemphero la mtumiki wanu limene akupemphera pa malo ano.
21 So listen to the requests of your servant and of your people Israel when we pray toward this place. Yes, listen from the place where you live, from the heavens; and when you listen, forgive.
Imvani mapembedzero a mtumiki wanu ndi a anthu anu Aisraeli pamene akupemphera akuyangʼana malo ano. Imvani kumwambako, malo anu amene mumakhala; ndipo mukamva muzitikhululukira.
22 If a man sins against his neighbor and is required to swear an oath, and if he comes and swears an oath before your altar in this house,
“Munthu akalakwira mnzake, nawuzidwa kuti alumbire, akabwera kudzalumbira patsogolo pa guwa lansembe la Nyumba ino,
23 listen from the heavens and act. Judge your servants, condemning the guilty and bringing what he has done upon his own head. Declare the innocent not guilty and give to him according to his righteousness.
imvani kumwambako ndi kuchitapo kanthu. Weruzani atumiki anuwo, wochimwa mugamule kuti ndi wolakwa ndipo alangidwe chifukwa cha zimene wachita. Wosachimwa mugamule kuti wosalakwa, ndipo muonetse kusalakwa kwakeko.
24 When your people Israel are defeated by an enemy because they have sinned against you, if they turn back to you, confess your name, pray, and request forgiveness before you in this temple—
“Anthu anu Aisraeli akagonja kwa adani awo chifukwa akuchimwirani ndipo akatembenukira kwa Inu ndi kuvomereza Dzina lanu, kupemphera ndi kupembedzera pamaso panu mʼNyumba ino,
25 then please listen from the heavens and forgive the sin of your people Israel; bring them back to the land that you gave to them and to their ancestors.
pamenepo imvani kumwambako ndi kukhululukira tchimo la anthu anu Aisraeli ndi kuwabweretsa ku dziko limene munawapatsa iwo ndi makolo awo.
26 When the skies are shut up and there is no rain because the people have sinned against you—if they pray toward this place, confess your name, and turn from their sin when you have afflicted them—
“Pamene kumwamba kwatsekeka ndipo mvula sikugwa chifukwa anthu anu akuchimwirani, ndipo pamene apemphera akuyangʼana malo ano ndi kuvomereza Dzina lanu ndi kutembenuka kuchoka ku machimo awo chifukwa inu mwawalanga,
27 then listen in heaven and forgive the sin of your servants and of your people Israel, when you direct them to the good way in which they should walk. Send rain on your land, which you have given to your people as an inheritance.
pamenepo imvani kumwambako ndipo muwakhululukire atumiki anu, anthu anu Aisraeli. Aphunzitseni makhalidwe oyenera, ndipo gwetsani mvula mʼdziko limene munapereka kwa anthu anu monga cholowa chawo.
28 Suppose there is famine in the land, or suppose that there is disease, blight or mildew, locusts or caterpillars; or suppose that its enemies attack the city gates in their land, or that there is any plague or sickness—
“Pamene mʼdziko mwagwa njala kapena mliri, chinoni kapena chiwawu, dzombe kapena kapuchi, kapena pamene adani azungulira mzinda wawo wina uliwonse, kaya mavuto kapena matenda abwera,
29 and suppose then that prayers and requests are made by a person or by all your people Israel—each knowing the plague and sorrow in his own heart as he spreads out his hands toward this temple.
ndipo wina aliyense mwa Aisraeli akapemphera kapena kukudandaulirani, aliyense wa iwo akadziwa masautso ake ndi ululu wake, ndi kukweza manja awo kuloza Nyumba ino,
30 Then listen from heaven, the place where you live; forgive, and reward every person for all his ways; you know his heart, because you and you only know the hearts of human beings.
pamenepo imvani kumwambako, malo anu wokhalamo. Khululukani ndipo muchitire aliyense molingana ndi zonse zimene anachita popeza Inu mumadziwa mtima wake, (pakuti ndinu nokha amene mumadziwa mitima ya anthu),
31 Do this so that they may fear you, so that they may walk in your ways all the days that they live on the land that you gave to our ancestors.
motero iwo adzakuopani ndipo adzayenda mʼnjira zanu masiku onse amene adzakhale mʼdziko limene munalipereka kwa makolo athu.
32 As for the foreigner who does not belong to your people Israel, but who—because of your great name, your mighty hand, and your outstretched arm—comes and prays toward this house,
“Ndipo kunena za mlendo amene si mmodzi wa anthu anu Aisraeli, koma wabwera kuchokera ku dziko lakutali chifukwa cha dzina lanu lotchukali, ndiponso za dzanja lanu lamphamvu ndi lochita zazikulu, kudzapemphera akuyangʼana Nyumba ino,
33 then please listen from heaven, the place where you live, and do all that the foreigner asks of you, so that all the people of the earth may know your name and fear you, as do your own people Israel, and that they might know that this house I have built is called by your name.
pamenepo imvani kumwambako, malo anu okhalamo, ndipo muchite zonse zimene mlendoyo akukupemphani, kotero kuti anthu onse a dziko lapansi adziwe dzina lanu ndi kukuopani monga amachitira anthu anu Aisraeli, ndipo adziwe kuti nyumba ino imene ndakumangirani imadziwika ndi dzina lanu.
34 Suppose that your people go out to battle against their enemies, by whatever way you may send them, and suppose that they pray to you toward this city that you have chosen, and toward the house that I have built for your name.
“Anthu akapita ku nkhondo kukamenyana ndi adani awo, kulikonse kumene mungawatume, ndipo akapemphera moyangʼana mzinda uno umene mwausankha ndi Nyumba yanu imene ndakumangirani,
35 Then listen from the heavens to their prayer, their request, and help their cause.
pamenepo imvani kumwamba pemphero lawo ndi kupempha kwawo ndipo muwapulumutse.
36 Suppose they sin against you—since there is no one who does not sin—and suppose that you are angry with them and hand them over to the enemy, so that the enemy carries them away and takes them as captives to their land, whether distant or near.
“Pamene achimwira inu, pakuti palibe amene sachimwa, ndipo inu mwawakwiyira ndi kuwapereka kwa adani awo, amene awatenga ukapolo ku dziko lawo lakutali kapena pafupi.
37 Then suppose they realize they are in the land where they have been exiled, and suppose that they repent and seek favor from you in the land of their captivity. Suppose that they say, 'We have acted perversely and sinned. We have behaved wickedly.'
Ngati asintha mitima yawo ku dziko limene ali akapolo ndi kulapa ndi kukudandaulirani inu mʼdziko la ukapolo wawo ndi kunena kuti, ‘Ife tachimwa, tachita zolakwa ndipo tachita moyipa kwambiri.’
38 Suppose that they return to you with all their heart and with all their soul in the land of their captivity, where they took them as captives, and suppose that they pray toward their land, which you gave to their ancestors, and toward the city that you chose, and toward the house that I have built for your name.
Ndipo ngati atembenukira kwa inu ndi mtima ndi moyo wawo wonse mʼdziko lawo la ukapolo kumene anatengedwako ndi kupemphera moyangʼana dziko limene inu munalipereka kwa makolo awo, moyangʼana Nyumba yanu imene ndakumangirani;
39 Then listen from the heavens, the place where you live, to their prayer and to their requests, and help their cause. Forgive your people, who have sinned against you.
pamenepo imvani kumwamba, malo anu okhala, pemphero lawo ndi kudandaula kwawo, ndipo muwapulumutse. Ndipo mukhululukire anthu anu, amene akuchimwirani.
40 Now, my God, I beg you, let your eyes be open, and let your ears be attentive to the prayer that is made in this place.
“Tsono Inu Mulungu wanga, tsekulani maso anu ndi makutu anu kuti mumve mapemphero ochitikira pa malo ano.
41 Now then arise, Yahweh God, to your resting place, you and the ark of your strength. Let your priests, Yahweh God, be clothed with salvation, and let your saints rejoice in your goodness.
“Tsopano dzukani Inu Yehova Mulungu, ndipo bwerani ku malo anu ampumulo,
42 Yahweh God, do not turn the face of your anointed away from you. Keep in mind your acts of covenant loyalty for David, your servant.”
Inu Yehova Mulungu musamukane wodzozedwa wanu.

< 2 Chronicles 6 >